2 Samueli 21 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 21:1-22

Agibiyoni Abwezera

1Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide kunali njala kwa zaka zitatu zotsatana. Kotero Davide anapemphera kwa Yehova. Yehova anati, “Izi zachitika chifukwa chakuti Sauli ndi banja lake akanali ndi mlandu wakupha Agibiyoni.”

2Mfumu inayitanitsa Agibiyoni ndipo inayankhula nawo. (Tsono Agibiyoni sanali Aisraeli, koma otsala mwa Aamori. Aisraeli analumbira kuwasiya ndi moyo, koma Sauli chifukwa cha chikondi cha pa Israeli ndi Yuda, anafuna kuwawonongeratu). 3Davide anafunsa Agibiyoni kuti, “Kodi ine ndikuchitireni chiyani? Ndipepese bwanji kuti inu mudalitse cholowa cha Yehova?”

4Agibiyoni anamuyankha kuti, “Ife tilibe ufulu woti nʼkulamula Sauli ndi banja lake kuti atipatse siliva kapena golide, tilibenso ufulu woti nʼkupha wina aliyense mu Israeli.”

Davide anafunsa, “Mukufuna ine ndikuchitireni chiyani?”

5Iwo anayankha mfumu kuti, “Tsono za munthu amene anatiwononga ndi kukonza chiwembu choti titheretu ndi kukhala wopanda malo mu Israeli, 6mutipatse adzukulu ake aamuna asanu ndi awiri kuti tiwaphe ndi kuwapereka pamaso pa Yehova ku Gibeya wa Sauli, wosankhidwa wa Yehova.”

Choncho mfumu inati, “Ine ndidzakupatsani.”

7Koma mfumu inasunga Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli, chifukwa cha kulumbira kumene mfumu Davide ndi Yonatani mwana wa Sauli anachita pamaso pa Yehova. 8Ndipo mfumu inatenga Arimoni ndi Mefiboseti, ana aamuna awiri a Rizipa, mwana wamkazi wa Ayiwa, amene anaberekera Sauli pamodzi ndi ana asanu a Merabi mwana wamkazi wa Sauli, amene anabereka Adirieli mwana wa Barizilai Mmeholati. 9Iye anawapereka kwa anthu a ku Gibiyoni, amene anawapha nawayika pa phiri la Yehova. Onse asanu ndi awiri anafera limodzi. Iwo anaphedwa masiku oyamba kukolola barele.

10Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa anatenga chiguduli ndi kudziyalira pa mwala (pamene panali mitemboyo). Kuyambira nthawi yoyamba kukolola mpaka pamene mvula inayambanso kugwa, iye sanalole kuti mbalame zikhudze mitemboyo masana kapena nyama zakuthengo usiku. 11Davide atawuzidwa zimene Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa, mzikazi wa Sauli anachita, 12anapita kukatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi (iwo anawatenga mwamseri kuchoka pabwalo la ku Beti-Sani, kumene Afilisti anawapachika atapha Sauli ku Gilibowa). 13Davide anakatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kumeneko ndiponso mafupa otayidwa a amene anaphedwa nawasonkhanitsa pamodzi.

14Iwo anayika mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani mʼmanda a Kisi abambo ake a Sauli ku Zera mʼdziko la Benjamini, ndipo anachita zonse zimene mfumu inalamula. Atachita zimenezi, Mulungu anayankha pemphero lopempherera dzikolo.

Nkhondo ndi Afilisti

15Nthawi inanso panali nkhondo pakati pa Afilisti ndi Aisraeli, Davide anapita ndi ankhondo ake kukamenyana ndi Afilisti ndipo iye anatopa kwambiri. 16Ndipo Isibi-Benobi, mmodzi mwa zidzukulu za Rafa, amene mkondo wake unkalemera makilogalamu atatu ndi theka ndipo analinso ndi lupanga latsopano, anati adzapha Davide. 17Koma Abisai mwana wa Zeruya anabwera kudzapulumutsa Davide. Iye anamukantha Mfilisitiyo ndi kumupha. Pamenepo asilikali a Davide analumbira kwa iye kuti, “Inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuti nyale ya Israeli isadzazimitsidwe.”

18Patapita nthawi, panali nkhondo ina ndi Afilisti ku Gobu. Pa nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Safu, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai.

19Pa nkhondo inanso ndi Afilisti ku Gobu, Elihanani mwana wa Yaare-Oregimu wa ku Betelehemu anapha Goliati Mgiti, amene anali ndi mkondo ngati ndodo yowombera nsalu.

20Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati panali munthu wina wamtali kwambiri wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa. 21Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.

22Anthu anayi amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo onse anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

撒母耳記下 21:1-22

基遍人向掃羅家復仇

1大衛執政期間,連續有三年饑荒,大衛就求問耶和華。耶和華說:「發生這饑荒是因為掃羅一家人的血債,他們殺害了基遍人。」 2原來基遍人不是以色列人,他們是亞摩利人的遺民。以色列人曾起誓不傷害他們,但掃羅以色列人和猶大人發熱心,試圖剷除基遍人。大衛就召來基遍人, 3問他們:「我可以為你們做些什麼來贖罪,使你們願意祝福耶和華的子民21·3 子民」希伯來文是「產業」。呢?」 4基遍人答道:「金銀不能解決我們和掃羅一家人的問題,我們也不想處死任何以色列人。」大衛說:「你們要我怎麼辦?」 5他們說:「掃羅曾試圖滅絕我們,把我們從以色列境內剷除。 6請你把掃羅的七個子孫交給我們。耶和華選立了掃羅,我們就在耶和華面前把他們吊死在掃羅的家鄉基比亞城。」王說:「我必把他們交給你們。」

7大衛王因為與掃羅的兒子約拿單在耶和華面前起過誓,就沒有把掃羅的孫子、約拿單的兒子米非波設交出來。 8他把埃亞的女兒利斯巴掃羅所生的兩個兒子亞摩尼米非波設掃羅女兒米拉米何拉巴西萊的兒子亞得列所生的五個兒子交給基遍人。 9基遍人在耶和華面前把他們七人吊死在山上,那時正好是收割大麥的時候。

10掃羅的嬪妃、埃亞的女兒利斯巴在一塊磐石上用麻布搭了一座棚看屍。她白天不讓飛鳥靠近,夜間不容野獸走近,從開始收割大麥,一直守到降下雨來。 11大衛知道這件事以後, 12就去基列·雅比人那裡把掃羅約拿單的骸骨運來。從前非利士人在基利波殺死掃羅約拿單,把他們的屍體掛在伯珊的廣場,後來基列·雅比人把屍體偷走了。 13大衛運回掃羅約拿單的骸骨,又收殮了掃羅那七個子孫的骸骨。 14眾人按照大衛的吩咐,把掃羅約拿單的骸骨埋葬在掃羅父親基士的墓裡,在便雅憫境內的洗拉。此後,上帝垂聽了人們為國家的禱告。

與非利士人交戰

15以色列人又和非利士人交戰,大衛親自出征。在他十分疲倦的時候, 16一個名叫以實·比諾的巨人佩戴新刀,手拿三公斤半重的銅矛,衝上來要殺他。 17洗魯雅的兒子亞比篩趕來救駕,殺死了非利士巨人。這事以後,大衛的部下向他起誓說:「你絕不可再跟我們一起出戰,免得以色列的燈熄滅。」 18後來,以色列人和非利士人在歌伯打仗,戶沙西比該殺了另一個非利士巨人撒弗19在同一個地方,伯利恆雅雷俄珥金的兒子伊勒哈難又殺了迦特歌利亞歌利亞的長矛粗如織布機的軸。 20迦特的一次交戰中,有一個非利士巨人每隻手腳各有六個手指和腳趾,共二十四個手指和腳趾。 21他向以色列人罵陣,大衛的哥哥示米亞的兒子約拿單就殺了他。 22這四個迦特巨人的後裔都死在大衛和他的部下手裡。