3 Yohane 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Yohane 1:1-15

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.

2Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu. 3Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi. 4Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.

5Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo. 6Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu. 7Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira. 8Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.

Za Diotrefe ndi Demetriyo

9Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera. 10Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.

11Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu. 12Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.

13Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. 14Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso.

15Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約翰三書 1:1-15

1我這作長老的寫信給親愛的該猶,就是我本著真理所愛的人。 2親愛的弟兄,衷心地祝你凡事順利,身體和靈魂一樣健康。

該猶的好品行

3有弟兄們來為你的行為做見證,說你忠心地遵行真理,這使我非常欣慰。 4沒有比聽見自己的孩子遵行真理更使我歡喜了。

5親愛的弟兄,你常常忠心地照顧素不相識的弟兄, 6他們把你的愛心告訴了教會。願你照著上帝所喜悅的方式繼續幫助他們, 7因為他們為了主耶穌的名四處傳道,不收取非信徒的任何東西。 8我們應該接待這樣的人,好與他們一同傳揚真理。

丟特腓的惡行

9我曾寫信給你那裡的教會,但喜歡做領袖的丟特腓不理會我們。 10因此,我若去你們那裡,會提及他的所作所為,就是他怎樣惡言中傷我們。不僅如此,他還拒絕接待弟兄,並且禁止別人接待,甚至將接待的人趕出教會。

抑惡揚善

11親愛的弟兄,不要效法罪惡,要效法美善。行善的人屬於上帝,行惡的人不認識上帝。 12低米丟得到了眾人的好評,真理本身也為他做見證,我們也為他做見證。你們知道我們的見證是真實的。

結語

13我本來有很多事想跟你談,但不想用筆墨寫給你, 14只希望可以快快地見到你,跟你當面暢談。

15祝你平安!這裡的朋友們都問候你,請代我一一問候你那邊的朋友。