2 Samueli 1 – CCL & TCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 1:1-27

Davide Amva za Imfa ya Sauli

1Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri. 2Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.

3Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”

4Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?”

Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”

5Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”

6Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira. 7Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’ ”

8Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”

9“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’

10“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”

11Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo. 12Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.

13Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”

14Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”

15Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa. 16Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’ ”

Davide Alira Maliro a Sauli ndi Yonatani

17Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani. 18Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:

19“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda.

Taonani amphamvu agwa kumeneko!

20“Musakanene zimenezi ku Gati,

musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni,

kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale,

ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.

21“Inu mapiri a ku Gilibowa,

musakhalenso ndi mame kapena mvula,

kapena minda yobereka zopereka za ufa.

Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa,

chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.

22“Pa magazi a ophedwa,

pa mnofu wa amphamvu,

uta wa Yonatani sunabwerere,

lupanga la Sauli silinabwere chabe.

23“Sauli ndi Yonatani,

pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima,

ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe.

Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga,

anali ndi mphamvu zoposa mkango.

24“Inu ana aakazi a Israeli,

mulireni Sauli,

amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa,

amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.

25“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo!

Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.

26Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani,

unali wokondedwa kwambiri kwa ine.

Chikondi chako pa ine chinali chopambana,

chopambana kuposa chikondi cha akazi.

27“Taonani amphamvu agwa!

Zida zankhondo zawonongeka!”

Tagalog Contemporary Bible

2 Samuel 1:1-27

Nalaman ni David ang Pagkamatay ni Saul

1Bumalik sina David sa Ziklag pagkatapos nilang matalo ang mga Amalekita. Patay na noon si Saul. Nanatili sila ng dalawang araw sa Ziklag. 2Nang ikatlong araw, may dumating na tao sa Ziklag mula sa kampo ni Saul; punit ang damit niya at may alikabok ang ulo bilang pagluluksa. Lumapit siya kay David at yumukod bilang paggalang sa kanya. 3Tinanong siya ni David, “Saan ka nanggaling?” Sumagot siya, “Nakatakas po ako mula sa kampo ng mga Israelita.” 4Nagtanong si David, “Bakit, ano ang nangyari? Sabihin mo sa akin.” Sinabi niya, “Tumakas po ang mga sundalo ng Israel sa labanan. Maraming napatay sa kanila pati na po si Saul at ang anak niyang si Jonatan.” 5Nagtanong si David sa binata, “Paano mo nalamang patay na sina Saul at Jonatan?” 6Ikinuwento ng binata ang nangyari, “Nagkataon na nandoon po ako sa Bundok ng Gilboa, at nakita ko roon si Saul na nakasandal sa sibat niya. Palapit na po sa kanya ang mga kalaban na nakasakay sa mga karwahe at kabayo. 7Nang lumingon siya, nakita niya ako at tinawag niya ako. Sumagot ako, ‘Ano po ang maitutulong ko?’ 8Tinanong niya kung sino ako. Sumagot ako na isa akong Amalekita. 9Pagkatapos, nakiusap siya sa akin, ‘Lumapit ka rito at patayin mo ako, tapusin mo na ang paghihirap ko. Gusto ko nang mamatay dahil hirap na ako sa kalagayan ko.’ 10Kaya nilapitan ko siya at pinatay dahil alam kong hindi na rin siya mabubuhay sa grabeng sugat na natamo niya. Pagkatapos, kinuha ko po ang korona sa ulo niya at pulseras sa kamay niya, at dinala ko po rito sa inyo.”

11Nang marinig ito ni David at ng mga tauhan niya, pinunit nila ang kanilang mga damit bilang pagluluksa. 12Umiyak at nag-ayuno sila hanggang gabi para kay Saul at sa anak nitong si Jonatan, at para sa mga mamamayan ng Panginoon, ang bayan ng Israel, dahil marami ang namatay sa digmaan. 13Tinanong pa ni David ang binatang nagbalita sa kanya, “Taga-saan ka?” Sumagot siya, “Isa po akong dayuhang Amalekita na nakatira sa lupain ninyo.” 14Nagtanong si David, “Bakit hindi ka man lang natakot na patayin ang piniling hari ng Panginoon?” 15Pagkatapos, tinawag ni David ang isa sa mga tauhan niya at inutusan, “Patayin mo ang taong ito!” Pinatay nga ng tauhan niya ang tao. 16Sinabi ni David, “Ikaw ang dapat sisihin sa kamatayan mo. Ikaw na mismo ang tumestigo laban sa sarili mo nang sabihin mong pinatay mo ang piniling hari ng Panginoon.”

Ang Awit ng Kalungkutan ni David para kina Saul at Jonatan

17Gumawa si David ng isang awit para kay Saul at sa anak nitong si Jonatan, 18at iniutos niyang ituro ito sa mga mamamayan ng Juda. Tinawag itong Awit Tungkol sa Pana at nakasulat ito sa Aklat ni Jashar. Ito ang panaghoy niya:

19“O Israel, ang mga dakilang mandirigma moʼy namatay sa kabundukan mismo ng Israel.

Napatay din ang mga magigiting mong sundalo.

20Huwag itong ipaalam sa Gat, o sa mga lansangan ng Ashkelon,

baka ikagalak ito ng mga babaeng Filisteo na hindi nakakakilala sa Dios.

21O Bundok ng Gilboa, wala sanang ulan o hamog na dumating sa iyo.

Wala sanang tumubong pananim sa iyong bukirin upang ihandog sa Dios.1:21 upang ihandog sa Dios: o, sa sambahan sa matataas na lugar.

Sapagkat diyan nadungisan ng mga kaaway ang pananggalang ng magiting na si Haring Saul.

At wala nang magpapahid dito ng langis upang itoʼy linisin at pakintabin.

22Sa pamamagitan ng espada ni Saul at pana ni Jonatan, maraming magigiting na kalaban ang kanilang napatay.

23Minahal at kinagiliwan ng mga Israelita sina Saul at Jonatan.

Magkasama sila sa buhay at kamatayan.

Sa digmaan, mas mabilis pa sila sa agila at mas malakas pa sa leon.

24Mga babae ng Israel, magdalamhati kayo para kay Saul.

Dahil sa kanyaʼy nakapagsuot kayo ng mga mamahaling damit at alahas na ginto.

25Ang magigiting na sundalo ng Israel ay napatay sa labanan.

Pinatay din si Jonatan sa inyong kabundukan.

26Nagdadalamhati ako sa iyo, Jonatan kapatid ko!

Mahal na mahal kita; ang pagmamahal mo sa akin ay mas higit pa sa pagmamahal ng mga babae.

27Nangabuwal ang magigiting na sundalo ng Israel.

Ang kanilang mga sandataʼy nangawala.”