2 Timoteyo 2 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 2:1-26

1Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu. 2Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena. 3Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu. 4Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira. 5Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo. 6Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola. 7Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.

8Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino 9umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo. 10Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha.

11Mawu oyenera kuwadalira ndi awa:

Ngati ife tinafa naye pamodzi,

tidzakhalanso moyo pamodzi naye.

12Ngati tinapirira,

tidzalamuliranso naye pamodzi.

Ngati ife timukana,

Iye adzatikananso.

13Ngati ndife osakhulupirika,

Iye adzakhalabe wokhulupirika

popeza sangathe kudzikana.

Kuthana ndi Aphunzitsi Onyenga

14Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo. 15Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola. 16Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera. 17Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto. 18Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena. 19Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”

20Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba. 21Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.

22Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa. 23Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano. 24Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa. 25Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi. 26Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.

Thai New Contemporary Bible

2ทิโมธี 2:1-26

1เหตุฉะนั้นลูกของข้าพเจ้าเอ๋ย ท่านจงเข้มแข็งในพระคุณซึ่งมีอยู่ในพระเยซูคริสต์ 2สิ่งต่างๆ ที่ท่านได้ยินข้าพเจ้าพูดต่อหน้าพยานหลายคนจงมอบหมายแก่ผู้ที่เชื่อถือได้ ซึ่งมีคุณสมบัติเหมาะสมที่จะสอนผู้อื่นด้วย 3จงทนต่อความยากลำบากร่วมกับเราเยี่ยงทหารที่ดีของพระเยซูคริสต์ 4ไม่มีทหารคนใดเข้าประจำการแล้วยังยุ่งเกี่ยวกับเรื่องฝ่ายพลเรือน เขาย่อมมุ่งทำให้ผู้บังคับบัญชาพอใจ 5เช่นกันนักกีฬาย่อมไม่ได้รับมงกุฎแห่งชัยชนะหากไม่แข่งขันตามกติกา 6กสิกรผู้ตรากตรำควรได้รับส่วนแบ่งของพืชผลก่อนใคร 7จงใคร่ครวญสิ่งที่ข้าพเจ้าได้พูดมา เพราะองค์พระผู้เป็นเจ้าจะประทานความเข้าใจอย่างถ่องแท้ในสิ่งทั้งปวงเหล่านี้แก่ท่าน

8จงระลึกถึงพระเยซูคริสต์ซึ่งทรงให้เป็นขึ้นจากตาย ทรงสืบเชื้อสายจากดาวิด นี่คือข่าวประเสริฐที่ข้าพเจ้าประกาศ 9เพื่อข่าวประเสริฐนี้ข้าพเจ้าจึงทนทุกข์อยู่ ถึงขนาดถูกล่ามโซ่เหมือนโจรผู้ร้าย แต่ไม่มีใครเอาโซ่ล่ามพระวจนะของพระเจ้าไว้ได้ 10ฉะนั้นข้าพเจ้ายอมทนทุกอย่างเพื่อเห็นแก่ผู้ที่ทรงเลือกสรรไว้ เพื่อว่าคนเหล่านั้นจะได้รับความรอดซึ่งอยู่ในพระเยซูคริสต์พร้อมด้วยศักดิ์ศรีนิรันดร์

11นี่เป็นคำกล่าวที่เชื่อถือได้คือ

ถ้าเราตายกับพระองค์

เราก็จะมีชีวิตกับพระองค์ด้วย

12ถ้าเราอดทน

เราก็จะได้ครองร่วมกับพระองค์ด้วย

ถ้าเราปฏิเสธพระองค์

พระองค์ก็จะทรงปฏิเสธเราด้วย

13ถ้าเราไม่สัตย์ซื่อ

พระองค์ก็ยังคงสัตย์ซื่อ

เพราะพระองค์ปฏิเสธพระองค์เองไม่ได้

คนงานที่พระเจ้าพอพระทัย

14จงหมั่นเตือนประชากรทั้งหลายให้ระลึกถึงสิ่งเหล่านี้ จงตักเตือนพวกเขาต่อหน้าพระเจ้าไม่ให้โต้เถียงกันเรื่องคำต่างๆ ซึ่งไร้ค่า มีแต่จะทำลายผู้ฟัง 15จงพยายามอย่างสุดกำลังที่จะให้ตัวท่านเป็นผู้ที่พระเจ้าทรงรับรอง เป็นคนงานที่ไม่ต้องอับอาย และใช้ถ้อยคำแห่งความจริงอย่างถูกต้อง 16จงหลีกห่างจากการพูดจาไร้สาระไม่ยำเกรงพระเจ้าซึ่งจะนำผู้ที่หมกมุ่นให้ยิ่งต่ำทรามลง 17คำสอนของพวกเขาแพร่ลามเหมือนเนื้อร้าย ฮิเมเนอัสกับฟีเลทัสก็อยู่ในพวกนี้ 18เขาทั้งสองเตลิดจากความจริง พวกเขากล่าวว่าการเป็นขึ้นจากตายได้ผ่านพ้นไปแล้ว และได้ทำลายความเชื่อของบางคนลง 19แต่รากฐานมั่นคงของพระเจ้าตั้งอยู่อย่างไม่คลอนแคลน ประทับตราด้วยข้อความที่ว่า “พระเจ้าทรงรู้จักบรรดาผู้ที่เป็นของพระองค์”2:19 กดว.16:5 และ “ทุกคนที่เอ่ยพระนามขององค์พระผู้เป็นเจ้าจงหลีกหนีจากความชั่วร้าย”

20ในบ้านหลังใหญ่ไม่ใช่มีแต่ภาชนะทองและเงินเท่านั้น แต่มีภาชนะไม้และดินด้วย บางชิ้นใช้ในงานที่ทรงเกียรติ บางชิ้นเพื่อใช้สอยธรรมดา 21ถ้าผู้ใดชำระตนให้พ้นจากสิ่งไร้ค่า เขาก็จะเป็นภาชนะอันทรงเกียรติ ได้รับการชำระให้บริสุทธิ์ มีประโยชน์สำหรับองค์เจ้านาย และถูกเตรียมไว้พร้อมเพื่อจะทำการดีทุกประการ

22ท่านจงหนีจากราคะตัณหาของคนหนุ่มและจงใฝ่หาความชอบธรรม ความเชื่อ ความรัก และสันติสุขร่วมกับบรรดาผู้ที่ร้องเรียกองค์พระผู้เป็นเจ้าด้วยใจบริสุทธิ์ 23อย่าข้องแวะกับการโต้แย้งต่างๆ อันโง่เขลาไร้สาระเพราะท่านรู้ว่าสิ่งเหล่านี้ก่อให้เกิดการทะเลาะวิวาท 24ฝ่ายผู้รับใช้ขององค์พระผู้เป็นเจ้าต้องไม่ทะเลาะวิวาท แต่เขาต้องสุภาพอ่อนโยนต่อทุกคน สามารถสอนผู้อื่นได้ ไม่เจ้าอารมณ์ 25เขาต้องชี้แจงอย่างสุภาพแก่บรรดาผู้ที่ต่อต้านเขาโดยหวังว่าพระเจ้าจะทรงให้คนเหล่านี้กลับใจเพื่อจะรู้ถึงความจริง 26และโดยหวังว่าคนเหล่านี้จะได้สติและหลุดพ้นจากกับดักของมารซึ่งได้จับพวกเขาไว้เป็นเชลยให้ทำตามความประสงค์ของมัน