2 Timoteyo 1 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Knijga O Kristu

2 Timoteju 1:1-18

1Ovo je pismo od Pavla, apostola Krista Isusa Božjom voljom, poslanoga da navješćuje život koji je Bog obećao po vjeri u Krista Isusa.

2Mojemu ljubljenom sinu Timoteju.

Neka ti je milost, milosrđe i mir od našega Boga Oca i Gospodina Isusa Krista.

Poticaj na vjernost

3Timoteju, zahvaljujem za tebe Bogu, kojemu služim čiste savjesti kao i moji preci, dok se bez prestanka, danonoćno, molim za tebe. 4Kad se sjetim tvojih suza, obuzme me čežnja da te opet vidim i da se razveselim.

5Znam kakvu iskrenu vjeru u Boga imaš—kao najprije tvoja baka Loida, a zatim i tvoja mati Eunika. 6Zato te molim: raspiruj duhovni dar koji ti je Bog dao kad sam na tebe položio ruke. 7Jer Bog nam nije dao duha bojažljivosti, već Duha snage, ljubavi i razboritosti. 8Ne srami se govoriti o našemu Gospodinu niti o meni, iako sam u zatvoru! Budi spreman sa mnom trpjeti zaradi navješćivanja Radosne vijesti. Bog će ti za to dati snage.

9On nas je spasio i pozvao nas da živimo svetim životom—ne zato što smo to svojim djelima zaslužili, nego zato što je to bio njegov naum još od vječnosti: da nam daruje svoju milost u Isusu Kristu. 10Sada nam je sve to objavio dolaskom našega Spasitelja Isusa Krista, koji je skršio moć smrti i učinio da kroz Radosnu vijest zasja život i besmrtnost. 11Bog me je postavio da budem propovjednik, apostol i učitelj te Radosne vijesti.

12Zato i trpim ovdje u tamnici. Ali ne stidim se toga jer poznajem onoga u koga se pouzdajem i siguran sam da je on kadar sačuvati povjereno do dana svojega dolaska.

13Uzor neka ti bude zdravo učenje koje si od mene čuo u vjeri i ljubavi u Kristu Isusu. 14Dobro čuvaj blago koje ti je povjereno s pomoću Svetoga Duha koji prebiva u nama.

15Kao što znaš, svi kršćani u Maloj Aziji su me napustili—među njima i Figel i Hermogen. 16Neka Gospodin milosrđem daruje Oneziforov dom jer me je često znao osvježiti svojim posjetom. Nije se sramio što sam u zatvoru. 17Naprotiv, kad je došao u Rim, brižno me potražio i pronašao. 18Neka mu Gospodin daruje milosrđe na dan Kristova dolaska. Znaš koliko mi je puta pomogao u Efezu.