Afilipi 2 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 2:1-30

Kutsanzira Kudzichepetsa kwa Khristu

1Ngati muli ndi chilimbikitso chilichonse chifukwa cholumikizana ndi Khristu, ngati muli ndi chitonthozo chifukwa cha chikondi chake, ngati muli ndi mtima umodzi mwa Mzimu, ndipo ngati mumakomerana mtima ndi kuchitirana chifundo, 2tsono tsirizani chimwemwe changa pokhala amaganizo ofanana, achikondi chimodzimodzi, amodzi mu mzimu ndi acholinga chimodzinso. 3Musachite kalikonse ndi mtima odzikonda chabe kapena odzitukumula chabe. Koma khalani odzichepetsa ndipo aliyense aziona mnzake ngati womuposa iyeyo. 4Musamangofuna zokomera inu nokha koma aliyense azifuna zokomeranso ena.

5Pa ubale wanu wina ndi mnzake, mukhale ndi mtima wofanana ndi wa Khristu Yesu:

6Iyeyu, pokhala Mulungu ndithu,

sanatenge kufanana ndi Mulungu kukhala chinthu choyenera kuchigwiritsa.

7Koma anadzichepetsa kotheratu

nakhala ndi khalidwe ngati la kapolo

ndi kukhala munthu ngati anthu ena onse.

8Ndipo pokhala munthu choncho

anadzichepetsa yekha

ndipo anamvera mpaka imfa yake,

imfa yake ya pamtanda!

9Choncho Mulungu anamukweza Iye kukhala wapamwamba kwambiri,

ndipo anamupatsa dzina loposa dzina lina lililonse

10kuti pakumva dzina la Yesu, bondo lililonse limugwadire,

kumwamba ndi pa dziko lapansi ndi pansi pa dziko,

11ndipo lilime lililonse livomereze kuti Yesu Khristu ndi Ambuye

kuchitira ulemu Mulungu Atate.

Kuwala monga Nyenyezi

12Tsono, abwenzi anga okondedwa, monga mwakhala omvera nthawi zonse, osati pamene ndinali nanu pokha, koma tsopano koposa pamene ndili kutali. Pitirizani kugwira ntchito ya chipulumutso chanu mwa mantha ndi kunjenjemera, 13pakuti ndi Mulungu amene amagwira ntchito mwa inu kuti mufune ndi kuchita zimene zimamukondweretsa Iyeyo.

14Muzichita zonse mosawiringula kapena mosatsutsapo, 15kuti mukhale wopanda cholakwa ndi angwiro, ana a Mulungu wopanda cholakwika mu mʼbado uno wachinyengo ndi wosocheretsa. Mukatero mudzawala pakati pawo ngati nyenyezi zakumwamba 16powawuza mawu amoyo. Ndipo ine ndidzatha kunyadira pa tsiku la Khristu kuti sindinathamange kapena kugwira ntchito pachabe. 17Koma ngakhale ndikuthiridwa ngati nsembe ya chakumwa yoperekedwa pa nsembe ndi pa utumiki wochokera mʼchikhulupiriro chanu, ndine wokondwa ndi wosangalala pamodzi ndi inu nonse. 18Chomwechonso, inu khalani okondwa ndi osangalala nane pamodzi.

Timoteyo ndi Epafrodito

19Ngati Ambuye Yesu alola, ndikukhulupirira kuti ndidzamutuma Timoteyo msanga kwanuko, kuti mwina ndingadzasangalale ndikadzamva za moyo wanu. 20Ndilibenso wina monga iyeyu amene ali ndi chidwi chenicheni pa za moyo wanu. 21Pakuti aliyense amangofuna zokomera iye yekha osati zokomera Yesu Khristu. 22Koma inu mukudziwa kuti Timoteyo wadzionetsa yekha, chifukwa watumikira ndi ine pa ntchito ya Uthenga Wabwino monga mwana ndi abambo ake. 23Choncho ndikuyembekezera kumutuma msanga ndikangodziwa mmene zinthu zanga ziyendere. 24Ndipo ndikukhulupirira kuti Ambuye akalola ine mwini ndidzafikanso kwanuko posachedwapa.

25Koma ndikuganiza kuti nʼkofunika kuti ndikutumizireni mʼbale wanga Epafrodito, mtumiki mnzanga ndi msilikali mnzanga, amenenso ndi mtumiki wanu amene munamutumiza kuti adzandithandize pa zosowa zanga. 26Pakuti akukulakalakani nonsenu ndipo akusauka mu mtima chifukwa munamva kuti akudwala. 27Zoonadi ankadwala ndipo anatsala pangʼono kumwalira. Koma Mulungu anamuchitira chifundo, ndipo sanangomuchitira chifundo iye yekhayu komanso ine, kuti chisoni changa chisachuluke. 28Choncho khumbo langa lofulumiza kumutumiza lakula, kuti pamene mumuonenso musangalale komanso kuti nkhawa yanga ichepe. 29Mulandireni mwa Ambuye ndi chimwemwe chachikulu, ndipo anthu onga iyeyu muziwachitira ulemu. 30Iyeyu anatsala pangʼono kufa chifukwa cha ntchito ya Khristu, anayika moyo pa chiswe kuti akwaniritse thandizo limene inu simukanatha.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס השליח אל-הפיליפיים 2:1-30

1אם קיים עידוד הדדי כלשהו בין המאמינים, אם אתם אוהבים אותי עד כדי לרצות לעזור לי, אם יש בלבכם רחמים ואהדה, אם יש בעיניכם משמעות כלשהי לעובדה שאנו אחים באמונה וששוכן בנו אותו רוח הקודש, 2אזי דעו לכם שתגרמו לי שמחה אמיתית אם תאהבו איש את רעהו, אם לא תריבו זה עם זה, ואם תעבדו יחד בלב ובדעה אחת למען מטרה אחת.

3אל תהיו אנוכיים, ואל תנסו לעשות רושם על אחרים. היו ענווים, התחשבו באחרים והעריכו אותם יותר מאשר את עצמכם. 4אל תעסקו כל הזמן רק בעניינים שלכם, אלא התעניינו גם באנשים אחרים ובמעשיהם. 5התנהגו עם הזולת כמו שישוע התנהג איתנו: 6למרות שהיה בדמות אלוהים הוא לא דרש את זכויותיו כאלוהים, 7אלא הפשיט מעצמו את כוחו הרב, את ההוד והתהילה, ולבש דמות עבד הדומה לבן־אדם. 8הוא אף השפיל את עצמו כל־כך עד שבחר למות מוות בזוי על הצלב.

9על כן העלהו אלוהים למרומי השמים ונתן לו שם העולה בכבודו על כל שם אחר, 10כדי שבשם ישוע יכרעו כולם ברך וישתחוו לו בשמים, בארץ ומתחת לארץ, 11וכל אדם יודה שישוע הוא האדון, לכבודו של אלוהים האב.

12ידידי היקרים, כשהייתי אצלכם שמעתם בקולי תמיד. עתה כשאני רחוק מכם, אני מבקש שתמשיכו לעשות מעשים טובים שנובעים מישועתכם. שמעו בקול אלוהים ביראה עמוקה, והתרחקו מכל דבר העלול לא למצוא־חן בעיניו. 13כי אלוהים הוא פועל בכם לרצות להישמע לו, והוא גם עוזר לכם למלא את רצונו.

14עשו כל דבר ללא ויכוחים וללא תלונות, 15כדי שאיש לא יוכל לדבר נגדכם. עליכם לחיות חיים פשוטים, טהורים ותמימים, כמו בני אלוהים בתוך עולם של נוכלים ורמאים. עליכם להאיר ולזרוח ביניהם כקרני אור בחשכה, 16ולספר להם על דבר אלוהים – על דבר החיים! אם כך תנהגו, אתגאה בכם בשובו של המשיח אלינו, שכן עבודתי ביניכם לא הייתה לשווא.

17גם אם עלי לשפוך את דמי כנסך על קורבן אמונתכם, כלומר, אם יהיה עלי להקריב את חיי למענכם, אגיל ואשמח עם כל אחד מכם. 18גם אתם צריכים לשמוח איתי על כך.

19אם ירצה השם אשלח אליכם בקרוב את טימותיוס, וכשישוב מביקורו אשמח לשמוע מפיו מה נשמע אצלכם. 20הידעתם שטימותיוס מתעניין בכם יותר מכל אדם אחר? 21נראה שכל אחד אחר דואג רק לעצמו ולתוכניותיו, ולא לתוכניותיו של ישוע המשיח. 22אך מכירים אתם את טימותיוס. בכל הנוגע להפצת הבשורה על המשיח הוא כבן לי. 23אני מקווה לשלחו אליכם ברגע שאדע מה עומד לקרות לי כאן. 24אני בטוח שהאדון יאפשר לי לבקר אתכם בקרוב.

25חושבני כי בינתיים מוטב שאשלח אליכם חזרה את אפפרודיטוס. שלחתם אותו כדי שיעזור לי בענייני, והוא אמנם עזר לי. שנינו היינו ממש כאחים; עבדנו יחד ואף סבלנו יחד למען המשיח. 26עתה אני מחזירו הביתה, שכן הוא מתגעגע אליכם מאוד ומודאג מהעובדה ששמעתם כי היה חולה. 27הוא באמת היה חולה, ואפילו עמד למות! אולם אלוהים ריחם עליו וגם עלי – בחסכו ממני את הצער הזה שלא יתווסף לסבלי.

28אני רוצה מאוד להחזיר אליכם את אפפרודיטוס, שכן אני יודע עד כמה תשמחו לראותו, וגם אני אשמח ויוקל לי מאוד. 29קבלוהו באדון בשמחה רבה, והביעו את הוקרתכם והערכתכם, כי הוא סיכן את חייו למען עבודת המשיח, 30ואף עמד למות בעודו משתדל לעשות מה שאתם לא יכולתם לעשות, בגלל היותכם רחוקים ממני.