Afilipi 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 1:1-30

1Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu.

Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.

2Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.

Kuyamika ndi Pemphero

3Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu. 4Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe 5chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano. 6Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.

7Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu. 8Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.

9Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo, 10kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu. 11Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.

Maunyolo a Paulo Apititsa Mʼtsogolo Uthenga Wabwino

12Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino. 13Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu. 14Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.

15Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino. 16Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino. 17Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo. 18Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi.

Ndithu, ndidzapitirira kukondwera, 19pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe. 20Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa. 21Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu. 22Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa. 23Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri. 24Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu. 25Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro 26kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.

Moyo Woyenerana ndi Uthenga Wabwino

27Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino 28osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu. 29Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu. 30Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.

Persian Contemporary Bible

فيليپیان 1:1-30

سلام و درود از پولس

1از طرف پولس و تيموتائوس، خدمتگزاران عيسی مسيح، به كشيشان و خدمتگزاران كليسا، و تمام مسيحيان راستين در شهر فيليپی.

2از درگاه پدرمان خدا و خداوندمان عيسی مسيح، طالب فيض و آرامش برای شما هستم.

شكرگزاری و دعای پولس

3هرگاه شما را به ياد می‌آورم، خدا را برای وجودتان سپاس می‌گويم. 4هر بار كه برای شما دعا می‌كنم، قلبم لبريز از شادی می‌گردد، 5زيرا شما از همان روزی كه پيغام انجيل را شنيديد تا به حال، كمكهای بسياری در اشاعه و گسترش آن نموده‌ايد. 6اطمينان دارم خدا كه اين عمل نيكو را در شما آغاز نمود، شما را ياری خواهد داد تا در فيض او رشد كنيد تا به هنگام بازگشت عيسی مسيح، كار او در شما تكميل شده باشد.

7اين طبيعی است كه دربارهٔ شما چنين احساسی داشته باشم، چون همهٔ شما در دل من جای داريد. چه، زمانی كه در زندان بودم و چه، زمانی كه آزادانه در ميان شما به سر می‌بردم، به اتفاق هم از حقيقت دفاع می‌كرديم و خبر نجات مسيح را به گوش مردم می‌رسانديم؛ به همين جهت همواره با هم در بركات خدا شريک بوده‌ايم. 8فقط خدا می‌داند كه عيسی مسيح چه محبت و اشتياق عميقی نسبت به شما در من گذاشته است.

9از اين رو، برای شما دعا می‌كنم كه محبتتان نسبت به ديگران روز‌به‌روز فزونی يابد و دانش و بينش روحانی‌تان نيز به حد كمال برسد، 10تا بتوانيد فرق ميان خوب و بد، و درست و نادرست را تشخيص دهيد. دعا می‌كنم كه زندگی‌تان چنان پاک گردد كه هيچكس نتواند تا زمان بازگشت خداوند ما مسيح، عيبی در شما بيابد. 11همچنين دعا می‌كنم كه همواره به اعمال نيكو بپردازيد، اعمالی كه باعث ستايش و جلال خداوند می‌گردند و نشان می‌دهند كه شما فرزند خدا هستيد.

شادی پولس برای بشارت انجيل مسيح

12برادران عزيز، می‌خواهم اين را نيز بدانيد كه آنچه برای من پيش آمده، در واقع به اشاعه و گسترش پيغام انجيل منجر شده است؛ 13زيرا اكنون همه، منجمله سربازان گارد، به خوبی می‌دانند كه من به علت مسيحی بودن، در زندان به سر می‌برم. 14به علاوه، زندانی بودن من باعث شده كه بسياری از مسيحيان اينجا، ديگر ترسی از زندان نداشته باشند؛ و صبر و تحمل من به آنان جرأت بخشيده كه با شهامت بيشتری پيغام مسيح را اعلام كنند.

15البته، بعضی به كاری كه خدا توسط من انجام می‌دهد، حسادت می‌ورزند و به همين علت می‌كوشند كه خودشان نيز انجيل را موعظه كنند؛ هدف ايشان از اين كار اينست كه مورد تشويق و توجه ديگران قرار گيرند. اما بعضی نيز انگيزه و هدفی خالص برای اين كار دارند؛ 16‏-17اينان مرا دوست دارند و پی برده‌اند كه خدا مرا برای دفاع از حقيقت به اينجا آورده است. عده‌ای هم برای اين موعظه می‌كنند كه حسادت مرا برانگيزند، با اين تصور كه پيشرفت كار آنان، غمی به غمهای من در زندان می‌افزايد. 18اما هر کس با هر انگيزه و هدفی انجيل را موعظه كند، باعث شادی من می‌شود، چون به هر حال پيغام نجاتبخش مسيح به گوش همه می‌رسد.

بلی، شادی من پايان نخواهد پذيرفت، 19زيرا می‌دانم تا زمانی كه شما برايم دعا می‌كنيد و روح‌القدس نيز مرا ياری می‌نمايد، تمام اين امور به نفع من تمام خواهد شد.

زندگی پولس برای مسيح

20آرزوی قلبی و اميد من اينست كه هرگز در انجام وظايف خود، شرمنده و سرافكنده نشوم، بلكه همواره آماده باشم تا در تمام سختيها با كمال دليری دربارهٔ مسيح سخن بگويم، همانطور كه در گذشته نيز چنين كرده‌ام؛ تا بدين وسيله، چه زنده باشم و چه بميرم، باعث سربلندی مسيح گردم. 21چون برای من، «زندگی» فرصتی است برای خدمت به مسيح، و «مرگ» به معنی رفتن به نزد او می‌باشد. 22اما اگر زنده ماندن من، سبب خواهد شد كه عدهٔ بيشتری را به سوی مسيح هدايت كنم، در اين صورت واقعاً نمی‌دانم كدام بهتر است، مردن يا زنده ماندن. 23گاه می‌خواهم زنده بمانم و گاه آرزو می‌كنم كه اين زندگی را ترک گويم و به نزد مسيح بشتابم، كه اين برای من خيلی بهتر است. 24اما در حقيقت اگر زنده بمانم، می‌توانم كمک بيشتری به شما بكنم. 25بلی، وجود من هنوز در اينجا لازم است؛ از این رو يقين دارم كه باز مدتی در اين دنيا خواهم ماند و به رشد و شادی شما در ايمان، كمک خواهم نمود. 26ماندن من، شما را شاد خواهد ساخت؛ و هنگامی كه نزد شما بيايم، مطمئنم او را تجليل خواهيد كرد كه مرا سالم نگاه داشته است.

زندگی در مقام شهروندان آسمان

27‏-28اما هر چه برای من پيش آيد، چه شما را بار ديگر ببينم، چه نبينم، به ياد داشته باشيد كه همواره بايد همچون مسيحی واقعی زندگی كنيد، تا هميشه خبرهای خوب دربارهٔ شما به من برسد و بشنوم كه دوش به دوش يكديگر، استوار ايستاده‌ايد و هدف همگی‌تان اينست كه بدون توجه به مخالفتهای دشمن، پيغام نجاتبخش انجيل را به همه اعلام كنيد. همين امر برای ايشان نشانهٔ هلاكت است، اما برای شما نشانهٔ اينست كه خدا با شماست و به شما زندگی جاويد عطا كرده است. 29زيرا خدا به شما اين افتخار را داده است كه نه فقط به او ايمان آوريد، بلكه در راه او متحمل زحمات و مشقات نيز بشويد. 30در اين مجاهده و پيكار، ما با يكديگر شريک می‌باشيم. شما در گذشته شاهد زحمات من در راه مسيح بوده‌ايد، و همانطور كه می‌دانيد هنوز هم درگير همان زحمات و مبارزات هستم.