Aefeso 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aefeso 1:1-23

1Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu.

Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:

2Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.

Madalitso Auzimu mwa Khristu

3Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu. 4Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake, 5Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake. 6Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda. 7Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu 8chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso, 9Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake. 10Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.

11Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake, 12nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake. 13Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza. 14Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.

Kuyamika ndi Kupemphera

15Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse, 16ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga. 17Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni. 18Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima. 19Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija 20imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba. 21Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. 22Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo, 23umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以弗所書 1:1-23

1我是奉上帝旨意作基督耶穌使徒的保羅,寫信給以弗所忠於基督耶穌的眾聖徒。

2願我們的父上帝和主耶穌基督賜給你們恩典和平安!

基督徒的屬靈恩福

3讚美我們主耶穌基督的父上帝!祂在基督裡賜給了我們天上各樣屬靈的恩福。 4早在創造世界以前,祂已經在基督裡揀選了我們,使我們在祂眼中成為聖潔無瑕的人。

5上帝因為愛我們,就按照祂自己美好的旨意,預定我們藉著耶穌基督得到作祂兒女的名分。 6我們讚美祂奇妙無比的恩典,這恩典是上帝藉著祂的愛子賜給我們的。 7我們藉著祂愛子的血蒙救贖,過犯得到赦免,這都是出於祂的洪恩。 8上帝用各種智慧和聰明把這恩典豐豐富富地賜給我們, 9照著祂在基督裡所定的美好計劃叫我們知道祂旨意的奧祕, 10等所定的時候一到,叫天地萬物一同歸在基督的名下。

11我們也在基督裡被揀選成為祂的子民。這都是按自己旨意行萬事的上帝預先定下的計劃, 12好讓我們這些首先在基督裡得到盼望的人都來頌讚祂的榮耀。

13你們聽過真理之道,就是那使你們得救的福音,而且也信了基督。你們既然信祂,就領受了上帝應許賜下的聖靈為印記。 14聖靈是我們領受產業的擔保,直到上帝的子民得到救贖,使祂的榮耀受到頌讚。

保羅的禱告

15我聽到你們對主耶穌的信心和對眾聖徒的愛心後, 16不斷地為你們感謝上帝,禱告的時候常常提到你們。 17我求我們主耶穌基督的上帝——榮耀的父把賜智慧和啟示的靈給你們,好使你們更深地認識祂。 18我也求上帝照亮你們心中的眼睛,使你們知道祂的呼召給你們帶來了何等的盼望,祂應許賜給眾聖徒的產業有何等豐富的榮耀, 19並且祂在我們這些信的人身上所運行的能力是何等浩大。 20上帝曾用這大能使基督從死裡復活,使基督在天上坐在自己右邊, 21遠遠超越今生永世所有執政的、掌權的、有能力的、作主宰的和一切的權勢。 22祂又使萬物降服在基督腳下,使基督為教會作萬物的元首。 23教會是基督的身體,蘊涵著那無所不在、充滿萬物者的豐盛。