Aefeso 4 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 4:1-32

Umodzi Mʼthupi la Khristu

1Ine monga wamʼndende chifukwa chotumikira Ambuye, ndikukulimbikitsani kuti mukhale moyo woyenera mayitanidwe amene munalandira. 2Mukhale odzichepetsa kwathunthu ndi ofatsa; mukhale oleza mtima, ololerana wina ndi mnzake mwachikondi. 3Muyesetse kusunga umodzi wa Mzimu; umodzi umene umatimangirira pamodzi mu mtendere. 4Pali thupi limodzi ndiponso Mzimu mmodzi, monganso pali chiyembekezo chimodzi chimene anakuyitanirani. 5Pali Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi; 6Mulungu mmodzi ndi Atate a onse, ndipo ali mwa onse.

7Koma aliyense wa ife wapatsidwa chisomo molingana ndi muyeso wa mphatso ya Khristu. 8Nʼchifukwa chake akunena kuti,

“Iye atakwera kumwamba,

anatenga chigulu cha a mʼndende

ndipo anapereka mphatso kwa anthu.”

9Kodi mawu akuti, “Iye anakwera” akutanthauza chiyani, ngati Iyeyo sanatsikire kunsi kwa dziko lapansi? 10Iye amene anatsika ndi yemweyo anakwera koposa mʼmayiko a kumwamba onse, ndi cholinga choti zinthu zonse zikhale zodzaza ndi Iye. 11Iye ndiye amene anapereka mphatso kwa ena kuti akhale atumwi ndi ena aneneri, ena alaliki, ndi ena abusa ndi aphunzitsi. 12Ntchito yawo ndi kukonza oyera mtima kuti agwire ntchito ya utumiki kuti thupi la Khristu lilimbikitsidwe. 13Izi zidzatifikitsa tonse ku umodzi wachikhulupiriro, kumudziwa Mwana wa Mulungu, kukhwima msinkhu ndi kufika pa muyeso wangwiro weniweni wopezeka mwa Khristu.

14Motero sitidzakhalanso makanda, ogwedezekagwedezeka ndi mafunde, otengekatengeka ndi mphepo iliyonse ya chiphunzitso ndi kuchenjera kwa anthu achinyengo amene amasocheretsa anthu ndi kuchenjera kwawo. 15Mʼmalo mwake, poyankhula choonadi mwachikondi, tidzakula mu zinthu zonse ndi kukhala thupi la Khristu, amene ndi Mutu, omwe ndi mpingo. 16Mwa Iye thupi lonse lalumikizidwa ndi kugwirana pamodzi ndi mitsempha yothandizira. Likukula ndi kudzilimbitsa lokha mwachikondi, pomwe chiwalo chilichonse chikugwira ntchito yake.

Malangizo pa Makhalidwe a Chikhristu

17Tsono ine ndikukuwuzani izi, ndipo ndikunenetsa mwa Ambuye, kuti musayendenso monga amachitira anthu a mitundu ina potsata maganizo awo opanda pake. 18Maganizo awo ndi odetsedwa, ndi osiyanitsidwa ndi moyo wa Mulungu chifukwa cha umbuli umene uli mwa iwo chifukwa cha kuwuma mtima kwawo. 19Popeza sazindikiranso kanthu kalikonse, adzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti achite mtundu uliwonse wa zoyipa ndi zilakolako zosatha.

20Koma inu simunadziwe Khristu mʼnjira yotere. 21Zoonadi munamva za Iye ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye molingana ndi choonadi chimene chili mwa Yesu. 22Inu munaphunzitsidwa molingana ndi moyo wanu wakale, kuchotsa umunthu wakale, umene ukupitirira kuwonongeka ndi zilakolako zachinyengo; 23kuti mukonzedwe mwatsopano mʼmitima mwanu; 24ndi kuti muvale umunthu watsopano, wolengedwa kuti ufanane ndi Mulungu mu chilungamo chenicheni ndi chiyero.

25Chifukwa chake, aliyense wa inu aleke kunama ndipo ayankhule zoona kwa mʼbale wake, pakuti ife tonse ndife ziwalo za thupi limodzi. 26Kwiyani koma musachimwe. Dzuwa lisalowe mukanali chikwiyire. 27Musamupatse mpata Satana. 28Iye amene wakhala akuba asabenso, koma agwire ntchito ndi kuchita kenakake kaphindu ndi manja ake, kuti akhale ndi kenakake kogawana ndi amene akusowa.

29Mʼkamwa mwanu musatuluke mawu aliwonse onyansa, koma okhawo amene ndi othandiza kulimbikitsa ena molingana ndi zosowa zawo, kuti athandize amene akawamve. 30Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu amene mwasindikizidwa naye chizindikiro cha tsiku la kuwomboledwa. 31Chotsani kuzondana, ukali ndi kupsa mtima, chiwawa ndi kuyankhula zachipongwe, pamodzi ndi choyipa chilichonse. 32Mukomerane mtima ndi kuchitirana chifundo wina ndi mnzake. Khululukiranani wina ndi mnzake, monga momwe Mulungu anakukhululukirani mwa Khristu.

Knijga O Kristu

Efežanima 4:1-32

Jedinstvo u Tijelu

1Zaklinjem vas dakle kao sužanj u Gospodinu: živite dostojno poziva kojim vas je Bog pozvao. 2Budite ponizni i strpljivi. Podnosite nedostatke drugih s ljubavlju. 3Nastojte biti jedinstveni u Duhu, povezani mirom.

4Svi smo mi jedno Tijelo, svi imamo jednoga Duha i svi smo pozvani k jednoj nadi. 5Samo je jedan Gospodin, jedna je vjera, jedno krštenje. 6Samo je jedan Bog Otac nad svima nama, koji prebiva u svima nama i djeluje kroz sve nas. 7A svakomu od nas dana je milost, dar koji nam je Isus dodijelio. 8Zato u Svetome pismu piše:

“Uzlazeći na visinu,

poveo je sa sobom zarobljenike,

a ljudima je dao dare.”4:8 Psalam 68:19.

9Piše da je “uzišao”. To znači da je najprije sišao dolje, na zemlju. 10Koji je sišao, isti je onaj koji je uzišao nad sva nebesa, da sve ispuni.

11Jednima je darovao da budu apostoli; drugima da budu proroci; jednima da budu evanđelisti, drugima pastiri i učitelji; 12da osposobi svete da mogu služiti i izgrađivati Crkvu, Kristovo tijelo, 13sve dok ne postignemo takvo jedinstvo vjere i spoznaju Božjega Sina da postanemo zreli u Gospodinu, dok ne uzrastemo do Kristove punine.

14Tada više nećemo biti poput nejačadi koju valovi bacaju amo-tamo i koju goni svaki vjetar prijevarnih ljudskih učenja, lukavština koje zavode na krivi put. 15Živjet ćemo istinoljubivo, u ljubavi, te postajati sve sličnijima Kristu, koji je glava Crkve, svojega Tijela. 16Njegovom skrbi cijelo tijelo savršeno pristaje skupa. Svaki ud obavlja vlastiti posao i pomaže drugim udovima rasti, pa je cijelo Tijelo zdravo te raste i živi u ljubavi.

Živimo kao djeca svjetla

17Ovo kažem u Gospodinovo ime: zaklinjem vas da ne živite kao što žive pogani, razmišljajući isprazno. 18Oni su, naime, zaslijepljeni i zamračena uma, daleko su od Božjega života jer su zatvorili svoj razum prema njemu i ne mogu shvatiti Božje putove. 19Ne mare više je li što dobro ili zlo. Odali su se bludu i u pohlepi počinjaju kojekakve nečistoće.

20Ali vi niste tako poučeni kad ste spoznali Krista. 21Ako ste slušali o njemu i ako ste poučeni da je istina u Isusu, 22odbacite stari način života, starog čovjeka u vama kojega prijevarne požude vode u propast. 23Umjesto toga, Duh mora obnoviti vaš način razmišljanja. 24Morate postati novim čovjekom,4:24 U grčkome: obući se u novoga čovjeka. stvorenim na Božju sliku—pravednim, svetim i istinoljubivim.

25Odbacite zato laž i “govorite istinu jedan drugomu”4:25 Zaharija 8:16. jer pripadamo jedni drugima, udovi smo istoga Tijela. 26“Srdite se ako morate, ali nemojte da vas srdžba odvede u grijeh!”4:26 Psalam 4:5. 27Ne dajte đavlu priliku da djeluje.

28Tko je krao, neka to više ne čini. Radije neka se trudi vlastitim rukama priskrbiti dobra, da ima što podijeliti s onima koji su u potrebi. 29Nikakva ružna riječ neka ne prijeđe preko vaših usana. Neka sve što kažete bude dobro, na izgradnju i dobrobit onima koji vas slušaju.

30Ne žalostite svojim životom Božjega Svetog Duha, kojim ste zapečaćeni za dan otkupljenja.

31Klonite se svake gorčine, srdžbe, gnjeva, vike i kletve te svake opakosti! 32Budite, naprotiv, jedni drugima dobrostivi i milosrdni te praštajte jedni drugima kao što je i Bog u Kristu nama oprostio.