Aefeso 2 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 2:1-22

Amene anali Akufa Alandira Moyo

1Kunena za inu, kale munali akufa chifukwa cha zolakwa zanu ndi machimo anu, 2mmene inu munkakhalamo pamene munkatsatira njira za dziko lapansi ndi za ulamuliro waufumu wa mlengalenga, mzimu umene ukugwira ntchito tsopano mwa amene samvera. 3Nthawi ina tonsefe tinalinso ndi moyo wonga wawo, tinkachitanso zilizonse zimene matupi ndi maganizo athu ankafuna. Mwachibadwa chathu, tinali oyenera chilango monga anthu ena onse. 4Koma chifukwa cha chikondi chake chachikulu pa ife, Mulungu amene ndi olemera mʼchifundo, 5anatipanga kukhala amoyo ndi Khristu ngakhale pamene ife tinali akufa mu zolakwa zathu. Koma tinapulumutsidwa mwachisomo. 6Ndipo Mulungu anatiukitsa pamodzi ndi Khristu ndi kutikhazika pamodzi ndi Iye mmwamba mwa Khristu Yesu, 7ndi cholinga chakuti mʼnthawi imene ikubwera, Iyeyo adzaonetse chuma choposa cha chisomo chake, choonetsedwa mwa kukoma mtima kwake kwa ife mwa Khristu Yesu. 8Pakuti mwapulumutsidwa mwachisomo, kudzera mʼchikhulupiriro ndipo izi sizochokera mwa inu eni, koma ndi mphatso ya Mulungu, 9osati ndi ntchito, kuti wina aliyense asadzitamandire. 10Pakuti ndife ntchito ya Mulungu, olengedwa mwa Khristu Yesu kuti tichite ntchito zabwino, zimene Mulungu anazikonzeratu kale kuti tizichite.

Umodzi mwa Khristu

11Chifukwa chake kumbukirani kuti poyamba inu amene munali anthu a mitundu ina mwachibadwa ndipo munkatchedwa “osachita mdulidwe” ndi amene amadzitcha okha “a mdulidwe” (zimene zinachitika mʼthupi ndi manja a anthu). 12Kumbukirani kuti nthawi imene inu munali wopanda Khristu, simunkawerengedwa ngati nzika za Israeli ndipo munali alendo pa pangano la lonjezo, wopanda chiyembekezo ndi opanda Mulungu mʼdziko lapansi. 13Koma tsopano mwa Khristu Yesu, inu amene nthawi ina munali kutali, mwabweretsedwa pafupi kudzera mʼmagazi a Khristu.

14Pakuti Iye mwini ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti awiri akhale mmodzi ndipo anagumula chotchinga, khoma la udani lotilekanitsa, 15pothetsa mʼthupi lake lamulo pamodzi ndi zolamulira zake ndi malangizo. Cholinga chake chinali chakuti alenge mwa Iye mwini, munthu mmodzi watsopano kuchokera kwa abwino, motero nʼkupanga mtendere, 16ndi kuyanjanitsa onse awiriwa mʼthupi lake kwa Mulungu, kudzera pa mtanda, umene Iye anaphapo udani wawo. 17Iye anabwera ndipo analalikira mtendere kwa inu amene munali kutali ndi mtendere ndiponso kwa iwonso amene anali pafupi. 18Pakuti mwa Iye, ife tonse titha kufika kwa Atate mwa Mzimu mmodzi.

19Kotero kuti, inu sindinunso alendo ndi adani, koma nzika pamodzi ndi anthu a Mulungu ndiponso a mʼbanja la Mulungu. 20Ndinu okhazikika pa maziko a atumwi ndi a aneneri, pamodzi ndi Khristu Yesu mwini ngati mwala wa pa ngodya. 21Mwa Iyeyo, nyumba yonse yalumikizidwa pamodzi ndipo yakwezedwa kukhala Nyumba yoyera mwa Ambuye. 22Ndipo mwa Iye, inunso mukamangidwa pamodzi ndi ena onse kukhala nyumba yokhalamo imene Mulungu amakhala mwa Mzimu wake.

Thai New Contemporary Bible

เอเฟซัส 2:1-22

มีชีวิตในพระคริสต์

1ส่วนท่านทั้งหลายได้ตายแล้วในการล่วงละเมิดและในบาปทั้งหลาย 2ซึ่งท่านเคยทำเมื่อดำเนินชีวิตตามวิถีของโลกนี้ และวิถีของเจ้าแห่งย่านฟ้าอากาศซึ่งเป็นวิญญาณที่บัดนี้ทำการอยู่ในบรรดาผู้ที่ไม่เชื่อฟัง 3ครั้งหนึ่งเราเคยใช้ชีวิตร่วมกับพวกนั้นบำเรอตัณหาแห่งวิสัยบาปของเรา2:3 หรือเนื้อหนังของเรา สนองความอยากกับความคิดของมันตามวิสัย เราจึงควรแก่พระพิโรธเหมือนคนอื่น 4แต่เนื่องด้วยความรักใหญ่หลวงที่ทรงมีต่อเรา พระเจ้าผู้เปี่ยมด้วยพระเมตตาอันอุดม 5จึงทรงให้เรามีชีวิตอยู่กับพระคริสต์แม้เมื่อเราได้ตายแล้วในบาป คือท่านทั้งหลายได้รับความรอดโดยพระคุณ 6และพระองค์ทรงให้เราเป็นขึ้นมากับพระคริสต์ และในพระเยซูคริสต์ พระเจ้าทรงให้เรานั่งในสวรรคสถานกับพระคริสต์ 7เพื่อในยุคต่อๆ ไปพระองค์จะได้ทรงสำแดงความอุดมแห่งพระคุณอันหาใดเปรียบ ซึ่งได้ทรงแสดงด้วยพระกรุณาที่มีต่อเราในพระเยซูคริสต์ 8เพราะว่าท่านทั้งหลายได้รับความรอดโดยพระคุณผ่านทางความเชื่อ ความรอดนี้ไม่ได้มาจากตัวท่านเอง แต่เป็นของประทานจากพระเจ้า 9ไม่ใช่ความรอดโดยการประพฤติ เพื่อจะไม่มีใครอวดได้ 10เพราะเราทั้งหลายเป็นผลงานของพระเจ้าซึ่งทรงสร้างในพระเยซูคริสต์เพื่อให้ทำการดีที่พระเจ้าทรงจัดเตรียมไว้ล่วงหน้าให้เราทำ

หนึ่งเดียวกันในพระคริสต์

11เพราะฉะนั้นจงระลึกว่าแต่ก่อนท่านเป็นคนต่างชาติโดยกำเนิด และบรรดาผู้ที่เรียกตนเองว่า “พวกที่เข้าสุหนัต” (ซึ่งกระทำทางกายด้วยมือมนุษย์) เรียกท่านว่า “พวกไม่เข้าสุหนัต” 12จงระลึกว่าครั้งนั้นท่านแยกจากพระคริสต์ ไม่ได้เป็นพลเมืองอิสราเอลและเป็นคนต่างด้าวอยู่นอกพันธสัญญาที่ทรงสัญญาไว้ ไม่มีความหวังและอยู่ในโลกโดยปราศจากพระเจ้า 13แต่บัดนี้ในพระเยซูคริสต์ท่านทั้งหลายซึ่งเมื่อก่อนอยู่ไกลได้เข้ามาใกล้แล้วโดยพระโลหิตของพระคริสต์

14เพราะพระองค์เองทรงเป็นสันติสุขของเรา ผู้ทรงทำให้สองพวกกลายเป็นหนึ่งเดียวกัน และทรงทำลายสิ่งกีดขวาง คือกำแพงแห่งความเกลียดชังที่กีดกั้นลง 15โดยทรงล้มเลิกบทบัญญัติทั้งหมดของชาวยิวซึ่งประกอบด้วยข้อบังคับและกฎระเบียบต่างๆ ด้วยพระกายของพระองค์ จุดประสงค์ของพระองค์ก็เพื่อยุบสองฝ่ายและสร้างขึ้นใหม่เป็นหนึ่งเดียวในพระองค์ เช่นนี้แหละจึงทรงทำให้มีสันติสุข 16และในกายเดียวนี้ทั้งสองพวกจึงกลับคืนดีกับพระเจ้าโดยไม้กางเขน ซึ่งพระองค์ทรงใช้ทำลายความเป็นศัตรูกันให้หมดสิ้นไป 17พระองค์เสด็จมาประกาศสันติสุขแก่ท่านทั้งหลายที่อยู่ไกลและสันติสุขแก่ผู้ที่อยู่ใกล้ 18เพราะโดยพระองค์เราทั้งสองพวกสามารถเข้าถึงพระบิดาโดยพระวิญญาณองค์เดียวกัน

19ดังนั้นท่านจึงไม่ใช่คนต่างด้าวแปลกถิ่นอีกต่อไป แต่เป็นพลเมืองเดียวกับประชากรของพระเจ้าและเป็นสมาชิกในครอบครัวของพระเจ้า 20ท่านได้รับการสร้างขึ้นบนฐานรากของเหล่าอัครทูตและผู้เผยพระวจนะโดยมีพระเยซูคริสต์เองเป็นศิลามุมเอก 21ในพระองค์ ทุกส่วนของอาคารทั่วทั้งหมดต่อกันสนิท และประกอบกันขึ้นเป็นวิหารอันศักดิ์สิทธิ์ในองค์พระผู้เป็นเจ้า 22และในพระองค์ ท่านก็เช่นกันกำลังรับการทรงสร้างขึ้นด้วยกันให้เป็นที่ประทับซึ่งพระเจ้าสถิตอยู่โดยพระวิญญาณของพระองค์