2 Yohane 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Yohane 1:1-13

1Ndine mkulu wampingo, kulembera:

Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi. 2Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya.

3Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.

Choonadi ndi Chikondi

4Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira. 5Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake. 6Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.

7Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu. 8Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse. 9Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana. 10Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni. 11Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.

12Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.

13Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

Knijga O Kristu

2 Ivanova 1:1-13

Pozdrav

1Od starješine Ivana1 U grčkome: samo od starješine. izabranoj Gospođi i njezinoj djeci1 Ili: od Boga izabranoj crkvi i njezinim članovima; ili: izabranoj Kiriji i njezinoj djeci. koju volim u Istini—i to ne samo ja, već svi oni koji su Istinu upoznali 2—radi istine koja je trajno u nama i bit će s nama zauvijek.

3Neka budu s nama milost, milosrđe i mir koji dolaze od Boga Oca i od njegova Sina Isusa Krista u istini i ljubavi.

Život u istini

4Silno sam se obradovao što sam među tvojom djecom našao takve koji žive u istini, kao što nam je zapovjedio Otac.

5A sada te molim, Gospođo, da volimo jedni druge. Ne pišem ti to neku novu zapovijed, već onu koju smo imali od početka. 6Ljubav se sastoji u tomu da živimo po Božjim zapovijedima. Živite u toj zapovijedi da ljubite jedni druge, kao što ste čuli od početka.

7U svijetu su se pojavili brojni zavodnici koji ne priznaju da je Isus Krist došao na zemlju u tijelu. Takvi su ljudi obmanjivači i antikristi. 8Pazite da ne izgubite ono što ste već stekli, nego da primite potpunu plaću. 9Tko god zakorači izvan Kristova učenja, neće imati zajedništva s Bogom. Ali tko ostane u Kristovu učenju, imat će zajedništvo i s Ocem i sa Sinom.

10Dođe li vas tko poučavati, a ne donosi to učenje, ne pozivajte ga u svoj dom i ne pozdravljajte ga. 11Pozdravljate li ga, sudionici ste u njegovim zlodjelima.

Završetak i pozdrav

12Mnogo vam još toga imam kazati, ali ne želim to učiniti u pismu. Nadam se da ću doći k vama i licem u lice s vama razgovarati da naša radost bude potpuna.

13Pozdravljaju te djeca tvoje sestre,13 Ili: članovi tvoje sestrinske crkve. izabranice Božje.