2 Yohane 1 – CCL & PEV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Yohane 1:1-13

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi. 2Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya.

3Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.

Choonadi ndi Chikondi

4Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira. 5Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake. 6Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.

7Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu. 8Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse. 9Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana. 10Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni. 11Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.

12Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.

13Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

La Parola è Vita

2 Giovanni 1:1-13

1Questa lettera è scritta da me, Giovanni, anziano della Chiesa, alla Signora eletta e ai suoi figli, che amo sinceramente, come li amano anche tutti i credenti, 2grazie alla verità che è e resterà per sempre nel nostro cuore.

3Grazia, misericordia e pace saranno con noi come doni di Dio Padre e di Gesù Cristo, Figlio suo nella verità e nellʼamore.

Attenzione ai falsi maestri!

4Mi ha fatto molto piacere aver trovato qui alcuni dei tuoi figli, e constatare che vivono seguendo la verità e obbedendo ai comandamenti di Dio.

5Ed ora, signora, voglio ricordarti il vecchio comandamento che Dio ci ha dato fin dal principio, e cioè che i cristiani devono amarsi a vicenda. 6Se amiamo Dio, vivremo secondo i suoi comandamenti; e il comandamento che Dio ci ha dato fin dal principio, è questo: vivete nellʼamore.

7State in guardia dai falsi maestri (se ne sono presentati tanti), parlo di quelli che non credono che Gesù Cristo venne sulla terra come essere umano, con un corpo come il nostro. Qualsiasi persona così è lʼingannatore e lʼanticristo. 8Badate di non essere come loro e di non perdere il premio delle vostre fatiche, ma comportatevi in modo da ricevere una piena ricompensa dal Signore. 9Chi va al di là dellʼinsegnamento di Cristo, non ha Dio. Chi, invece, sta saldo nellʼinsegnamento di Cristo, resta unito al Padre e al Figlio.

10Se qualcuno viene da voi e non crede a ciò che Cristo ha insegnato, non fatelo neppure entrare in casa! E non lo salutate. 11Se lo fate, sarete suoi complici nella sua malvagità.

12Avrei ancora tante cose da scrivervi, ma non voglio farlo per lettera, perché spero di venire a trovarvi presto e di parlarne con voi a viva voce. Così la vostra gioia sarà completa.

13Ti salutano i figli di tua sorella, eletta da Dio. Giovanni.