3 Yohane 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Yohane 1:1-15

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.

2Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu. 3Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi. 4Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.

5Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo. 6Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu. 7Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira. 8Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.

Za Diotrefe ndi Demetriyo

9Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera. 10Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.

11Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu. 12Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.

13Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. 14Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso.

15Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.

Knijga O Kristu

3 Ivanova 1:1-15

Pozdrav

1Starješina Ivan,1:1 U grčkome: samo starješina. dragomu Gaju kojega volim u Istini.

2Dragi moj, molim se da u svemu budeš dobro te da ti je tijelo zdravo kao što znam da ti je zdrava duša. 3Veoma su me obradovala neka braća koja su došla i posvjedočila mi da živiš čestito i u Istini. 4Za mene nema veće radosti nego kad čujem da moja djeca žive u Istini!

Briga za Božje djelatnike

5Dragi moj, postupaš kao pravi vjernik pomažući braći, i to došljacima. 6Oni su ovdašnjoj Crkvi pričali o tvojim djelima ljubavi. Dobro činiš opskrbljujući ih za put kako je dostojno Boga. 7Jer oni putuju radi Gospodina1:7 U grčkome: radi Imena. i ne primaju ništa od nekršćana.1:7 U grčkome: od pogana. 8Dužni smo im pružati gostoprimstvo da budemo suradnici Istine.

9O tomu sam ukratko pisao Crkvi, ali Diotref, koji želi biti vođa, ne želi s nama ništa imati. 10Kad dođem onamo, spočitnut ću mu ono što čini naklapajući o nama zlobne riječi. Ne samo da odbija prihvatiti braću koja dođu već to zabranjuje i onima koji bi ih htjeli prihvatiti i izopćuje ih iz Crkve.

11Dragi moj, ne povodi se za lošim, nego za dobrim. Tko čini dobro, od Boga je; tko čini zlo, ne poznaje Boga. 12O Demetriju svi govore samo najbolje, a i sama Istina govori njemu u prilog. I mi o njemu možemo isto reći, a znaš da mi govorimo istinu.

Zaključak

13Mnogo vam još toga imam kazati, ali ne želim o tomu pisati. 14Nadam se da ću te uskoro vidjeti, pa ćemo razgovarati licem u lice.

15Neka je Božji mir s tobom.

Pozdravljaju te prijatelji! Molim te, pozdravi mi poimence svakoga našeg prijatelja.