2 Petro 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Petro 3:1-18

Kubwera kwa Ambuye

1Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera. 2Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.

3Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa. 4Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.” 5Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi. 6Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa. 7Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.

8Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi! 9Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.

10Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.

11Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu 12pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha. 13Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.

14Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye. 15Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa. 16Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.

17Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa. 18Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

彼得後書 3:1-18

主再來的應許

1親愛的弟兄姊妹,我現在寫給你們的是第二封信。這兩封信都是為了提醒你們,激勵你們保持真誠的心, 2叫你們記得從前聖先知們說的預言,以及我們的主和救主藉著派到你們那裡的使徒所傳給你們的誡命。

3最重要的是,你們要知道在末世的時候必出現喜歡冷嘲熱諷、為所欲為的人。他們說: 4「主要降臨的應許在哪裡?從我們的祖先長眠地下直到現在,萬物依舊與創世之初一樣。」 5他們故意忽略:太初,上帝憑口中的話語創造了諸天,並藉著水從水中造出了地; 6後來,那個世界被水淹沒而毀滅了。 7同樣,現在的天地要憑上帝的話語存留到不敬虔的人被審判和毀滅的日子,那時天地要被火焚燒。

8親愛的弟兄姊妹,有一件事你們不可忽略,就是主看一日如千年,千年如一日。 9主的應許還未實現,有人以為祂拖延,其實祂不是拖延,而是在寬容你們。祂不願任何人滅亡,願意人人悔改。 10不過,主再來的日子要像賊一樣突然臨到。那日,諸天必在一聲巨響中消失,有形有質的都要被烈火焚毀,大地和其中的一切將不復存在。

11-12一切都要這樣被焚毀,你們在熱切等候上帝來臨的日子期間,該怎樣過聖潔、敬虔的生活啊!因為到那日,天要被火焚毀,有形有質的都要被烈火熔化燒盡。 13但我們等候的是上帝應許的新天新地,有公義住在其中。

14所以,親愛的弟兄姊妹,你們既然盼望這些事,就當努力使自己在主面前毫無瑕疵,無可指責,安然無懼。 15你們要把耶穌的寬容看作是讓眾人得救的機會,正如我們親愛的弟兄保羅按著上帝賜給他的智慧寫信告訴你們的。 16他所有的書信都談到這些事。一些不學無術、反覆無常的人曲解了信中一些難懂的地方,就像曲解其他經文一樣,他們是自取滅亡。

17因此,親愛的弟兄姊妹,你們既然預先知道了這些事,就應該提防,不要讓那些不法之徒用錯謬的理論引誘你們,使你們失去原本堅固的立場。 18相反,你們要在我們的主和救主耶穌基督的恩典中不斷長進,越來越認識祂。

願榮耀歸給祂,從現在直到永遠。阿們!