Aefeso 6 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 6:1-24

Ana ndi Makolo Awo

1Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera. 2“Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo. 3Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.” 4Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.

Antchito ndi Mabwana Awo

5Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu. 6Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu. 7Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu. 8Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.

9Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.

Zida Zankhondo za Mulungu

10Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu. 11Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana. 12Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. 13Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu. 14Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa. 15Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato. 16Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo. 17Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu. 18Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.

19Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha. 20Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.

Mawu Otsiriza

21Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita. 22Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.

23Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse. 24Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.

Bibelen på hverdagsdansk

Efeserbrevet 6:1-24

Forholdet mellem børn og forældre

Kol. 3,20-22

1Til jer børn, som hører Herren til, siger jeg: Adlyd jeres forældre, for det er Guds vilje for jer. 2Der står jo skrevet: „Du skal ære din far og din mor,” og det er det første af budene, som har et løfte tilknyttet, nemlig dette: 3„…så du kan få et godt og langt liv på jorden.”6,3 Eller „…i landet.” 2.Mos. 20,12, 5.Mos. 5,16 fra LXX.

4Til jer forældre siger jeg: Vær ikke hårdhændede over for jeres børn, så de bliver oprørske, men vejled dem og advar dem, som Herren selv ville gøre det.

Forholdet mellem slaver og herrer

Kol. 3,23–4,1

5Til jer, som er slaver, siger jeg: Adlyd jeres jordiske herrer. Vis samme respekt og hengivenhed over for dem som over for Kristus. 6I skal ikke kun arbejde hårdt, når jeres herre holder øje med jer. Nej, I skal arbejde som Kristi tjenere, der af hele deres hjerte ønsker at gøre Guds vilje. 7Udfør villigt jeres arbejde, som var det Herren selv og ikke mennesker, I arbejdede for. 8Husk, at Herren vil lønne jer for godt udført arbejde, lige meget om I er slaver eller ej.

9Og I herrer skal tænke i de samme baner over for jeres slaver. Lad være med at underkue dem, for I ved, at I og jeres slaver har den samme Herre i Himlen, og han ser ikke på folks status i samfundet.

Den kristnes kamp og udrustning

10Til sidst vil jeg minde jer om at hente styrke fra Herren og hans vældige kraft. 11Ifør jer hele Guds rustning, så I kan forsvare jer mod Satans lumske angreb. 12Den kamp, vi står i, er jo ikke mod mennesker, men imod åndelige magter, autoriteter og herskere i denne mørke verden, mod en hær af onde ånder i himmelrummet.

13Derfor skal I tage hele Guds udrustning på, så I kan forsvare jer imod den Ondes angreb og stå fast, indtil alle angrebene er overstået. 14Spænd sandheden som bælte om livet. Tag ret levevis på som brynje 15og budskabet om fred som støvler, så I kan stå fast.6,15 Meningen er uklar. Kan måske også oversættes: „…og tag som støvler på fødderne villighed til at bringe fredens gode budskab.” 16Løft troens skjold, som I kan bruge til at stoppe Satans brændende pile. 17Tag frelsens hjelm på og forsvar jer med Åndens sværd, som er Guds ord. 18Vær altid i bøn til Gud under Åndens inspiration, hvad enten det er forbøn eller bøn om hjælp. Vær udholdende og årvågne, når I beder for alle dem, der hører Kristus til.

19Bed også for mig, at Gud må give mig de rette ord, så jeg med frimodighed kan kommunikere det budskab om Kristus, som Gud har åbenbaret for os, 20og som er årsag til, at jeg sidder i fængsel. Bed om, at jeg må have frimodighed til at fortsætte med at tale om det, for jeg ved, at det er den opgave, Herren har sendt mig for at udføre.

Afsluttende ord og velsignelse

21Dette brev bliver overbragt jer af Tykikos, som er en elsket medkristen og en trofast medarbejder i Herrens tjeneste. Han kan fortælle jer mere nyt herfra. 22Jeg sender ham til jer, for at I kan høre, hvordan det går os, og for at han kan være til opmuntring for jer.

23Fred, kærlighed og tro fra Gud Fader og Herren Jesus Kristus være med jer, kære venner. 24Guds nåde være over alle, som med en udødelig kærlighed elsker Jesus Kristus, vores Herre.