2 Petro 1 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Petro 1:1-21

1Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu.

Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.

2Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.

Kudziwa za Mayitanidwe ndi za Kusankhidwa Kwathu

3Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake. 4Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.

5Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru. 6Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu. 7Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi. 8Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu. 9Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.

10Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse. 11Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.

Kukhala Oyera Mtima

12Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano. 13Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani, 14chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu. 15Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.

16Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake. 17Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.” 18Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.

19Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu. 20Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha. 21Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.

Thai New Contemporary Bible

2เปโตร 1:1-21

1จดหมายฉบับนี้จากข้าพเจ้าซีโมนเปโตรผู้เป็นผู้รับใช้และอัครทูตของพระเยซูคริสต์

ถึงบรรดาผู้ได้รับความเชื่ออันล้ำค่าเช่นเดียวกับที่เราได้รับโดยทางความชอบธรรมของพระเยซูคริสต์ผู้ทรงเป็นพระเจ้าและพระผู้ช่วยให้รอดของเรา

2ขอพระคุณและสันติสุขมีแด่พวกท่านอย่างล้นเหลือผ่านทางการรู้จักพระเจ้าและรู้จักพระเยซูองค์พระผู้เป็นเจ้าของเรา

มั่นใจในการทรงเรียกและทรงเลือก

3ฤทธิ์อำนาจของพระองค์ได้ประทานทุกสิ่งที่จำเป็นแก่เราที่จะดำเนินชีวิตในทางพระเจ้า ผ่านทางการรู้จักพระองค์ผู้ทรงเรียกเราด้วยพระเกียรติสิริและคุณความดีของพระองค์เอง 4โดยสิ่งเหล่านี้พระองค์ได้ประทานพระสัญญาอันยิ่งใหญ่และล้ำค่าของพระองค์แก่เรา เพื่อว่าโดยทางพระสัญญาเหล่านี้พวกท่านจะได้มีส่วนในพระลักษณะของพระเจ้าและพ้นจากความเสื่อมทรามในโลกซึ่งเกิดจากตัณหาชั่ว

5ด้วยเหตุนี้ท่านจงพยายามทุกวิถีทางที่จะเพิ่มความดีเข้ากับความเชื่อ เพิ่มความรู้เข้ากับความดี 6เพิ่มการบังคับตนเข้ากับความรู้ เพิ่มความอดทนบากบั่นเข้ากับการบังคับตน เพิ่มการดำเนินในทางพระเจ้าเข้ากับความอดทนบากบั่น 7เพิ่มความรักฉันพี่น้องเข้ากับการดำเนินในทางพระเจ้า และเพิ่มความรักเข้ากับความรักฉันพี่น้อง 8เพราะถ้าท่านมีคุณสมบัติเหล่านี้มากยิ่งๆ ขึ้นก็จะทำให้ท่านมีประสิทธิภาพและเกิดผลในการรู้จักองค์พระเยซูคริสต์เจ้าของเรา 9แต่ถ้าผู้ใดขาดคุณสมบัติเหล่านี้ก็ตาบอดตาสั้น และลืมว่าตนได้รับการทรงชำระจากบาปในอดีตแล้ว

10เพราะฉะนั้นพี่น้องทั้งหลายของข้าพเจ้า จงขวนขวายให้มากยิ่งขึ้นที่จะประพฤติตนในทางซึ่งแสดงว่าพระเจ้าทรงเรียกและทรงเลือกท่านอย่างแน่นอน เพราะถ้าท่านทำสิ่งเหล่านี้ท่านจะไม่มีวันล้มลง 11และท่านจะได้รับการต้อนรับอย่างอบอุ่นสู่อาณาจักรนิรันดร์ของพระเยซูคริสต์องค์พระผู้เป็นเจ้าและพระผู้ช่วยให้รอดของเรา

คำพยากรณ์ของพระคัมภีร์

12ดังนั้นข้าพเจ้าจะเตือนท่านให้ระลึกถึงสิ่งเหล่านี้เสมอแม้ว่าท่านทราบเรื่องนี้แล้วและตั้งมั่นในความจริงที่มีอยู่ก็ตาม 13ข้าพเจ้าคิดว่าถูกต้องแล้วที่จะเตือนความจำของท่านตราบเท่าที่ข้าพเจ้ายังอยู่ในเรือนกายนี้ 14เพราะข้าพเจ้ารู้ว่าอีกไม่นานจะต้องจากเรือนกายนี้ไปตามที่องค์พระเยซูคริสต์เจ้าของเราได้ทรงสำแดงไว้แก่ข้าพเจ้าอย่างชัดเจน 15และข้าพเจ้าจะพยายามทำทุกวิถีทางให้พวกท่านสามารถระลึกถึงสิ่งเหล่านี้เสมอหลังจากข้าพเจ้าจากไปแล้ว

16เมื่อเราบอกพวกท่านถึงฤทธิ์อำนาจและการจะเสด็จมาขององค์พระเยซูคริสต์เจ้าของเรา พวกเราไม่ได้กุเรื่องขึ้นมาอย่างแยบยล แต่เราเป็นพยานผู้ได้เห็นพระบารมีอันยิ่งใหญ่ของพระองค์ 17เพราะพระเยซูทรงได้รับพระเกียรติและพระสิริจากพระเจ้าพระบิดา เมื่อมีพระสุรเสียงจากองค์ผู้ทรงเกียรติสิริยิ่งใหญ่ตรัสกับพระองค์ว่า “คนนี้คือลูกที่รักของเรา เราพอใจเขามาก”1:17 มธ.17:5; มก.9:7; ลก.9:35 18พวกเราเองได้ยินพระสุรเสียงนี้จากสวรรค์ขณะอยู่กับพระองค์ที่ภูเขาศักดิ์สิทธิ์

19ดังนั้นพวกเราจึงมั่นใจในถ้อยคำของผู้เผยพระวจนะมากยิ่งขึ้น จะเป็นการดีถ้าพวกท่านเอาใจใส่ถ้อยคำเหล่านี้ซึ่งเป็นเหมือนแสงสว่างส่องในที่มืดจนกว่าจะถึงรุ่งเช้าและดาวแห่งรุ่งอรุณจะปรากฏขึ้นในใจท่าน 20เหนือสิ่งอื่นใดท่านต้องเข้าใจว่าไม่มีคำพยากรณ์ใดในพระคัมภีร์ที่มาจากความเข้าใจของตัวผู้เผยพระวจนะเอง 21เพราะคำของผู้เผยพระวจนะนั้นไม่เคยเกิดจากเจตจำนงของมนุษย์ แต่มนุษย์กล่าวถ้อยคำซึ่งมาจากพระเจ้าตามที่พระวิญญาณบริสุทธิ์ทรงดลใจเขา