Afilipi 3 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 3:1-21

Osakhulupirira za Thupi

1Abale anga, ndikupitiriza kunena kuti, kondwani mwa Ambuye! Sizondivuta kuti ndilembenso mawu omwewo, ndipo zimenezi nʼzokuthandizani inuyo.

2Chenjerani ndi agalu amenewa, anthu ochita zoyipa, anthu amene amadula thupi lawo. 3Pakuti ochita mdulidwe weniweni ndife. Ife amene timatumikira Mulungu motsogozedwa ndi Mzimu. Ife amene timanyadira Khristu, ndipo sitidalira zinthu za thupi 4ngakhale kuti ineyo ndili ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupizo.

Ngati pali winanso amene akuganiza kuti ali ndi zifukwa zokwanira kudalira zinthu za thupi, ineyo ndili ndi zifukwa zoposa pamenepo. 5Ndinachita mdulidwe pa tsiku lachisanu ndi chitatu nditangobadwa. Ndine wa mtundu wa Israeli, wa fuko la Benjamini, Mhebri wa Ahebri, kunena za malamulo, ndinali Mfarisi. 6Kunena za changu changa, ndinkazunza mpingo. Kunena za chilungamo chopezeka chifukwa chotsata malamulo, ineyo ndinali wopanda cholakwa.

7Koma zonse zimene ndinkaziyesa zaphindu, tsopano ndikuziona kuti nʼzosapindulitsa chifukwa cha Khristu. 8Kuwonjeza pamenepo, ndikuziona zonse kuti nʼzopanda phindu poyerekeza ndi phindu lopambana la kudziwa Khristu Yesu Ambuye anga. Nʼchifukwa cha Yesuyo ndataya zinthu zonse ndipo ndikuziyesa zinyalala kuti ndipindule Khristu 9ndi kuti ndipezeke mwa Iyeyo, osati ndi chilungamo changa chobwera chifukwa chotsata malamulo, koma chimene chimabwera chifukwa chokhulupirira Khristu. Chilungamochi nʼchochokera kwa Mulungu, timachilandira mwachikhulupiriro. 10Ine ndikufuna kudziwa Khristu, ndithu, kudziwa mphamvu zake za kuuka kwa akufa. Ndikufuna kuyanjana naye mʼmasautso ake, kufanana naye pa imfa yake 11kuti nanenso ndidzaukitsidwe kwa akufa.

Kuthamanga Mpaka Kumapeto pa Mpikisano wa Liwiro

12Sikuti ndazipeza kale zonsezi, kapena kuti ndakhala kale wangwiro, koma ndikuthamangabe ndi kuyesetsa kuti ndipeze chimene Khristu Yesu anandiyitanira. 13Abale, sindidziyesera ndekha kuti ndachipeza kale chimenechi. Koma chinthu chimodzi chimene ndimachita, nʼkuyiwala zamʼmbuyo ndi kuthamangira molimbika zinthu zimene zili mʼtsogolo mwanga. 14Ndikuthamangira kokathera mpikisanowo kuti ndikalandire mphotho imeneyi kumwamba, imene Mulungu anandiyitanira mwa Khristu Yesu.

Kutsanzira Paulo

15Choncho ife tonse amene tili okhwima pa moyo wauzimu, tikhale ndi maganizo omwewa. Ndipo ngati pena ndi pena muli ndi maganizo osiyana ndi amenewa, pameneponso Mulungu adzakuwunikirani. 16Tiyeni ife tizikhala mogwirizana ndi zimene tinapeza kale basi.

17Abale, nonsenu pamodzi mudzinditsanzira ine, ndipo monga inu muli ndi chitsanzo, phunzirani kwa amene akukhala moyo motsatira momwe timakhalira. 18Pakuti monga ndakhala ndikukuwuzani kawirikawiri mʼmbuyomu, ndipo tsopano ndikunenanso ndi misozi kuti, anthu ambiri akukhala monga adani a mtanda wa Khristu. 19Mapeto awo ndi chiwonongeko, mulungu wawo ndi mimba zawo, ndipo ulemerero wawo ndi manyazi awo. Mtima wawo uli pa zinthu za dziko lapansi. 20Koma ife ndife nzika za kumwamba ndipo tikudikirira mwachidwi Mpulumutsi wochokera kumeneko, Ambuye Yesu Khristu. 21Iyeyo, ndi mphamvu imene imamuthandiza kukhazikitsa zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, adzasintha matupi athu achabewa kuti akhale ofanana ndi thupi lake la ulemerero.

Bibelen på hverdagsdansk

Filipperbrevet 3:1-21

Advarsel mod jødisk religiøsitet

1Venner, glæd jer over at tilhøre Herren! Jeg gentager gerne mig selv for at slå det helt fast for jer.

2Vogt jer for de ondskabsfulde mennesker blandt jøderne, der siger, at I skal omskæres for at høre med til Guds folk. 3Det er jo os, der er Guds folk, os, der tjener Gud i Åndens kraft og sætter al vores lid til, hvad Jesus Kristus har gjort for os og ikke til en religiøs baggrund og tradition.

4Skal vi endelig tale om religiøs baggrund, så er der næppe nogen, der har en bedre baggrund end mig. 5-6Jeg er født israelit og hører til Benjamins stamme. Alle mine forfædre er jøder, og jeg blev omskåret på ugedagen for min fødsel. Som farisæer var jeg fanatisk med hensyn til at overholde den jødiske lov, hvilket resulterede i, at jeg forfulgte de kristne. Jeg opfyldte alle reglerne til punkt og prikke.

7Men alt det, som jeg dengang mente, var så vældig værdifuldt, har jeg lært at regne for værdiløst på grund af Kristus. 8Ja, faktisk regner jeg alt det gamle for at være uden værdi, fordi jeg nu har noget langt bedre. Jeg har nemlig lært Jesus Kristus at kende som min Herre. Derfor har jeg taget afstand fra min tidligere religiøsitet og kasseret den som affald. 9Nu ønsker jeg kun at blive ét med Kristus. Jeg forsøger ikke længere at opnå Guds accept ved at prøve at overholde den jødiske lov, men sætter min lid til, hvad Kristus har gjort for mig. 10Derved kan jeg også blive ét med ham i hans lidelser og død og få del i den kraft, der oprejste ham fra de døde. 11Jeg ser jo frem til at genopstå fra de døde, ligesom han gjorde.

Hold målet for øje

12Jeg mener ikke, at jeg allerede har forstået det hele eller er blevet fuldkommen. Men jeg bliver ved med at arbejde hen mod det mål, som Kristus gav mig, da han i sin tid greb ind i mit liv. 13Kære venner, jeg mener som sagt ikke, at jeg har nået målet endnu, men jeg bestræber mig på ikke at se tilbage på det, der ligger bag mig, og kæmper i stedet frem mod det, der ligger foran. 14Jeg løber frem mod målet for at kunne modtage den himmelske sejrskrans, som Gud har kaldet os til gennem Jesus Kristus. 15Lad nu alle os, som er nået til åndelig modenhed, have samme indstilling. Og skulle der være et og andet, I ser anderledes på, så vil Gud åbenbare det for jer. 16Men lad os i alle tilfælde stå sammen og være enige, så langt som vi nu er nået i vores fælles forståelse.

17Følg mit eksempel, kære venner, og læg mærke til dem, der lever med os som forbillede. 18Mange gange har jeg sagt det, og jeg siger det igen med tårer i øjnene: Der er mange, som har taget afstand fra budskabet om Kristi forsoningsdød på korset. 19De går deres undergang i møde. De lever for at tilfredsstille deres lyster, sætter en ære i det, de burde skamme sig over, og er kun optaget af jordiske ting. 20Men vores fokus og hjemsted er i Himlen, hvorfra vi med længsel venter på, at vores Frelser, Jesus Kristus, skal vende tilbage. 21Han vil forvandle vores ufuldkomne, jordiske legemer og gøre dem lig sit eget fuldkomne, himmelske legeme ved den kraft, som gør ham til Herre over alle ting.