Aefeso 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 3:1-21

Paulo Mlaliki wa Anthu a Mitundu Ina

1Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.

2Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu, 3ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule. 4Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu, 5chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri. 6Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.

7Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu. 8Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu. 9Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. 10Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu. 11Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. 12Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima. 13Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.

Paulo Apempherera Aefeso

14Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate, 15amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo. 16Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake, 17kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi 18kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu. 19Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.

20Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife, 21Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni.

New Russian Translation

Эфесянам 3:1-21

Павел избран возвещать Радостную Весть язычникам

1Вот почему я, Павел, нахожусь в заключении за Иисуса Христа ради вас, язычников.

2Вы, конечно же, слышали о том, что Бог возложил на меня ответственность передать вам Божью благодать. 3Он открыл мне тайный план, о котором я вам уже вкратце писал. 4Прочитав это, вы также сможете постичь то, что я знаю о тайне Христа, 5которая не была открыта прежним поколениям людей, но теперь Дух открыл ее святым Божьим апостолам и пророкам. 6Тайна эта заключается в том, что через Радостную Весть язычники вместе с иудеями становятся наследниками благословений Божьих и членами единого тела. Им также принадлежит обещание, данное в Иисусе Христе.

7По благодати Божьей, данной мне благодаря действию Его силы, я стал служителем этой Радостной Вести. 8Я – самый незначительный из всех святых, и мне была дана эта благодать: возвещать язычникам Радостную Весть о неизмеримом богатстве Христа. 9Мне было доверено просветить всех относительно этого плана, который был от самого начала скрыт Богом, сотворившим все. 10Согласно ему, многообразная мудрость Божья должна теперь открыться начальствам и властям на небесах через Церковь. 11Это Его вечный замысел, который Он осуществил во Христе Иисусе, нашем Господе. 12В Нем и по вере в Него мы можем свободно и уверенно приходить к Богу. 13Поэтому я прошу вас не отчаиваться из-за моих страданий ради вас, потому что они служат к вашей славе.

Любовь Иисуса Христа

14Ради этого я и стою на коленях в молитве перед Отцом, 15от Которого получает имя каждый род на небесах и на земле. 16Я молюсь, чтобы по богатству Своей славы Он Духом Своим наделил вас внутренней силой 17и чтобы через веру в ваши сердца вселился Христос; 18молюсь, чтобы вы, укорененные и утвержденные в любви, вместе со всеми святыми могли понять ширину, длину, высоту и глубину любви Христа 19и могли познать эту любовь, которая превыше человеческого разумения; молюсь, чтобы ваша жизнь преисполнилась всей полнотой Божьей. 20А Тому, Чья сила действует в нас, и Кто может сделать гораздо больше того, о чем мы просим или даже о чем помышляем, 21да будет слава из поколения в поколение, навеки, через Иисуса Христа и через Церковь! Аминь.