2 Timoteyo 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Persian Contemporary Bible

دوم تيموتائوس 1:1-18

سلام و درود از پولس

1از طرف من، پولس، كه طبق درخواست خدا فرستادهٔ عيسی مسيح هستم، و مأموريت يافته‌ام كه اين وعدهٔ خدا را در همه جا اعلام كنم كه هر كه به مسيح ايمان آورد، زندگی جاويد خواهد يافت؛

2به فرزند عزيزم تيموتائوس.

از درگاه خدای پدر و خداوندمان عيسی مسيح، طالب فيض و رحمت و آرامش برای تو می‌باشم.

تشويق به وفاداری

3چقدر خدا را برای وجود تو شكر می‌كنم! هر روز برايت دعا می‌كنم و بسياری از شبها تا دير وقت به خدای خود التماس می‌كنم كه تو را مورد لطف بی‌پايان خود قرار دهد. او خدای اجداد من و خدای من است، و تنها آرزويم در زندگی اينست كه رضايت او را فراهم سازم.

4نمی‌دانی چقدر مشتاق ديدارت هستم و تا چه حد از ديدن مجدد تو شاد خواهم شد، زيرا هميشه اشكهايی را كه به هنگام وداع می‌ريختی، به یاد دارم. 5هيچگاه از ياد نمی‌برم چه ايمان خالصی به خداوند داشتی، درست مانند مادرت «یونیکی» و مادر بزرگت «لوئيز»؛ و اطمينان دارم كه حالا نيز ايمانت به همان اندازه مستحكم است. 6به همين جهت، می‌خواهم يادآوری كنم كه آن عطای الهی را كه در توست شعله‌ور سازی، همان عطايی كه خدا به هنگام دعا و قرار گرفتن دستهای من بر سر تو، در وجود تو قرار داد. 7زيرا آن روحی كه خدا به ما داده است، در ما ترس بوجود نمی‌آورد، بلكه ما را سرشار از محبت و قدرت می‌سازد و ما را ياری می‌دهد تا بتوانيم خود را تحت انضباط قرار دهيم. 8اگر اين عطای الهی را در وجودت شعله‌ور نگاه داری، هرگز بيم نخواهی داشت از اينكه به مردم اعلام كنی كه مسيح نجات دهندهٔ همه است؛ در ضمن، شرمگين نخواهی شد كه از من به عنوان دوست خود ياد كنی، دوستی كه به خاطر مسيح در زندان است. بلكه برعكس، خودت نيز حاضر خواهی بود به خاطر انجيل مسيح همراه من رنج و زحمت بكشی، و خدا تو را در اين زحمات تقويت خواهد نمود.

9اين خداست كه ما را نجات داد و برای خدمت خود برگزيد، نه به دلیل لياقت ما، بلكه به سبب اينكه پيش از آفرينش جهان اراده فرموده بود لطف و محبت خود را بوسيلهٔ عيسی مسيح به ما نشان دهد. 10و حال، با ظهور نجات دهنده‌مان عيسی مسيح، ارادهٔ او آشكار شده است؛ او قدرت مرگ را در هم شكست، و به ما راه ورود به زندگی جاويد را نشان داد كه همانا ايمان آوردن به پيغام انجيل اوست؛ 11و برای اعلام و تعليم همين پيغام است كه خدا مرا برگزيده تا رسول و فرستادهٔ او در ميان غيريهوديان باشم. 12به همين دليل است كه در اين زندان متحمل زحمات هستم، اما شرمگين نيستم زيرا می‌دانم به چه كسی ايمان آورده‌ام و يقين دارم كه او می‌تواند امانتی را كه به او سپرده‌ام، تا روز بازگشت خود محفوظ نگاه دارد.

13به سخنان و تعاليم صحيحی كه از من شنيدی، محكم بچسب و از آنها سرمشق بگير، بخصوص از ايمان و محبتی كه عيسی مسيح عطا می‌كند. 14آن امانت نيكو، يعنی عطای الهی را به كمک روح‌القدس كه در وجود تو ساكن است، حفظ كن.

15همانطور كه می‌دانی، تمام مسيحيانی كه از ايالت «آسيا» به اينجا آمده بودند، مرا به حال خود گذاشته و رفته‌اند؛ حتی «فيجلوس» و «هرموجنس» نيز مرا ترک گفته‌اند. 16خداوند «اُنيسيفوروس» و خانوادهٔ او را مورد لطف و رحمت خود قرار دهد، زيرا بارها به ديدن من آمد و باعث دلگرمی و شادی من گرديد. او هيچگاه از زندانی بودن من عار نداشت، 17بلكه به محض رسيدن به روم، همه جا به دنبال من گشت تا اينكه مرا پيدا كرد. 18خداوند در روز بازگشت مسيح بر او رحمت فرمايد. تو خودت به خوبی آگاهی كه اين مرد در «اَفَسُس» نيز چقدر به من خدمت كرد.