2 Timoteyo 1 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Swedish Contemporary Bible

2 Timotheosbrevet 1:1-18

Hälsning

1Från Paulus, som genom Guds vilja är apostel1:1 Eller sändebud. åt Kristus1:1 Se not till Matt 1:1. Jesus, i enlighet med löftet om livet som finns i Kristus Jesus.

2Till Timotheos, mitt kära barn1:2 Paulus kallade Timotheos sitt barn, eftersom han hade fört honom till tro på Jesus. Jfr 1 Tim 1:2..

Nåd, barmhärtighet och frid från Gud, Fadern, och Kristus Jesus, vår Herre.

Var trogen i din uppgift

3Jag tackar Gud, som jag liksom mina förfäder tjänar, med rent samvete, när jag dag och natt ständigt kommer ihåg dig i mina böner.

4Jag minns dina tårar och längtar efter att få se dig igen och fyllas av glädje. 5Jag minns också den uppriktiga tro du har, den som fanns hos din mormor Lois och din mor Eunike. Jag är övertygad om att samma tro nu finns i dig.

6Därför vill jag påminna dig om att blåsa liv i den nådegåva Gud gav dig, när jag lade mina händer på dig. 7Gud har inte gett oss en modlöshetens ande, utan kraftens, kärlekens och självbehärskningens. 8Därför ska du inte skämmas för att vittna om vår Herre, och inte heller skämmas över mig som sitter i fängelse för hans skull. Var beredd att lida för evangeliet du också, för Gud ska ge dig kraft.

9Han har räddat oss och kallat oss med en helig kallelse, inte på grund av våra gärningar, utan på grund av sitt beslut och sin nåd, som han gav oss i Kristus Jesus redan före tidens början, 10men som nu har uppenbarats när vår Frälsare Kristus Jesus trätt fram. Han har brutit dödens makt och fört liv och oförgänglighet fram i ljuset genom evangeliet, 11som jag har utsetts att vara apostel, förkunnare och lärare för. 12Det är också därför som jag får lida. Men jag skäms inte, för jag vet vem jag tror på, och jag är säker på att han också kan bevara det som har anförtrotts mig, ända till den dagen.

13Ta det som du har hört från mig som modell för en sund undervisning, i tro och kärlek genom Kristus Jesus. 14Bevara genom den heliga Anden som bor i oss det goda som du är anförtrodd.

15Som du vet har alla i provinsen Asien1:15 Provinsen Asien var en romersk provins i nuvarande Turkiet. Huvudstaden hette Efesos. svikit mig, även Fygelos och Hermogenes. 16Må Herren visa barmhärtighet mot Onesiforos och alla i hans hus, för han har ofta uppmuntrat mig och inte skämts för mina kedjor. 17När han kom till Rom letade han efter mig överallt tills han hittade mig. 18Må Herren visa barmhärtighet mot honom på den dagen. Dessutom var han till enorm hjälp i Efesos, det vet du bättre än någon annan.