2 Samueli 23 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 23:1-39

Mawu Otsiriza a Davide

1Nawa mawu otsiriza a Davide:

“Mawu a Davide mwana wa Yese,

mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba,

munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo,

woyimba nyimbo za Israeli:

2“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine;

mawu ake anali pakamwa panga.

3Mulungu wa Israeli anayankhula,

Thanthwe la Israeli linati kwa ine:

‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo,

pamene alamulira moopa Mulungu,

4amakhala ngati kuwala kwa mmamawa,

mmawa wopanda mitambo,

monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa

imene imameretsa udzu mʼnthaka.’

5“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu?

Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine,

lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse?

Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa,

ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?

6Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga,

imene sitengedwa ndi manja.

7Aliyense amene wayikhudza mingayo

amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo;

nayitentha pa moto.”

Ankhondo Otchuka a Davide

8Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide:

Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.

9Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo. 10Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.

11Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo. 12Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.

13Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu. 14Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu. 15Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!” 16Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova. 17Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo.

Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.

18Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja. 19Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.

20Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango. 21Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe. 22Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja. 23Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.

24Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa:

Asaheli mʼbale wa Yowabu,

Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,

25Sama Mharodi,

Elika Mherodi,

26Helezi Mpaliti,

Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,

27Abiezeri wa ku Anatoti,

Sibekai Mhusati,

28Zalimoni Mwahohi,

Maharai Mnetofa,

29Heledi mwana wa Baana Mnetofa,

Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,

30Benaya Mpiratoni,

Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.

31Abi-Aliboni Mwaribati,

Azimaveti Mbarihumi,

32Eliyahiba Msaaliboni,

ana a Yaseni,

Yonatani, 33mwana wa Sama Mharari,

Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,

34Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati,

Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,

35Heziro wa ku Karimeli,

Paarai Mwaribi,

36Igala mwana wa Natani wa ku Zoba,

mwana wa Hagiri,

37Zeleki Mwamoni,

Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,

38Ira Mwitiri,

Garebu Mwitiri,

39ndi Uriya Mhiti.

Onse pamodzi analipo 37.

Nueva Versión Internacional

2 Samuel 23:1-39

Últimas palabras de David

1Estas son las últimas palabras de David:

«Mensaje de David, hijo de Isaí,

dulce cantor de Israel;

hombre exaltado por el Altísimo

y ungido por el Dios de Jacob.

2»El Espíritu del Señor habló por medio de mí;

puso sus palabras en mi lengua.

3El Dios de Israel habló,

la Roca de Israel me dijo:

“El que gobierne a la gente con justicia,

el que gobierne en el temor de Dios,

4será como la luz de la aurora

en un amanecer sin nubes,

que tras la lluvia resplandece

para que brote la hierba en la tierra”.

5»Dios ha establecido mi casa;

ha hecho conmigo un pacto eterno,

bien reglamentado y seguro.

Dios hará que brote mi salvación

y que se cumpla todo mi deseo.

6Pero los malvados son como espinos que se desechan;

nadie los toca con la mano.

7Se recogen con un hierro o con el asta de una lanza

y ahí el fuego los consume».

Héroes en el ejército de David

23:8-391Cr 11:10-41

8Estos son los nombres de los soldados más valientes de David:

Joseb Basébet el tacmonita, que era el principal de los tres más famosos, en una batalla mató con su lanza23:8 mató con su lanza (mss. de LXX; véase 1Cr 11:11); Adino el eznita mató (TM). a ochocientos hombres.

9En segundo lugar estaba Eleazar, hijo de Dodó, el ajojita, que también era uno de los tres más famosos. Estuvo con David cuando desafiaron a los filisteos que se habían concentrado en Pasdamín23:9 en Pasdamín (texto probable; véase 1Cr 11:13); allí (TM). para la batalla. Los israelitas se retiraron, 10pero Eleazar se mantuvo firme y derrotó a tantos filisteos que, por la fatiga, la mano se le quedó pegada a la espada. Aquel día el Señor dio una gran victoria. Las tropas regresaron adonde estaba Eleazar, pero solo para tomar los despojos.

11El tercer valiente era Sama, hijo de Agué, el ararita. En cierta ocasión, los filisteos formaron sus tropas23:11 formaron sus tropas. Alt. se concentraron en Lejí. en un campo sembrado de lentejas. El ejército de Israel huyó ante ellos, 12pero Sama se plantó en medio del campo y lo defendió, derrotando a los filisteos. El Señor les dio una gran victoria.

13En otra ocasión, tres de los treinta más valientes fueron a la cueva de Adulán, donde estaba David. Era el comienzo de la siega y una tropa filistea acampaba en el valle de Refayin. 14David se encontraba en su fortaleza. En ese tiempo había una guarnición filistea en Belén. 15Como David tenía mucha sed, exclamó: «¡Ojalá pudiera yo beber agua del pozo que está a la entrada de Belén!». 16Entonces los tres valientes se metieron en el campamento filisteo, sacaron agua del pozo de Belén y se la llevaron a David. Pero él no quiso beberla, sino que derramó el agua en honor al Señor 17y declaró solemnemente: «¡Que el Señor me libre de beberla! ¡Eso sería como beber la sangre de hombres que han puesto su vida en peligro!». Y no quiso beberla.

Tales hazañas hicieron estos tres héroes.

18Abisay, el hermano de Joab, hijo de Sarvia, estaba al mando de los tres y ganó fama entre ellos. En cierta ocasión, lanza en mano atacó y mató a trescientos hombres. 19Se destacó más que los tres valientes y llegó a ser su comandante, pero no fue contado entre ellos.

20Benaías, hijo de Joyadá, era un guerrero de Cabsel que realizó muchas hazañas. Derrotó a dos de los mejores hombres23:20 dos de los mejores hombres. Alt. los dos [hijos] de Ariel. de Moab y, en otra ocasión, cuando estaba nevando, se metió en una cisterna y mató un león. 21También derrotó a un egipcio de gran estatura. El egipcio empuñaba una lanza, pero Benaías, que no llevaba más que un palo, le arrebató la lanza y lo mató con ella. 22Tales hazañas hizo Benaías, hijo de Joyadá. También él ganó fama como los tres valientes, 23pero no fue contado entre ellos, aunque se destacó más que los treinta valientes. Además, David lo puso al mando de su guardia real.

24Entre los treinta valientes estaban:

Asael, hermano de Joab;

Eljanán, hijo de Dodó, que era de Belén;

25Sama, el jarodita;

Elicá, el jarodita;

26Heles, el paltita;

Irá, hijo de Iqués, el tecoíta;

27Abiezer, el anatotita;

Mebunay, el jusatita;

28Zalmón, el ajojita;

Maray, el netofatita;

29Jéled;23:29 Jéled (mss. hebreos; véase 1Cr 11:30); Jéleb (TM). hijo de Baná, el netofatita;

Itay, hijo de Ribay, que era de Guibeá en el territorio de Benjamín;

30Benaías, el piratonita;

Hiday, que era de los arroyos de Gaas;

31Abí Albón, el arbatita;

Azmávet, el bajurinita;

32Elijaba, el salbonita;

los hijos de Jasén;

Jonatán, hijo de23:32 Jonatán, hijo de (mss. de LXX); Jonatán (TM). 33Sama, el ararita;

Ahían, hijo de Sarar, el ararita;

34Elifelet, hijo de Ajasbay, el macateo;

Elián, hijo de Ajitofel, el guilonita;

35Jezró, que era de Carmel;

Paray, el arbita;

36Igal, hijo de Natán, que era de Sobá;

el hijo de Hagrí;23:36 el hijo de Hagrí (mss. de LXX; véase 1Cr 11:38); Baní el, gadita (TM).

37Sélec, el amonita;

Najaray, el berotita, que fue escudero de Joab, hijo de Sarvia;

38Ira, el itrita;

Gareb, el itrita,

39y Urías, el hitita.

En total fueron treinta y siete.