Aefeso 2 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 2:1-22

Amene anali Akufa Alandira Moyo

1Kunena za inu, kale munali akufa chifukwa cha zolakwa zanu ndi machimo anu, 2mmene inu munkakhalamo pamene munkatsatira njira za dziko lapansi ndi za ulamuliro waufumu wa mlengalenga, mzimu umene ukugwira ntchito tsopano mwa amene samvera. 3Nthawi ina tonsefe tinalinso ndi moyo wonga wawo, tinkachitanso zilizonse zimene matupi ndi maganizo athu ankafuna. Mwachibadwa chathu, tinali oyenera chilango monga anthu ena onse. 4Koma chifukwa cha chikondi chake chachikulu pa ife, Mulungu amene ndi olemera mʼchifundo, 5anatipanga kukhala amoyo ndi Khristu ngakhale pamene ife tinali akufa mu zolakwa zathu. Koma tinapulumutsidwa mwachisomo. 6Ndipo Mulungu anatiukitsa pamodzi ndi Khristu ndi kutikhazika pamodzi ndi Iye mmwamba mwa Khristu Yesu, 7ndi cholinga chakuti mʼnthawi imene ikubwera, Iyeyo adzaonetse chuma choposa cha chisomo chake, choonetsedwa mwa kukoma mtima kwake kwa ife mwa Khristu Yesu. 8Pakuti mwapulumutsidwa mwachisomo, kudzera mʼchikhulupiriro ndipo izi sizochokera mwa inu eni, koma ndi mphatso ya Mulungu, 9osati ndi ntchito, kuti wina aliyense asadzitamandire. 10Pakuti ndife ntchito ya Mulungu, olengedwa mwa Khristu Yesu kuti tichite ntchito zabwino, zimene Mulungu anazikonzeratu kale kuti tizichite.

Umodzi mwa Khristu

11Chifukwa chake kumbukirani kuti poyamba inu amene munali anthu a mitundu ina mwachibadwa ndipo munkatchedwa “osachita mdulidwe” ndi amene amadzitcha okha “a mdulidwe” (zimene zinachitika mʼthupi ndi manja a anthu). 12Kumbukirani kuti nthawi imene inu munali wopanda Khristu, simunkawerengedwa ngati nzika za Israeli ndipo munali alendo pa pangano la lonjezo, wopanda chiyembekezo ndi opanda Mulungu mʼdziko lapansi. 13Koma tsopano mwa Khristu Yesu, inu amene nthawi ina munali kutali, mwabweretsedwa pafupi kudzera mʼmagazi a Khristu.

14Pakuti Iye mwini ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti awiri akhale mmodzi ndipo anagumula chotchinga, khoma la udani lotilekanitsa, 15pothetsa mʼthupi lake lamulo pamodzi ndi zolamulira zake ndi malangizo. Cholinga chake chinali chakuti alenge mwa Iye mwini, munthu mmodzi watsopano kuchokera kwa abwino, motero nʼkupanga mtendere, 16ndi kuyanjanitsa onse awiriwa mʼthupi lake kwa Mulungu, kudzera pa mtanda, umene Iye anaphapo udani wawo. 17Iye anabwera ndipo analalikira mtendere kwa inu amene munali kutali ndi mtendere ndiponso kwa iwonso amene anali pafupi. 18Pakuti mwa Iye, ife tonse titha kufika kwa Atate mwa Mzimu mmodzi.

19Kotero kuti, inu sindinunso alendo ndi adani, koma nzika pamodzi ndi anthu a Mulungu ndiponso a mʼbanja la Mulungu. 20Ndinu okhazikika pa maziko a atumwi ndi a aneneri, pamodzi ndi Khristu Yesu mwini ngati mwala wa pa ngodya. 21Mwa Iyeyo, nyumba yonse yalumikizidwa pamodzi ndipo yakwezedwa kukhala Nyumba yoyera mwa Ambuye. 22Ndipo mwa Iye, inunso mukamangidwa pamodzi ndi ena onse kukhala nyumba yokhalamo imene Mulungu amakhala mwa Mzimu wake.

Swedish Contemporary Bible

Efesierbrevet 2:1-22

Nytt liv i gemenskapen med Kristus

1Ni var döda i era överträdelser och synder, 2då ni levde på den nuvarande världens vis. Ni följde härskaren över luftens rike, den andemakt som nu verkar i olydnadens människor. 3På det sättet levde vi allihop förut. Vi följde våra mänskliga impulser och lät kroppens begär och våra egna tankar styra oss. Av naturen var vi vredens barn, precis som alla andra.

4Men vår Gud som är rik på barmhärtighet har älskat oss så mycket 5att han gjorde oss levande tillsammans med Kristus, trots att vi var döda genom våra överträdelser. Det är av nåd som ni är räddade. 6Han har uppväckt oss med honom och gett oss en plats i himlen i Kristus Jesus, 7för att i kommande tidsåldrar visa sin överväldigande rika nåd i godheten mot oss i Kristus Jesus.

8Ni är alltså räddade av nåd genom tron, inte av er själva, utan det är en gåva från Gud, 9inte på grund av gärningar, och därför kan heller ingen skryta. 10Vi är hans verk, skapade i Kristus Jesus till goda gärningar, som Gud från början planerade att vi skulle göra.

Alla är ett i gemenskapen med Kristus

11Kom därför ihåg att ni som var födda hedningar och kallades oomskurna av dem som kallas omskurna, utifrån den fysiska omskärelse som människor utför, 12kom ihåg att ni på den tiden var utan Kristus, utan medborgarskap i Israel, utan delaktighet i förbunden och deras löfte, utan hopp och utan Gud här i världen. 13Men nu har ni i Kristus, ni som en gång var långt borta, kommit nära genom Kristus blod.

14Han är nämligen vår fred, han som gjorde de två till ett och rev ner fiendskapens skiljemur. 15Han har i sin kropp tillintetgjort lagen med dess bud och föreskrifter, för att i sig skapa en ny människa av de två, och därmed stifta fred. 16I denna enda kropp försonade han de båda med Gud genom korset, där han dödade fiendskapen. 17Han kom med evangeliet om fred för er som var långt borta, och fred för dem som var nära. 18Och nu kan vi båda genom honom komma inför Fadern, i en och samma Ande.

19Alltså är ni inte längre gäster och främlingar, utan har samma medborgarskap som de heliga och tillhör Guds husfolk. 20Ni är byggda på apostlarnas och profeternas2:20 Detta syftar antagligen på de profeter som verkade i församlingarna. Se 3:5. grund, med Kristus Jesus själv som hörnsten. 21Det är i honom som hela huset fogas samman, så att det byggs upp till ett heligt tempel i Herren. 22I honom fogas också ni samman till en boning åt Gud i Anden.