2 Timoteyo 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Thai New Contemporary Bible

2ทิโมธี 1:1-18

1จดหมายฉบับนี้จากข้าพเจ้าเปาโลผู้เป็นอัครทูตของพระเยซูคริสต์โดยพระประสงค์ของพระเจ้าตามพระสัญญาแห่งชีวิตซึ่งอยู่ในพระเยซูคริสต์

2ถึงทิโมธีลูกที่รักของข้าพเจ้า

ขอพระคุณ พระเมตตา และสันติสุขจากพระเจ้าพระบิดาและพระเยซูคริสต์องค์พระผู้เป็นเจ้าของเรามีแก่ท่าน

ให้กำลังใจให้สัตย์ซื่อ

3เมื่อข้าพเจ้าระลึกถึงท่านในคำอธิษฐานอยู่เสมอทั้งวันทั้งคืน ข้าพเจ้าก็ขอบพระคุณพระเจ้าผู้ซึ่งข้าพเจ้ารับใช้อยู่ด้วยจิตสำนึกอันใสสะอาดเช่นเดียวกับบรรพบุรุษของข้าพเจ้า 4เมื่อหวนนึกถึงน้ำตาของท่าน ข้าพเจ้าก็อยากจะมาหาท่านเพื่อข้าพเจ้าจะได้เปี่ยมด้วยความชื่นชมยินดี 5ข้าพเจ้าคิดถึงความเชื่ออันจริงใจของท่าน ซึ่งตั้งแต่แรกนั้นก็มีอยู่ในโลอิสยายของท่านและในยูนีสมารดาของท่าน และข้าพเจ้าเชื่อว่าบัดนี้มีอยู่ในท่านเช่นกัน 6ด้วยเหตุนี้ข้าพเจ้าจึงขอเตือนท่านว่าจงทำให้ของประทานของพระเจ้าซึ่งมีอยู่ในตัวท่านผ่านทางการวางมือของข้าพเจ้านั้นรุ่งเรือง1:6 หรือพัดให้ติดไฟขึ้น 7เพราะพระเจ้าไม่ได้ทรงให้เรามีใจขลาดอาย แต่ประทานใจอันเปี่ยมด้วยฤทธิ์อำนาจ ความรัก และการรู้จักบังคับตนเองแก่เรา

8ดังนั้นอย่าละอายที่จะเป็นพยานเรื่ององค์พระผู้เป็นเจ้าของเราหรือละอายในตัวของข้าพเจ้าผู้ถูกจองจำเพื่อพระองค์ แต่จงร่วมทนทุกข์กับข้าพเจ้าเพื่อข่าวประเสริฐโดยฤทธิ์อำนาจของพระเจ้า 9ผู้ทรงช่วยเราให้รอดและทรงเรียกเรามาสู่ชีวิตอันบริสุทธิ์ ไม่ใช่เพราะการกระทำใดๆ ของเราแต่เพราะพระประสงค์และพระคุณของพระองค์เอง พระคุณนี้ได้ประทานแก่เราในพระเยซูคริสต์ตั้งแต่ก่อนจุดเริ่มต้นของเวลา 10แต่บัดนี้ทรงให้ประจักษ์แจ้งโดยการเสด็จมาของพระเยซูคริสต์พระผู้ช่วยให้รอดของเรา ผู้ได้ทรงทำลายความตายและทรงนำชีวิตกับความเป็นอมตะมาสู่ความสว่างโดยทางข่าวประเสริฐ 11และทรงแต่งตั้งข้าพเจ้าให้เป็นผู้ป่าวประกาศ เป็นอัครทูต และเป็นผู้สอนข่าวประเสริฐนี้ 12นั่นเป็นเหตุให้ข้าพเจ้าทนทุกข์อย่างที่เป็นอยู่ กระนั้นข้าพเจ้าก็ไม่ละอายเพราะข้าพเจ้ารู้จักพระองค์ที่ข้าพเจ้าเชื่อ และมั่นใจว่าพระองค์ทรงสามารถรักษาสิ่งที่ข้าพเจ้ามอบไว้กับพระองค์จนถึงวันนั้นได้

13จงยึดถือแบบอย่างของคำสอนอันมีหลักที่ท่านได้ยินจากข้าพเจ้าด้วยความเชื่อและความรักในพระเยซูคริสต์ 14สำหรับความจริงแห่งข่าวประเสริฐที่ท่านได้รับมอบหมายไว้นั้น จงพิทักษ์รักษาไว้โดยการช่วยเหลือจากพระวิญญาณบริสุทธิ์ผู้สถิตในเราทั้งหลาย

15ท่านก็ทราบว่าทุกคนในแคว้นเอเชียทิ้งข้าพเจ้าไปหมด รวมทั้งฟีเจลัสกับเฮอร์โมเกเนส

16ขอพระเจ้าทรงสำแดงพระเมตตาแก่ครอบครัวของโอเนสิโฟรัสเพราะเขาทำให้ข้าพเจ้าชื่นใจบ่อยครั้งและไม่ละอายเลยที่ข้าพเจ้าถูกจองจำอยู่ 17ตรงกันข้ามเมื่อเขาอยู่ในกรุงโรม เขาพยายามเที่ยวสืบหาข้าพเจ้าจนพบ 18ขอพระเจ้าทรงให้เขาได้รับพระเมตตาจากองค์พระผู้เป็นเจ้าในวันนั้นด้วยเถิด! ท่านก็ทราบดีว่าเมื่ออยู่ที่เมืองเอเฟซัสเขาได้ช่วยเหลือข้าพเจ้าในหลายๆ ด้าน