2 Samueli 7 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 7:1-29

Lonjezo la Mulungu kwa Davide

1Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira, 2mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”

3Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”

4Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,

5“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo? 6Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti. 7Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’ ”

8“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli. 9Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi. 10Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja, 11monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse.

“ ‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako: 12Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake. 13Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya. 14Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu. 15Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu. 16Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’ ”

17Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.

Pemphero la Davide

18Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati:

“Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?” 19Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?

20Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu. 21Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.

22Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu. 23Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto? 24Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.

25“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera, 26kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.

27“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere. 28Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu. 29Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

New Russian Translation

2 Царств 7:1-29

Божье обещание Давиду

1После того как царь поселился в своем дворце и Господь дал ему покой от всех окружающих его врагов, 2он сказал пророку Нафану:

– Смотри, я живу во дворце из кедра, а Божий ковчег остается в шатре.

3Нафан ответил царю:

– Иди и делай все, что у тебя на сердце, потому что Господь с тобой.

4В ту ночь к Нафану было слово Господа:

5– Пойди и скажи Моему слуге Давиду: «Так говорит Господь: Разве ты – тот, кто построит Мне дом для Моего обитания? 6Я не жил в доме с того дня, как вывел израильтян из Египта и до сегодняшнего дня, но странствовал в шатре и в скинии. 7Где бы Я ни ходил со всеми израильтянами, разве Я говорил с каким-либо из их родов7:7 Или: «кому-нибудь из их правителей»., которым Я повелел пасти Мой народ Израиля: „Почему вы не построили Мне дом из кедра?“»

8Итак, скажи Моему слуге Давиду: «Так говорит Господь Сил: Я взял тебя, когда ты смотрел и ухаживал на пастбище за овцами, чтобы ты стал правителем Моего народа Израиля. 9Я был с тобой, куда бы ты ни ходил, и сокрушил перед тобой всех твоих врагов. Я уподоблю твое имя именам великих людей земли. 10Я устрою место для Своего народа, Израиля, и укореню его, чтобы ему иметь свой дом, и никто его больше не тревожил. Нечестивые больше не будут притеснять его, как прежде, 11с того времени, как Я поставил судей над Своим народом, Израилем. Я также дам тебе покой от всех твоих врагов.

Господь объявляет тебе, что Сам утвердит твой дом. 12Когда твои дни завершатся и ты упокоишься со своими предками, Я возведу на престол твоего потомка, того, кто произойдет от тебя и упрочу его царство. 13Он построит дом для Моего имени, и Я упрочу престол его царства навеки. 14Я буду ему Отцом, и он будет Мне сыном7:12-14 Эти слова также являются пророчеством об Иисусе Христе (см. Лк. 1:32; Рим. 1:3; Евр. 1:5).. Когда он согрешит, Я накажу его розгой людской, ударами, наносимыми людьми. 15Но Я не отниму от него Своей милости, как отнял ее от Саула, которого Я отверг ради тебя. 16Твой дом и твое царство будут непоколебимы предо Мной7:16 Так в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «перед тобой»; ср. ст. 26 и 29. вовеки; твой престол будет упрочен навеки».

17Нафан пересказал Давиду все слова этого откровения.

Молитва Давида

(1 Пар. 17:16-27)

18Тогда царь Давид вошел, сел перед Господом и сказал:

– Кто я, о Владыка Господи, и что такое моя семья, что Ты так возвеличил меня? 19И словно этого не было достаточно в Твоих глазах, о Владыка Господи, Ты еще рассказал о будущем дома Твоего слуги. И это будет Закон для людей7:19 Смысл этой фразы в еврейском тексте неясен., о Владыка Господи.

20Что еще может сказать Тебе Давид? Ведь Ты знаешь Твоего слугу, Владыка Господи! 21Ради Твоего слова и по воле Своей Ты совершил это великое дело и открыл его Своему слуге.

22Как Ты велик, Владыка Господи! Нет подобного Тебе и нет Бога, кроме Тебя, как слышали мы своими ушами. 23И кто подобен народу Твоему, Израилю, единственному народу на земле, к которому приходил Бог, чтобы выкупить его и сделать Своим народом? Чтобы все узнали имя Твое, Ты совершил великие и ужасные дела, выкупив Свой народ из Египта и изгнав перед ним другие народы и их богов. 24Ты сделал Израиль Своим собственным народом навеки, и Ты, Господи, стал его Богом.

25И теперь, Господи Боже, пусть обещание, которое Ты дал о Своем слуге и его доме, утвердится навеки, и сделай, как Ты обещал. 26Пусть возвеличится Твое имя вовеки, чтобы люди говорили: «Господь Сил – Бог над Израилем!» И дом Твоего слуги Давида утвердится пред Тобой.

27О Господь Сил, Бог Израиля, Ты открыл это Своему слуге, говоря: «Я устрою тебе дом». Поэтому Твой слуга набрался смелости принести Тебе эту молитву. 28О Владыка Господи, Ты – Бог! Твои слова истинны, и Ты обещал Своему слуге это благо. 29Пусть же станет Тебе угодно благословлять дом Твоего слуги, чтобы он был перед Тобой вечно. Ведь Ты, Владыка Господи, сказал это, и дом Твоего слуги будет благословен навеки от Твоего благословения!