3 Yohane 1 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

3 Yohane 1:1-15

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.

2Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu. 3Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi. 4Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.

5Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo. 6Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu. 7Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira. 8Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.

Za Diotrefe ndi Demetriyo

9Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera. 10Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.

11Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu. 12Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.

13Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. 14Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso.

15Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约翰三书 1:1-15

1我这做长老的写信给亲爱的该犹,就是我本着真理所爱的人。 2亲爱的弟兄,衷心地祝你凡事顺利,身体和灵魂一样健康。

该犹的好品行

3有弟兄们来为你的行为做见证,说你忠心地遵行真理,这使我非常欣慰。 4没有比听见自己的孩子遵行真理更使我欢喜了。

5亲爱的弟兄,你常常忠心地照顾素不相识的弟兄, 6他们把你的爱心告诉了教会。愿你照着上帝所喜悦的方式继续帮助他们, 7因为他们为了主耶稣的名四处传道,不收取非信徒的任何东西。 8我们应该接待这样的人,好与他们一同传扬真理。

丢特腓的恶行

9我曾写信给你那里的教会,但喜欢做领袖的丢特腓不理会我们。 10因此,我若去你们那里,会提及他的所作所为,就是他怎样恶言中伤我们。不仅如此,他还拒绝接待弟兄,并且禁止别人接待,甚至将接待的人赶出教会。

抑恶扬善

11亲爱的弟兄,不要效法罪恶,要效法美善。行善的人属于上帝,行恶的人不认识上帝。 12低米丢得到了众人的好评,真理本身也为他做见证,我们也为他做见证。你们知道我们的见证是真实的。

结语

13我本来有很多事想跟你谈,但不想用笔墨写给你, 14只希望可以快快地见到你,跟你当面畅谈。

15祝你平安!这里的朋友们都问候你,请代我一一问候你那边的朋友。