2 Timoteyo 1 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Timoteyo 1:1-18

1Paulo mtumwi wa Khristu Yesu mwa chifuniro cha Mulungu. Anandituma kuti ndilalike za lonjezo la moyo umene uli mwa Khristu Yesu.

2Kwa Timoteyo, mwana wanga wokondedwa:

Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye athu Yesu Khristu.

Chilimbikitso Pokhala Wokhulupirika

3Ndikuyamika Mulungu amene ndimamutumikira ndi chikumbumtima chosatsutsika, monga momwe ankachitira makolo anga. Usiku ndi usana ndimakukumbukira mosalekeza mʼmapemphero anga. 4Ndikamakumbukira misozi yako, ndimalakalaka nditakuona kuti ndidzazidwe ndi chimwemwe. 5Ndakumbukira za chikhulupiriro chako choona chimene chinayamba mwa agogo ako a Loisi ndi mwa amayi ako Yunike ndipo ndikutsimikiza mtima kuti chilinso mwa iwe.

Kumvera Paulo ndi Uthenga Wabwino

6Nʼchifukwa chake ndikukukumbutsa kuti upemerere monga amachitira moto, mphatso imene Mulungu anakupatsa nditakusanjika manja. 7Pakuti Mzimu amene Mulungu anatipatsa, si Mzimu wotipatsa manyazi, koma Mzimu wotipatsa mphamvu, chikondi ndi kudzisunga.

8Choncho usachite manyazi kuchitira umboni Ambuye athu, kapena kuchita manyazi chifukwa cha ine wamʼndende. Koma umve nane zowawa chifukwa cha Uthenga Wabwino, mothandizidwa ndi mphamvu za Mulungu. 9Iye anatipulumutsa ndipo anatiyitanira ku moyo oyera mtima, osati chifukwa cha chilichonse chimene tinachita, koma chifukwa cha chikonzero ndi chisomo chake. Chisomo chimenechi anatipatsa ife mwa Khristu Yesu nthawi isanayambe. 10Koma tsopano Mulungu watiwululira kudzera mʼkuoneka kwa Mpulumutsi wathu, Khristu Yesu, amene anathetsa mphamvu za imfa ndipo mwa Uthenga Wabwino anaonetsa poyera moyo umene sungafe. 11Ine ndinasankhidwa kukhala wamthenga, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wa Uthenga Wabwinowu. 12Nʼchifukwa chake ndikuvutika monga ndililimu. Komabe zimenezi sizikundichititsa manyazi, popeza ndikumudziwa amene ndamukhulupirira ndipo ndikutsimikiza mtima kuti akhoza kusamalira chimene ndinamusungitsa mpaka tsiku lijalo.

13Zimene unamva kwa ine, uzisunge kuti zikhale chitsanzo cha chiphunzitso choona, mwa chikhulupiriro ndi chikondi mwa Khristu Yesu. 14Samalira bwino zokoma zimene anakusungitsa. Uzisamalire mothandizidwa ndi Mzimu Woyera amene amakhala mwa ife.

Zitsanzo za Kusakhulupirika ndi Kukhulupirika

15Iwe udziwa kuti onse a mʼchigawo cha Asiya anandithawa, kuphatikizapo Fugelo ndi Herimogene omwe.

16Mulungu achitire chifundo banja lonse la Onesiforo chifukwa ankandisangalatsa kawirikawiri ndipo sankachita nane manyazi ngakhale ndinali womangidwa ndi maunyolo. 17Mʼmalo mwake, atangofika ku Roma, anandifunafuna ndipo anandipeza. 18Ambuye amulole kuti adzalandire chifundo kwa Ambuye pa tsiku lijalo! Ukudziwa bwino momwe iye anandithandizira mʼnjira zosiyanasiyana ku Efeso.

Священное Писание

2 Тиметею 1:1-18

Приветствие

1От Паула, посланника Исы Масиха1:1 Масих (переводится как «Помазанник») – праведный Царь и Освободитель, Спаситель, обещанный Всевышним ещё в Таурате, Забуре и Книге Пророков., избранного по воле Всевышнего и посланного возвещать обещанную Им жизнь в единении с Исой Масихом.

2Моему дорогому сыну Тиметею.

Благодать, милость и мир тебе от Небесного Отца и нашего Повелителя Исы Масиха.

Благодарность и ободрение

3Я благодарю Всевышнего, Которому служу с чистой совестью, как это делали и мои праотцы, когда непрестанно вспоминаю о тебе в своих молитвах, которые я совершаю день и ночь. 4Я вспоминаю твои слёзы и очень хочу увидеть тебя: эта встреча крайне обрадовала бы меня. 5Я вспоминаю и о твоей искренней вере: так верили и твоя бабушка Лоида, и твоя мать Эвника, и убеждён, что эта же вера живёт и в тебе. 6По этой причине раздуй угольки твоего дара, который ты получил от Всевышнего через возложение моих рук. 7Ведь Всевышний не вселил в наши сердца страх, но дал нам силу, любовь и благоразумие.

8Поэтому не бойся говорить о нашем Повелителе и не стыдись того, что я нахожусь в заключении за Него. Наоборот, раздели со мной страдания за Радостную Весть, положившись на силу Всевышнего. 9Всевышний спас нас и призвал нас Своим святым призывом не по нашим заслугам, но для исполнения Своей цели и по Своей благодати, данной нам через Ису Масиха ещё до начала времён. 10И теперь мы увидели эту благодать, когда пришёл наш Спаситель Иса Масих, Который уничтожил смерть и через Радостную Весть показал новую жизнь и бессмертие. 11И я был поставлен глашатаем, посланником Масиха и учителем этой Радостной Вести. 12За это я и страдаю сейчас, но не стыжусь этого, потому что знаю, в Кого я поверил, и знаю, что Он способен сохранить то, что мне доверил1:12 Или: «то, что я доверил Ему». до дня Его возвращения.

13Пусть образцом правильного учения будет для тебя то, что ты услышал от меня. Живи с верой и любовью в единении с Исой Масихом. 14Пусть Святой Дух, живущий в нас, поможет тебе сберечь то доброе, что было тебе доверено.

15Все в провинции Азия1:15 Здесь имеется в виду не материк, а римская провинция на западе Малой Азии (часть современной территории Турции), которая позднее дала своё название материку. оставили меня, включая Фигела и Гермогена; тебе это известно.

16Пусть Повелитель проявит милость к дому Онисифора, ведь он так часто ободрял меня, не стыдясь того, что я нахожусь в цепях. 17Напротив, когда он был в Риме, то старательно разыскивал меня и нашёл. 18Пусть же Повелитель помилует его в день Своего возвращения. А как много он помог мне в Эфесе, ты хорошо знаешь.