2 Timoteyo 2 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 2:1-26

1Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu. 2Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena. 3Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu. 4Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira. 5Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo. 6Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola. 7Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.

8Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino 9umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo. 10Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha.

11Mawu oyenera kuwadalira ndi awa:

Ngati ife tinafa naye pamodzi,

tidzakhalanso moyo pamodzi naye.

12Ngati tinapirira,

tidzalamuliranso naye pamodzi.

Ngati ife timukana,

Iye adzatikananso.

13Ngati ndife osakhulupirika,

Iye adzakhalabe wokhulupirika

popeza sangathe kudzikana.

Kuthana ndi Aphunzitsi Onyenga

14Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo. 15Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola. 16Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera. 17Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto. 18Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena. 19Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”

20Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba. 21Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.

22Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa. 23Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano. 24Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa. 25Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi. 26Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.

New International Version

2 Timothy 2:1-26

The Appeal Renewed

1You then, my son, be strong in the grace that is in Christ Jesus. 2And the things you have heard me say in the presence of many witnesses entrust to reliable people who will also be qualified to teach others. 3Join with me in suffering, like a good soldier of Christ Jesus. 4No one serving as a soldier gets entangled in civilian affairs, but rather tries to please his commanding officer. 5Similarly, anyone who competes as an athlete does not receive the victor’s crown except by competing according to the rules. 6The hardworking farmer should be the first to receive a share of the crops. 7Reflect on what I am saying, for the Lord will give you insight into all this.

8Remember Jesus Christ, raised from the dead, descended from David. This is my gospel, 9for which I am suffering even to the point of being chained like a criminal. But God’s word is not chained. 10Therefore I endure everything for the sake of the elect, that they too may obtain the salvation that is in Christ Jesus, with eternal glory.

11Here is a trustworthy saying:

If we died with him,

we will also live with him;

12if we endure,

we will also reign with him.

If we disown him,

he will also disown us;

13if we are faithless,

he remains faithful,

for he cannot disown himself.

Dealing With False Teachers

14Keep reminding God’s people of these things. Warn them before God against quarreling about words; it is of no value, and only ruins those who listen. 15Do your best to present yourself to God as one approved, a worker who does not need to be ashamed and who correctly handles the word of truth. 16Avoid godless chatter, because those who indulge in it will become more and more ungodly. 17Their teaching will spread like gangrene. Among them are Hymenaeus and Philetus, 18who have departed from the truth. They say that the resurrection has already taken place, and they destroy the faith of some. 19Nevertheless, God’s solid foundation stands firm, sealed with this inscription: “The Lord knows those who are his,” and, “Everyone who confesses the name of the Lord must turn away from wickedness.”

20In a large house there are articles not only of gold and silver, but also of wood and clay; some are for special purposes and some for common use. 21Those who cleanse themselves from the latter will be instruments for special purposes, made holy, useful to the Master and prepared to do any good work.

22Flee the evil desires of youth and pursue righteousness, faith, love and peace, along with those who call on the Lord out of a pure heart. 23Don’t have anything to do with foolish and stupid arguments, because you know they produce quarrels. 24And the Lord’s servant must not be quarrelsome but must be kind to everyone, able to teach, not resentful. 25Opponents must be gently instructed, in the hope that God will grant them repentance leading them to a knowledge of the truth, 26and that they will come to their senses and escape from the trap of the devil, who has taken them captive to do his will.