2 Yohane 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Yohane 1:1-13

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi. 2Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya.

3Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.

Choonadi ndi Chikondi

4Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira. 5Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake. 6Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.

7Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu. 8Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse. 9Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana. 10Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni. 11Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.

12Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.

13Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

New Russian Translation

2 Иоанна 1:1-13

Приветствие

1От старейшины1:1 Или: «от старца». – избранной госпоже1:1 Под госпожой, возможно, имеется в виду не какая-то женщина, а поместная церковь. Под детьми, в таком случае, подразумеваются ее члены. и ее детям, которых я люблю как пребывающих в истине, и не только я, но и все, кто знает истину; 2потому что истина эта живет в нас и будет с нами всегда.

3Благодать, милость и мир будут с нами в истине и любви от Бога Отца и от Иисуса Христа, Его Сына.

Повеление о любви

4Меня очень радует, что среди твоих детей есть ходящие в истине, как нам повелел Отец.

5И сейчас, госпожа, я пишу тебе не какое-то новое повеление, но то, которое было у нас с самого начала: будем любить друг друга. 6И любовь эта заключается в том, чтобы мы соблюдали Его повеления. Вы с самого начала слышали Его повеление, по нему и поступайте.

Оставайтесь верными Христу

7Много обманщиков вышло в мир, не признающих, что Иисус Христос пришел в человеческом теле1:7 Букв.: «во плоти».. Такой человек – обманщик и антихрист. 8Смотрите, чтобы не потерять то, ради чего мы трудились1:8 В ряде древних рукописей: «вы трудились»., но чтобы получить полную награду. 9Кто не живет согласно учению Христа, но идет иным путем, тот не имеет в себе Бога. Но тот, кто остается верным Его учению, имеет в себе и Отца, и Сына. 10Если кто-либо приходит к вам и приносит не это учение, того вы не должны принимать в дом и приветствовать его. 11Кто приветствует такого человека, тот становится соучастником в его злых делах.

12О многом еще я хотел бы вам сказать, но я не хочу доверять это бумаге и чернилам. Я надеюсь скоро быть у вас и лично поговорить с вами, чтобы наша радость1:12 В ряде древних рукописей: «ваша радость». была полной.

13Привет тебе от детей твоей избранной сестры1:13 Под сестрой, возможно, подразумевается родственная церковь, от членов которой Иоанн передает привет..