2 Timoteyo 4 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 4:1-22

1Pamaso pa Mulungu ndi pamaso pa Khristu Yesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa omwe pamene adzaonekera ndi ufumu wake, ndikukulamula kuti: 2Lalikira Mawu; khala wokonzeka pa nthawi yake, ngakhale pamene si pa nthawi yake. Konza zolakwa zawo, dzudzula ndipo limbikitsa moleza mtima kwambiri ndi malangizo osamalitsa. 3Pakuti idzafika nthawi imene anthu adzakana chiphunzitso choona. Mʼmalo mwake, chifukwa chokhumba kumva zowakomera zokha, adzasonkhanitsa aphunzitsi ambiri omawawuza zimene iwo akufuna kumva. 4Sadzafuna kumva choona koma adzafuna kumva nthano chabe. 5Koma iwe, khala tcheru nthawi zonse, pirira mʼzovuta, gwira ntchito ya mlaliki, gwira ntchito zonse za utumiki wako.

6Pakuti moyo wanga wayamba kale kuthiridwa ngati nsembe, ndipo nthawi yakwana yoti ndinyamuke ulendo wanga. 7Ndamenya nkhondo yabwino, ndatsiriza bwino mpikisano wa liwiro ndipo ndasunga chikhulupiriro. 8Tsopano mphotho yanga ikundidikira imene ndi chipewa cha chilungamo, imene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa pa tsiku lijalo, osati ine ndekha komanso onse amene akufunitsitsa kubwera kwake.

Ndemanga ya Paulo

9Uyesetse kubwera kuno msanga. 10Paja Dema anandisiya chifukwa chokonda dziko lapansi lino, ndipo anapita ku Tesalonika. Kresike anapita ku Galatiya ndipo Tito anapita ku Dalimatiya. 11Ndatsala ndi Luka yekha basi. Mutenge Marko ndipo ubwere naye kuno, chifukwa amandithandiza mu utumiki wanga. 12Ndatumiza Tukiko ku Efeso. 13Pobwera, unditengere chofunda pamwamba chimene ndinachisiya kwa Kupro ku Trowa. Unditengerenso mabuku anga, makamaka aja azikopawa.

14Alekisandro, mmisiri wa zitsulo anandichitira zoyipa kwambiri. Ambuye adzamubwezera pa zimene anachita. 15Iwenso ukhale naye tcheru chifukwa anatsutsa kwambiri uthenga wathu.

16Podziteteza koyamba pa mlandu wanga, panalibe ndi mmodzi yemwe amene anandithandiza, koma aliyense anandithawa. Mulungu awakhululukire. 17Koma Ambuye anayima nane limodzi, ndipo anandipatsa mphamvu, kuti kudzera mwa ine, uthenga ulalikidwe kwambiri, ndikuti anthu a mitundu ina amve. Ndipo ndinalanditsidwa mʼkamwa mwa mkango. 18Ambuye adzandilanditsa ku chilichonse chofuna kundichita choyipa ndipo adzandisamalira bwino mpaka kundilowetsa chonse mu ufumu wake wakumwamba. Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya.

Mawu Otsiriza

19Pereka moni kwa Prisila ndi Akura pamodzi ndi banja lonse la Onesiforo. 20Erasto anatsalira ku Korinto. Trofimo ndinamusiya akudwala ku Mileto. 21Uyesetse kubwera kuno nthawi yozizira isanafike. Eubulo akupereka moni, ndiponso Pude, Lino, Klaudiya ndi abale onse nawonso akupereka moni.

22Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale ndi inu nonse.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

提摩太后书 4:1-22

务要传道

1在上帝和审判活人死人的基督耶稣面前,我凭基督的显现和祂的国郑重嘱咐你: 2无论时机好坏,都要坚持传道,以百般的忍耐和教导督责人,警戒人,勉励人。 3因为有一天,人们会厌倦纯正的教导,耳朵发痒,寻找许多迎合他们私欲的老师。 4他们掩耳不听真理,反而偏向无稽之谈。 5然而,你要谨慎行事,不怕吃苦,专心传道,尽忠职守。

6我的生命如同奉献在祭坛上的酒正倾倒出来,我离世的日子快要到了。 7那美好的仗,我打过了;当跑的路,我跑完了;所信的道,我持守住了。 8从此,有公义的冠冕为我预备,按公义审判的主会在祂来的那一天把它赐给我,不但会赐给我,也会赐给所有爱慕祂显现的人。

最后的嘱咐

9请你尽快到我这里来, 10因为底马贪爱世界,离弃我跑到帖撒罗尼迦去了。革勒士去了加拉太提多去了挞马太11只剩下路加一人在我身边。你要把马可一起带来,因为他在传道的工作上对我很有帮助。 12至于推基古,我派他到以弗所去了。 13你来的时候,要把我在特罗亚时留在加布的外衣带来,也要带来那些书卷,特别是那些羊皮卷。

14铜匠亚历山大做了许多恶事害我,主必按他的所作所为报应他。 15你也要提防他,因为他极力反对我们所传的道。

16我第一次在法庭申辩的时候,没有人帮助我,众人都离弃了我,但愿他们不会因此而获罪。 17然而主站在我身旁加给我力量,使我可以把福音清楚地传给外族人。主把我从狮子口里救了出来。 18主必救我脱离一切凶险,带我进入祂的天国。愿荣耀归给上帝,直到永永远远。阿们!

问候

19请代我问候百基拉亚居拉,也问候阿尼色弗一家。 20以拉都留在了哥林多,我把生病的特罗非摩留在了米利都21你要尽快在冬天之前赶到这里来。友布罗布田利奴革劳底亚和众弟兄姊妹都问候你。

22愿主与你的灵同在!愿恩典与你们同在!