2 Samueli 20 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 20:1-26

Seba Awukira Davide

1Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti,

“Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide,

tilibe gawo mwa mwana wa Yese!

Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”

2Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.

3Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.

4Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.” 5Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.

6Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.” 7Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.

8Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.

9Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona. 10Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.

11Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!” 12Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu. 13Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.

14Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye. 15Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse, 16mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.” 17Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?”

Iye anayankha kuti, “Ndine.”

Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.”

Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”

18Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo. 19Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”

20Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga. 21Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.”

Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”

22Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.

23Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti. 24Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika, 25Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe 26ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.

Thai New Contemporary Bible

2ซามูเอล 20:1-26

เชบากบฏ

1มีผู้ก่อความไม่สงบคนหนึ่งชื่อเชบาบุตรบิครีชาวเบนยามินเผอิญอยู่ที่นั่น เขาเป่าแตรเขาสัตว์และร้องตะโกนว่า

“เราไม่มีส่วนอะไรกับดาวิด

เราไม่เกี่ยวข้องอะไรกับบุตรเจสซี!

พี่น้องอิสราเอลทั้งหลายเอ๋ย จงกลับบ้านกันเถิด!”

2คนอิสราเอลทั้งปวงจึงทิ้งดาวิดไปติดตามเชบาบุตรบิครี แต่คนยูดาห์อยู่เคียงข้างกษัตริย์ของตน ตามเสด็จตลอดทางจากแม่น้ำจอร์แดนสู่กรุงเยรูซาเล็ม

3เมื่อดาวิดเสด็จมาถึงวังในเยรูซาเล็ม พระองค์ทรงกักตัวสนมทั้งสิบซึ่งทรงทิ้งไว้ให้คอยรักษาวังนั้นไว้ที่ตำหนักแห่งหนึ่ง และให้ได้รับการเลี้ยงดูตามความต้องการ แต่กษัตริย์ไม่ได้รับเป็นสนมอีกต่อไป นางสนมเหล่านั้นจึงถูกกักอยู่ในฐานะแม่ม่ายจนวันตาย

4จากนั้นกษัตริย์ตรัสสั่งอามาสาว่า “จงระดมพลยูดาห์มาที่นี่ภายในสามวัน แล้วตัวเจ้าก็จงมาด้วย” 5แต่เมื่ออามาสาออกไประดมพลยูดาห์ เขาใช้เวลาเกินกว่าที่กษัตริย์กำหนดไว้

6ดาวิดตรัสกับอาบีชัยว่า “เชบาบุตรบิครีจะเป็นภัยต่อเรายิ่งกว่าอับซาโลมเสียอีก จงนำคนของเราตามล่าเอาตัวเขามา ก่อนที่เขาจะหนีเข้าเมืองป้อมปราการพ้นมือเราไปได้” 7คนของโยอาบ คนเคเรธี และคนเปเลท กับนักรบแกล้วกล้าทั้งหลายจึงยกออกไปจากกรุงเยรูซาเล็มภายใต้การนำของอาบีชัยเพื่อตามล่าเชบาบุตรบิครี

8ขณะที่พวกเขามาถึงศิลาใหญ่แห่งกิเบโอน อามาสามาพบกับพวกเขาที่นั่น โยอาบแต่งชุดออกศึก คาดดาบสั้นพร้อมฝักไว้ที่เอว เขาก้าวเข้าไปทักทายอามาสาและแอบชักดาบสั้นออกจากฝัก

9โยอาบพูดว่า “เป็นอย่างไรบ้างน้องชาย?” แล้วใช้มือขวาจับหนวดของอามาสาทำท่าเหมือนจะจูบ 10อามาสาไม่ทันสังเกตดาบสั้นในมือโยอาบ โยอาบจึงแทงเข้าที่ท้องจนไส้ทะลักออกมาที่พื้น โดยไม่ต้องแทงซ้ำ อามาสาตายคาที่ แล้วโยอาบกับอาบีชัยน้องชายก็ตามล่าเชบาบุตรบิครีต่อไป

11ทหารคนหนึ่งของโยอาบยืนข้างร่างของอามาสาและกล่าวว่า “ผู้ใดชื่นชอบโยอาบและผู้ใดเป็นฝ่ายดาวิด จงตามโยอาบมา” 12ส่วนอามาสานอนจมกองเลือดอยู่กลางถนน และเมื่อทหารคนนั้นเห็นทหารทั้งหมดหยุดดูศพของอามาสา เขาจึงลากศพจากถนนไปทิ้งไว้กลางทุ่งและโยนเสื้อผ้าคลุมไว้ 13เมื่อกำจัดร่างของอามาสาออกไปให้พ้นทางแล้ว ทุกคนต่างก็สมทบกับโยอาบ ออกตามล่าเชบาบุตรบิครี

14ฝ่ายเชบาเดินทางไปทั่วทุกเผ่าของอิสราเอลไปยังอาเบลเบธมาอาคาห์20:14 หรืออาเบลจนถึงเบธมาอาคาห์เช่นเดียวกับข้อ 15 และทั่วภูมิภาคของชาวเบไรต์ซึ่งรวมตัวกันมาติดตามเขา 15กองกำลังของโยอาบมาโอบล้อมเชบาในอาเบลเบธมาอาคาห์ ก่อเชิงเทินใหญ่ต่อกับกำแพงเมือง แล้วเริ่มทลายกำแพง 16หญิงเจ้าปัญญาคนหนึ่งร้องบอกจากตัวเมืองว่า “โปรดฟังหน่อยเถิด เรียกท่านโยอาบมาทางนี้ ดิฉันขอพูดด้วย” 17เมื่อโยอาบมาถึง หญิงนั้นถามว่า “ท่านคือโยอาบหรือ?”

เขาตอบว่า “ใช่”

นางกล่าวว่า “โปรดฟังสิ่งที่ผู้รับใช้ของท่านจะพูด”

โยอาบตอบว่า “เราฟังอยู่”

18นางกล่าวต่อไปว่า “เคยมีคำกล่าวไว้ว่า ‘ไปเอาคำตอบกับอาเบล’ แล้วเรื่องก็เรียบร้อย 19เราเป็นพวกที่รักสันติและจงรักภักดีในอิสราเอล ท่านกำลังพยายามทำลายเมืองแม่ของอิสราเอล เหตุใดท่านจึงต้องการที่จะกลืนกินมรดกขององค์พระผู้เป็นเจ้า?”

20โยอาบตอบว่า “ขอให้เรื่องนี้ห่างไกลจากเรา! เราไม่เคยคิดที่จะกลืนกินหรือทำลายเมืองนี้เลย! 21เราต้องการแต่เพียงได้ตัวคนที่ชื่อเชบาบุตรบิครีจากแดนเทือกเขาแห่งเอฟราอิมซึ่งกบฏต่อกษัตริย์ดาวิด หากเจ้าเอาตัวชายคนนี้มาให้ เราก็จะถอนกำลังไปจากเมืองนี้”

หญิงนั้นตอบว่า “เราจะโยนหัวเขาข้ามกำแพงลงมาให้ท่าน”

22หญิงนั้นจึงไปหาพวกชาวเมือง และให้คำปรึกษาอย่างฉลาดหลักแหลม พวกเขาก็ตัดศีรษะเชบาบุตรบิครีโยนลงมาให้โยอาบ โยอาบจึงเป่าแตรเขาสัตว์เรียกกองทหารให้แยกย้ายจากเมืองนั้นกลับบ้าน ส่วนโยอาบกลับมาเข้าเฝ้ากษัตริย์ที่กรุงเยรูซาเล็ม

23โยอาบเป็นผู้บัญชาการกองทัพทั้งหมดของอิสราเอล เบไนยาห์บุตรเยโฮยาดาเป็นผู้บัญชาการ คนเคเรธีและคนเปเลท 24อาโดนีรัม20:24 ภาษาฮีบรูว่าอาโดรัม(ดู1พกษ.4:6 และ 5:14)เป็นผู้ดูแลคนงานโยธา เยโฮชาฟัทบุตรอาหิลูดเป็นอาลักษณ์หลวง 25เชวาเป็นราชเลขา ศาโดกกับอาบียาธาร์เป็นปุโรหิต 26และอิราแห่งยาอีร์เป็นปุโรหิตของดาวิด