Afilipi 1 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 1:1-30

1Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu.

Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.

2Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.

Kuyamika ndi Pemphero

3Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu. 4Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe 5chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano. 6Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.

7Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu. 8Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.

9Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo, 10kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu. 11Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.

Maunyolo a Paulo Apititsa Mʼtsogolo Uthenga Wabwino

12Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino. 13Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu. 14Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.

15Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino. 16Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino. 17Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo. 18Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi.

Ndithu, ndidzapitirira kukondwera, 19pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe. 20Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa. 21Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu. 22Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa. 23Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri. 24Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu. 25Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro 26kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.

Moyo Woyenerana ndi Uthenga Wabwino

27Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino 28osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu. 29Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu. 30Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.

Słowo Życia

Filipian 1:1-30

Pozdrowienie

1Paweł i Tymoteusz, jako słudzy Chrystusa Jezusa, piszemy do wszystkich świętych w Filippi—wraz z przywódcami i ich pomocnikami. 2Niech Bóg, nasz Ojciec, i Pan, Jezus Chrystus, obdarzają was swoją łaską i pokojem!

Podziękowanie i modlitwa

3Za każdym razem, gdy was wspominam, dziękuję za was Bogu. 4Wszyscy jesteście obecni w moich modlitwach. 5Począwszy od dnia, w którym usłyszeliście dobrą nowinę, aż do dziś, jesteście bowiem wiernymi współpracownikami w głoszeniu jej innym ludziom. 6Jestem pewien, że Bóg, który rozpoczął w was to dobre dzieło, będzie je kontynuował aż do czasu powrotu Jezusa Chrystusa.

Miłość Pawła do Filipian

7Mam prawo tak o was myśleć, bo zajmujecie w moim sercu szczególne miejsce. Wszyscy wspieraliście mnie przecież, gdy byłem w więzieniu i gdy stawałem w obronie dobrej nowiny. 8A Bóg dobrze wie, jak bardzo za wami tęsknię—Jezus Chrystus wlał bowiem w moje serce ogromną miłość do was. 9Modlę się, aby również wasza miłość coraz bardziej wzrastała i aby prowadziła was do jeszcze większej duchowej wiedzy i rozeznania. 10Dzięki temu będziecie bowiem umieli wybierać to, co najlepsze, i będziecie czyści oraz nienaganni w dniu powrotu Chrystusa. 11On sprawi, że przez wasze prawe postępowanie oddacie chwałę i cześć Bogu.

Nic nie może zatrzymać dobrej nowiny

12Przyjaciele, pragnę abyście wiedzieli, że napotkane przeze mnie przeszkody tak naprawdę pomogły tylko w głoszeniu dobrej nowiny! 13Całe koszary i wszyscy dookoła wiedzą już, że zostałem uwięziony z powodu Chrystusa. 14Ponadto coraz większa grupa wierzących, zachęconych moją postawą, z odwagą głosi słowo Boże, nie bojąc się nawet więzienia. 15Są jednak i tacy, którzy mówią o Chrystusie dlatego, że zazdroszczą nam owoców naszej pracy. Wielu ma jednak zupełnie czyste motywy 16i opowiada ludziom o Jezusie z miłości do Niego. Oni dobrze wiedzą, że znalazłem się tu, aby bronić dobrej nowiny. 17Ci zaś, którzy mówią o Chrystusie powodowani zazdrością, nie mają szczerych zamiarów. Chcą bowiem przysporzyć mi jeszcze więcej cierpienia. 18Ale to jest bez znaczenia. Liczy się tylko to, że—szczerze czy nieszczerze—mówi się o Chrystusie! A z tego mogę się tylko cieszyć, 19bo wiem, że dzięki waszym modlitwom i pomocy Ducha Jezusa Chrystusa wszystko to przyczyni się do mojego uwolnienia.

20Jestem też przekonany, że niczego nie będę musiał się wstydzić. Wręcz przeciwnie! Jak zawsze, tak i teraz—żywy czy martwy—oddam chwałę Chrystusowi. 21Życie oznacza bowiem dla mnie służbę Chrystusowi, a śmierć—to czysty zysk! 22Jeśli więc mam pozostać przy życiu, to nadal będę Mu służył. Ale nie wiem, co wybrać, 23pragnę bowiem zarówno śmierci, jak i życia. Gdybym zakończył życie, to znalazłbym się już z Jezusem—a to jest coś, o czym marzę. 24Gdybym jednak pozostał przy życiu, to mógłbym jeszcze zrobić dla was wiele dobrego. 25A mam pewność, że tak właśnie się stanie—że zostanę jeszcze z wami, aby dbać o wasz duchowy wzrost i pomóc wam czerpać radość z wiary. 26Gdy się więc spotkamy, będziecie mogli być dumni z tego, że służę Jezusowi.

27Tymczasem postępujcie w sposób godny dobrej nowiny o Chrystusie. Chciałbym bowiem—niezależnie od tego, czy jestem z wami, czy nie—mieć pewność, że zachowujecie jedność, że wspólnie walczycie, głosząc dobrą nowinę, 28i że nie dajecie się zastraszyć przeciwnikom. Taka postawa będzie dla nich zapowiedzią zagłady, dla was zaś—zapowiedzią Bożego zbawienia. 29Bóg dał wam bowiem wielki przywilej—możecie nie tylko wierzyć Chrystusowi, ale także dla Niego cierpieć. 30Teraz więc przechodzicie te same cierpienia, które kiedyś widzieliście w moim życiu i o których zresztą nadal słyszycie.