Afilipi 1 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Afilipi 1:1-30

1Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu.

Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.

2Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.

Kuyamika ndi Pemphero

3Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu. 4Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe 5chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano. 6Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.

7Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu. 8Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.

9Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo, 10kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu. 11Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.

Maunyolo a Paulo Apititsa Mʼtsogolo Uthenga Wabwino

12Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino. 13Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu. 14Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.

15Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino. 16Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino. 17Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo. 18Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi.

Ndithu, ndidzapitirira kukondwera, 19pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe. 20Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa. 21Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu. 22Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa. 23Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri. 24Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu. 25Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro 26kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.

Moyo Woyenerana ndi Uthenga Wabwino

27Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino 28osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu. 29Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu. 30Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.

Bibelen på hverdagsdansk

Filipperbrevet 1:1-30

Indledende hilsen

1Kære ledere og medhjælpere i menigheden og alle i Filippi, som hører Jesus Kristus til. Dette brev er fra Paulus og Timoteus, Jesu Kristi tjenere. 2Nåde være med jer og fred fra Gud, vores Far, og Herren Jesus Kristus.

Taksigelse og bøn for filipperne

3-4Hver gang jeg tænker på jer, fyldes mit hjerte med glæde, og når jeg beder for jer, gør jeg det med tak til Gud. 5I har jo været med til at sprede det glædelige budskab om Kristus lige fra det øjeblik, I tog imod det, og I gør det stadig. 6Det var Gud, som begyndte sit gode værk i jer, og jeg er overbevist om, at han også vil fuldføre det. Han vil fortsat arbejde med jer indtil den dag, hvor Jesus Kristus kommer igen.

7Det er kun naturligt, at jeg tænker sådan om jer, for I har vist stor hengivenhed over for mig.1,7 Teksten kan enten forstås som: „jeg er hengiven over for jer” eller „I er hengivne over for mig”. Og I har stået sammen med mig, både når jeg har været i fængsel, og når jeg har forsvaret og begrundet det glædelige budskab om nåden. 8Gud ved, hvor meget jeg længes efter jer alle, og hvor højt jeg elsker jer med Jesu Kristi kærlighed.

9Jeg beder om, at jeres kærlighed må blive ved med at vokse, og at I må få stadig større åndelig forståelse og dømmekraft, 10så I kan skønne, hvad der er det væsentlige og træffe de rigtige valg. Jeg beder om, at I på dommens dag må kunne stå med en ren og uplettet samvittighed 11og med rige resultater af de gode gerninger, som Kristus har udført gennem jer til ære og pris for Gud.

Paulus’ fangenskab standser ikke forkyndelsen af Kristus

12Jeg er glad for at kunne fortælle jer, kære venner, at det, der er sket med mig, faktisk har bevirket, at budskabet om Kristus er nået endnu længere ud. 13Alle her omkring—og det gælder også soldaterne i garnisonen—er klar over, at jeg sidder i fængsel, fordi jeg tjener Kristus. 14Desuden har mit fangenskab givet mange af de kristne her større tillid til Gud, så de nu frimodigt forkynder Guds ord uden frygt.

15Selvom der er nogle, der taler om Kristus, fordi de er misundelige på mig og gerne vil skabe vanskeligheder for mig, er der andre, der har gode motiver. 16De sidstnævnte forkynder Ordet af kærlighed, og de ved, at jeg er her, fordi Herren har givet mig den opgave at forsvare budskabet om Jesus. 17De første derimod har ikke rene motiver, men taler om Kristus med baggrund i rivalisering og ønsker dermed at give mig endnu flere problemer her i fængslet. 18-19Men hvilket motiv de end har, så bliver det gode budskab om Kristus altså fortalt—og det vil jeg glæde mig over.

Jeg glæder mig også over, at I beder for mig, for jeg er sikker på, at ved jeres bøn og ved den hjælp, Jesu Kristi Ånd giver mig, vil jeg komme sejrrig igennem denne prøvelse. 20Det er mit håb og min faste overbevisning, at jeg ikke på nogen måde skal komme til at svigte Kristus, men at han nu som altid må blive æret ved, at jeg frimodigt forkynder det budskab, han har givet mig. Hvad enten jeg skal dø i tjenesten for ham, eller jeg får lov at leve, vil jeg altid ære ham. 21Så længe jeg lever, lever jeg for Kristus. Og når jeg dør, bliver det endnu bedre. 22Men siden der er gode resultater af mit arbejde her på jorden, ved jeg snart ikke, hvad jeg helst vil. 23På en måde foretrækker jeg at dø og derefter være sammen med Kristus, for det ville være herligt. 24Men så længe der endnu er brug for mig på jorden, er jeg parat til at blive. 25Derfor tror jeg også, at jeg skal blive her endnu en tid til glæde for jer og for at hjælpe jer til at vokse i troen. 26Når jeg så besøger jer en gang til, får I endnu mere grund til at lovprise Jesus Kristus for, hvad han udretter gennem min tjeneste.

Kæmp for troens sag

27Men hvad der end sker, så skal I leve på en sådan måde, at I ærer Kristus ved det. Hvad enten jeg kommer og besøger jer, eller jeg må nøjes med at høre om jer, forventer jeg, at I står side om side i samme ånd og kæmper for troens sag. 28I skal ikke være bange for, hvad jeres modstandere kan finde på at gøre. For dem er jeres tro jo et klart fingerpeg om, at de går fortabt, men at I vil få det evige liv. Det er alt sammen med i Guds plan. 29Af Guds nåde har I ikke alene fået lov at tro på Kristus, men I har også fået lov at lide for ham, 30mens I fortsat kæmper den samme kamp, som I engang så mig stå i, og som I nu hører, at jeg stadig står i.