Aefeso 1 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 1:1-23

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu.

Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:

2Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso Auzimu mwa Khristu

3Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. 4Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, 5Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. 6Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. 7Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu 8chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, 9Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.

11Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.

Kuyamika ndi Kupemphera

15Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse, 16ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga. 17Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni. 18Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima. 19Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija 20imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba. 21Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. 22Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo, 23umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

New International Version – UK

Ephesians 1:1-23

1Paul, an apostle of Christ Jesus by the will of God,

To God’s holy people in Ephesus,1:1 Some early manuscripts do not have in Ephesus. the faithful in Christ Jesus:

2Grace and peace to you from God our Father and the Lord Jesus Christ.

Praise for spiritual blessings in Christ

3Praise be to the God and Father of our Lord Jesus Christ, who has blessed us in the heavenly realms with every spiritual blessing in Christ. 4For he chose us in him before the creation of the world to be holy and blameless in his sight. In love 5he1:4,5 Or sight in love. 5 He predestined us for adoption to sonship1:5 The Greek word for adoption to sonship is a legal term referring to the full legal standing of an adopted male heir in Roman culture. through Jesus Christ, in accordance with his pleasure and will – 6to the praise of his glorious grace, which he has freely given us in the One he loves. 7In him we have redemption through his blood, the forgiveness of sins, in accordance with the riches of God’s grace 8that he lavished on us. With all wisdom and understanding, 9he1:8,9 Or us with all wisdom and understanding. 9 And he made known to us the mystery of his will according to his good pleasure, which he purposed in Christ, 10to be put into effect when the times reach their fulfilment – to bring unity to all things in heaven and on earth under Christ.

11In him we were also chosen,1:11 Or were made heirs having been predestined according to the plan of him who works out everything in conformity with the purpose of his will, 12in order that we, who were the first to put our hope in Christ, might be for the praise of his glory. 13And you also were included in Christ when you heard the message of truth, the gospel of your salvation. When you believed, you were marked in him with a seal, the promised Holy Spirit, 14who is a deposit guaranteeing our inheritance until the redemption of those who are God’s possession – to the praise of his glory.

Thanksgiving and prayer

15For this reason, ever since I heard about your faith in the Lord Jesus and your love for all God’s people, 16I have not stopped giving thanks for you, remembering you in my prayers. 17I keep asking that the God of our Lord Jesus Christ, the glorious Father, may give you the Spirit1:17 Or a spirit of wisdom and revelation, so that you may know him better. 18I pray that the eyes of your heart may be enlightened in order that you may know the hope to which he has called you, the riches of his glorious inheritance in his holy people, 19and his incomparably great power for us who believe. That power is the same as the mighty strength 20he exerted when he raised Christ from the dead and seated him at his right hand in the heavenly realms, 21far above all rule and authority, power and dominion, and every name that is invoked, not only in the present age but also in the one to come. 22And God placed all things under his feet and appointed him to be head over everything for the church, 23which is his body, the fullness of him who fills everything in every way.