Aefeso 6 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 6:1-24

Ana ndi Makolo Awo

1Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera. 2“Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo. 3Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.” 4Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.

Antchito ndi Mabwana Awo

5Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu. 6Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu. 7Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu. 8Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.

9Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.

Zida Zankhondo za Mulungu

10Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu. 11Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana. 12Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. 13Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu. 14Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa. 15Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato. 16Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo. 17Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu. 18Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.

19Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha. 20Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.

Mawu Otsiriza

21Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita. 22Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.

23Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse. 24Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.

Słowo Życia

Efezjan 6:1-24

Dzieci i rodzice

1Teraz kilka słów do was, dzieci: Bądźcie posłuszne rodzicom ze względu na Pana—bo tak należy postępować. 2-3„Szanuj rodziców, żeby ci się dobrze powodziło i abyś długo żył na ziemi!”—to pierwsze z dziesięciu przykazań, które zawiera obietnicę.

4Ojcowie, nie drażnijcie dzieci, ale wychowujcie je stosując dyscyplinę i nauczając je tego, co się podoba Panu.

Niewolnicy i panowie

5Niewolnicy, bądźcie posłuszni swoim panom—szczerze i z szacunkiem, jakbyście służyli samemu Chrystusowi. 6Nie róbcie tego na pokaz, aby się im przypodobać. Pracujcie tak, jakbyście byli niewolnikami samego Chrystusa, wypełniającymi Bożą wolę z potrzeby serca. 7Powtarzam: Służcie z zapałem, jakbyście czynili to dla Pana, a nie tylko dla ludzi. 8Pamiętajcie, że wszyscy—zarówno niewolnicy, jak i wolni—zostaną nagrodzeni przez Pana za ich dobre czyny.

9Wy zaś, panowie, traktujcie niewolników we właściwy sposób. Nie zmuszajcie ich do niczego groźbą i pamiętajcie, że w niebie zasiada wasz wspólny Pan. On traktuje wszystkich ludzi jednakowo.

Boża zbroja

10Na koniec—kilka słów zachęty: Korzystajcie z mocy naszego Pana, a wtedy również wy będziecie mocni. 11Załóżcie całą zbroję otrzymaną od Boga, abyście mogli odeprzeć podstępne ataki diabła. 12Nie walczymy bowiem z ludźmi, ale z władcami świata ciemności i z niewidzialnymi siłami zła.

13Używajcie więc całej zbroi Bożej, abyście w dniu ataku byli gotowi do obrony i byście odnieśli zwycięstwo. 14Bądźcie więc gotowi! Waszym pasem niech będzie prawda, a pancerzem—prawość. 15Waszymi butami niech będzie gotowość niesienia ludziom dobrej nowiny o pokoju. 16W każdej sytuacji osłaniajcie się tarczą, którą jest wasza wiara. Dzięki niej ugasicie wszystkie ogniste pociski szatana. 17Załóżcie też hełm, którym jest wasze zbawienie, a do rąk weźcie miecz Ducha, czyli słowo Boże. 18Poza tym wszystkim, korzystajcie z mocy Ducha Świętego, w każdej sytuacji modląc się do Boga i prosząc Go, aby miał w swojej opiece wszystkich świętych na świecie. 19A módlcie się również za mnie, aby Bóg dał mi właściwe słowa, gdy będę przemawiał, i abym bez obaw mógł przedstawiać ludziom tajemnicę dobrej nowiny, 20z powodu której jestem teraz w więzieniu. Proście więc Boga, abym—tak jak należy—mógł ją głosić z odwagą.

Końcowe pozdrowienie

21-22Chcę, abyście wiedzieli, co u mnie słychać. Dlatego wysyłam do was Tychika, mojego drogiego przyjaciela i wiernego pomocnika w pracy dla Pana. On wszystko wam opowie i doda wam otuchy.

23Przyjaciele, niech Bóg Ojciec i Jezus Chrystus, nasz Pan, obdarzają was pokojem, miłością i wiarą! 24Wszystkim wam, którzy kochacie naszego Pana, Jezusa Chrystusa, życzę łaski od Boga!