2 Timoteyo 3 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 3:1-17

Zoopsa za Mʼmasiku Otsiriza

1Koma dziwa izi: Mʼmasiku otsiriza kudzafika nthawi zoopsa kwambiri. 2Anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, odzitama, onyada, achipongwe, osamvera makolo awo, osayamika, wopanda chiyero. 3Adzakhala wopanda chikondi, osakhululuka, osinjirira, osadziletsa, ankhanza, osakonda zabwino, 4opereka anzawo kwa adani awo, osaopa zoyipa, odzitukumula, okonda zowasangalatsa mʼmalo mokonda Mulungu. 5Adzakhala ndi maonekedwe achipembedzo koma mphamvu yake ndi kumayikana. Anthu amenewa uziwapewa.

6Iwowa ndi anthu aja amene amayendayenda mʼmakomo a anthu nʼkumanyenga akazi ofowoka mʼmaganizo, olemedwa ndi machimo ndiponso otengeka ndi zilakolako zoyipa zamitundumitundu, 7amaphunzira nthawi zonse koma samatha kuzindikira choonadi. 8Monga momwe Yanesi ndi Yambere anawukira Mose, momwemonso anthu amenewa amawukira choonadi. Nzeru zawo ndi zowonongeka ndipo pa za chikhulupiriro, ndi okanidwa. 9Koma sadzapita nazo patali kwambiri zimenezi, pakuti anthu onse adzaona kupusa kwawo monga anachitira Yanesi ndi Yambere.

Paulo Alimbikitsa Timoteyo

10Tsono iwe, umadziwa zonse zimene ndimaphunzitsa, makhalidwe anga, cholinga changa, chikhulupiriro changa, kuleza mtima kwanga, chikondi changa, ndi kupirira kwanga, 11mazunzo anga, masautso anga, monga zinandichitikira ku Antiokeya, ku Ikoniya ndi ku Lusitra. Ndinazunzika kwambiri. Koma Ambuye anandipulumutsa pa zonsezi. 12Kunena zoona, munthu aliyense amene akufuna kukhala moyo wolemekeza Mulungu mwa Khristu Yesu, adzazunzikadi, 13pomwe anthu oyipa ndi onyenga adzanka nayipirayipira, kunamiza ena, iwo nʼkumanamizidwanso. 14Koma iwe pitiriza zimene waziphunzira ndi kuzivomereza, chifukwa ukudziwa amene anakuphunzitsa zimenezi. 15Kuyambira uli wamngʼono wakhala ukudziwa Malemba Oyera, amene akhoza kukupatsa nzeru zokupulumutsa kudzera mʼchikhulupiriro cha mwa Yesu Khristu. 16Malemba onse anawalembetsa ndi Mulungu, ndipo othandiza pophunzitsa, podzudzula, pokonza cholakwika ndi polangiza za chilungamo 17kuti munthu wa Mulungu akonzekere bwino lomwe kugwira ntchito iliyonse yabwino.

Thai New Contemporary Bible

2ทิโมธี 3:1-17

ความอธรรมในวาระสุดท้าย

1แต่จงรู้ไว้ด้วยว่าจะเกิดกลียุคในวาระสุดท้าย 2ผู้คนจะรักตนเอง รักเงิน ชอบโอ้อวด หยิ่งยโส ชอบด่าว่า ไม่เชื่อฟังพ่อแม่ อกตัญญู ไม่บริสุทธิ์ 3ไม่มีความรัก ไม่ให้อภัย ชอบนินทาว่าร้าย ไม่มีการควบคุมตนเอง โหดร้าย ไม่รักความดี 4ทรยศหักหลัง หุนหันพลันแล่น ถือดี รักสนุกมากกว่ารักพระเจ้า 5ยึดถือทางพระเจ้าเพียงเปลือกนอกแต่กลับปฏิเสธฤทธิ์อำนาจของพระเจ้า อย่าไปคบคนแบบนี้

6พวกเขาคืบคลานไปตามบ้านต่างๆ จูงจมูกหญิงเบาปัญญาผู้บาปหนาซึ่งโอนเอนไปกับสารพัดตัณหาชั่ว 7หญิงเหล่านี้ใฝ่เรียนแต่ไม่สามารถรู้ถึงความจริงได้เลย 8เช่นเดียวกับที่ยันเนสกับยัมเบรส์ต่อต้านโมเสส คนเหล่านี้ก็ต่อต้านความจริง พวกเขาเป็นคนใจทราม ความเชื่อของเขาก็ไม่เป็นที่ยอมรับ 9แต่เขาจะไปได้ไม่ไกลเพราะความโง่เขลาของคนเหล่านี้จะปรากฏชัดแก่ทุกๆ คนเหมือนในกรณีของสองคนนั้น

เปาโลกำชับทิโมธี

10แต่ท่านรู้ถึงคำสอนทั้งปวงของข้าพเจ้า วิถีชีวิตของข้าพเจ้า เป้าหมายของข้าพเจ้า ความเชื่อ ความอดทน ความรัก ความเด็ดเดี่ยวมั่นคง 11การกดขี่ข่มเหง ความทุกข์ยาก ท่านรู้ถึงการถูกข่มเหงนานาประการที่เกิดกับข้าพเจ้าในเมืองอันทิโอก เมืองอิโคนียูม และเมืองลิสตรา ถึงกระนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้าก็ทรงช่วยข้าพเจ้าให้รอดพ้นจากสิ่งทั้งปวงเหล่านี้ 12อันที่จริงบรรดาผู้ที่ปรารถนาจะดำเนินชีวิตตามทางพระเจ้าในพระเยซูคริสต์จะถูกข่มเหง 13ขณะที่คนชั่วและคนหลอกลวงจะเสื่อมทรามลง ทั้งล่อลวงคนอื่นและถูกคนอื่นล่อลวง 14แต่ส่วนท่านจงดำเนินต่อไปในสิ่งที่ท่านได้เรียนรู้และได้เชื่อมั่น เพราะท่านรู้จักคนเหล่านั้นที่ท่านเรียนรู้จากเขา 15และรู้ว่าตั้งแต่เด็กมาแล้ว ท่านก็ได้รู้พระคัมภีร์ศักดิ์สิทธิ์ซึ่งสามารถทำให้ท่านมีปัญญาที่จะมาถึงความรอดได้โดยความเชื่อในพระเยซูคริสต์ 16พระคัมภีร์ทุกตอน3:16 หรือพระคัมภีร์ทั้งหมดได้รับการดลใจจากพระเจ้า และเป็นประโยชน์ในการสั่งสอน การว่ากล่าวตักเตือน การแก้ไขข้อบกพร่อง และการฝึกฝนในความชอบธรรม 17เพื่อเตรียมคนของพระเจ้าให้พรักพร้อมสำหรับการดีทุกอย่าง