2 Mbiri 9 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 9:1-31

Mfumu Yayikazi ya ku Seba Ichezera Solomoni

1Mfumu yayikazi ya ku Seba itamva za kutchuka kwa Solomoni, inabwera mu Yerusalemu kudzamuyesa ndi mafunso okhwima. Inafika ndi gulu lalikulu la ngamira zonyamula zokometsera zakudya, golide wambiri, ndi miyala yokongola. Inafika kwa Solomoni ndipo inayankhula naye zonse zimene zinali mu mtima mwake. 2Solomoni anayankha mafunso ake onse ndipo panalibe kanthu kalikonse kovuta kwa iye komwe sanathe kufotokozera mfumu yayikaziyo. 3Mfumu yayikazi ya ku Seba itaona nzeru za Solomoni komanso nyumba yaufumu imene anamanga, 4chakudya cha pa tebulo pake, moyo wa antchito ake ndi zovala zawo; atumiki opereka zakumwa ndi zovala zawo ndiponso nsembe zopsereza zimene ankapereka ku Nyumba ya Yehova, inathedwa nzeru.

5Iyo inati kwa mfumu, “Mbiri imene ndinamva ndili ku dziko kwathu, ya zomwe munachita komanso nzeru zanu ndi yoona. 6Koma sindinakhulupirire zimene ankanena mpaka nditafika ndi kuona ndi maso anga. Kunena zoona sanandiwuze ngakhale theka lomwe la kuchuluka kwa nzeru zanu, pakuti zaposa zimene ndinamva. 7Ngodala anthu anu! Ngodala atumiki anu amene amayimirira pamaso panu nthawi zonse ndi kumamva nzeru zanu! 8Atamandike Yehova Mulungu wanu amene wakondwera nanu nakukhazikani pa mpando wake waufumu kuti mulamulire mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu. Chifukwa cha chikondi cha Mulungu wanu pa Israeli, ndi khumbo lake kuti akusungeni mpaka muyaya, Iye wayika inu kukhala mfumu yawo kuti mulamulire moyenera ndi mwachilungamo.”

9Kenaka iyo inapereka kwa mfumu makilogalamu 4,000 a golide, zonunkhira zambirimbiri ndi miyala yokongola. Nʼkale lomwe sikunaonekenso zonunkhiritsa ngati zomwe mfumu yayikazi ya ku Seba inapereka kwa mfumu Solomoni.

10(Anthu a Hiramu ndi anthu a Solomoni anabweretsa golide kuchokera ku Ofiri ndipo anabweretsanso mitengo ya mʼbawa ndi miyala yokongola. 11Mfumu inagwiritsa ntchito mitengo ya mʼbawa pokonzera makwerero a Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndiponso kupangira anthu oyimba apangwe ndi azeze. Zinthu zonga zimenezi sizinaonekeponso mu Yuda).

12Mfumu Solomoni inapereka kwa mfumu yayikazi ya ku Seba zonse zimene inazifuna ndi kuzipempha ndipo Solomoni anayipatsa mfumuyo zoposa zimene iyo inabweretsa kwa Solomoni. Ndipo mfumuyo inabwerera ku dziko lake pamodzi ndi atumiki ake.

Ulemerero wa Mfumu Solomoni

13Kulemera kwa golide amene Solomoni amalandira pa chaka kunali makilogalamu 23,000, 14osawerengera amene ankabwera ndi anthu ochita malonda ndi osinthanitsa zinthu. Komanso mafumu onse a ku Arabiya ndi abwanamkubwa a mʼdzikomo amabweretsa golide ndi siliva kwa Solomoni.

15Mfumu Solomoni inapanga zishango zazikulu 200 zagolide wosasantha. Mʼchishango chilichonse mumalowa golide wolemera makilogalamu asanu ndi awiri. 16Iye anapanganso zishango zingʼonozingʼono 300 zagolide wosasantha ndipo chishango chilichonse chimapangidwa ndi golide wolemera makilogalamu atatu. Mfumu inayika zishangozi mʼnyumba yaufumu yotchedwa Nkhalango ya Lebanoni.

17Ndipo mfumu inapanganso mpando waukulu waufumu wa nyanga za njovu ndipo unakutidwa ndi golide woyengeka bwino. 18Mpando waufumuwo unali ndi makwerero asanu ndi limodzi ndi choyikapo mapazi cholumikizidwa ku mpandowo. Mʼmbali zonse za mpandowo munali zosanjikapo manja, ndi chifanizo cha mkango chitayima posanjikapo manjapo. 19Mikango khumi ndi iwiri inayimirira pa makwerero asanu ndi imodzi aja. Umodzi mbali ina ya khwerero ndi wina mbali inayo. Palibe mpando wonga uwu umene unapangidwapo mu ufumu wina uliwonse. 20Zikho zonse za mfumu Solomoni zinali zagolide, ndiponso zipangizo zonse za ku nyumba yaufumu ya Nkhalango ya Lebanoni zinali zagolide oyengeka bwino. Panalibe chinthu chopangidwa ndi siliva, chifukwa siliva samayesedwa kanthu mʼnthawi ya Solomoni. 21Mfumu inali ndi sitima zambiri zapamadzi zimene zimayendetsedwa ndi antchito a Hiramu. Zimabwera kamodzi pa zaka zitatu zilizonse zitanyamula golide, siliva ndi nyanga za njovu, ndiponso anyani ndi apusi.

22Mfumu Solomoni anapambana mafumu ena onse a dziko lapansi pa chuma ndi nzeru. 23Mafumu onse a dziko lapansi ankafunafuna kuonana ndi Solomoni kuti adzamve nzeru zimene Mulungu anayika mu mtima mwake. 24Chaka ndi chaka, aliyense amene amabwera, amabweretsa mphatso monga zipangizo zasiliva ndi golide, mikanjo, zida zankhondo ndi zokometsera zakudya komanso akavalo ndi abulu.

25Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo ndi magaleta, ndi akavalo 12,000 amene amawasunga mʼmizinda yosungira magaleta ndiponso ena anali ndi iye ku Yerusalemu. 26Iye ankalamulira mafumu onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika ku malire a dziko la Igupto. 27Mfumu inasandutsa siliva kukhala wambiri ngati miyala wamba mu Yerusalemu ndipo mikungudza kukhala yochuluka ngati mitengo ya mkuyu ya ku zigwa. 28Solomoni ankayitanitsa akavalo ake kuchokera ku Igupto ndi mayiko ena onse.

Kumwalira kwa Solomoni

29Tsono ntchito zina zonse za Solomoni, kuyambira pachiyambi mpaka kumaliza, kodi sizinalembedwa mʼbuku la mbiri la mneneri Natani, ndi mʼbuku la uneneri wa Ahiya wa ku Silo ndi mʼbuku la masomphenya a mlosi Ido, lokamba za Yeroboamu mwana wa Nebati? 30Solomoni analamulira Aisraeli onse ku Yerusalemu zaka makumi anayi. 31Ndipo anamwalira nagona ndi makolo ake. Anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.

New Russian Translation

2 Паралипоменон 9:1-31

Царица Шевы посещает Соломона

(3 Цар. 10:1-13)

1Когда царица Шевы услышала о славе Соломона, она пришла в Иерусалим, чтобы испытать его трудными вопросами. Прибыв с очень большой свитой, с верблюдами, везущими пряности и великое множество золота и драгоценных камней, она пришла к Соломону и говорила с ним обо всем, что было у нее на сердце. 2Соломон ответил на все ее вопросы: для него не было ничего слишком трудного, чего он не смог бы ей объяснить. 3Когда царица Шевы увидела мудрость Соломона и дворец, который он построил, 4еду у него на столе, жилища его приближенных, как прислуживают его слуги, как они одеты, каковы его виночерпии, как одеты они, и какие всесожжения он совершает в доме9:4 Так в некоторых древних переводах (ср. 3 Цар. 10:5); в еврейском тексте: «его подъем, которым он поднимается в храм». Господа, у нее захватило дух. 5Она сказала царю:

– Молва, которую я слышала в своей стране о твоих делах и мудрости, правдива, 6но я не верила слухам, пока не пришла и не увидела это своими глазами. И что же, мне не рассказали и о половине твоей мудрости! Ты далеко превзошел ту молву, что я слышала. 7Блаженны твои люди! Блаженны твои приближенные, которые всегда стоят перед тобой и внимают твоей мудрости! 8Да будет благословен Господь, твой Бог, Который благоволит к тебе и посадил тебя царем на Своем престоле, чтобы ты правил для Господа, твоего Бога. Ради любви твоего Бога к Израилю, ради желания утвердить их навеки, Он сделал тебя его царем, чтобы ты поступал справедливо и праведно.

9Она подарила царю сто двадцать талантов9:9 Около 4 т. золота, великое множество пряностей и драгоценных камней. Никогда больше не было пряностей, подобных тем, что царица Шевы подарила царю Соломону.

10Хирамовы люди и люди Соломона привозили золото из Офира. Еще они привезли красное дерево и драгоценные камни. 11Царь сделал из красного дерева лестницы9:11 Так в некоторых древних переводах; смысл этого места в еврейском тексте неясен. для Господнего дома и для царского дворца, а также арфы и лиры для музыкантов. Прежде в Иудее не видели ничего подобного.

12Царь Соломон подарил царице Шевы все, что она пожелала и о чем просила. Он подарил ей больше, чем она привезла ему. После этого она ушла и вернулась со свитой в свою страну.

Богатство и великолепие Соломона

(3 Цар. 10:14-29; 2 Пар. 1:14-17)

13Золота, которое Соломон получал ежегодно, было по весу шестьсот шестьдесят шесть талантов9:13 Около 23 т., 14не считая того дохода, что поступал от купцов и торговцев, и от всех царей Аравии и наместников страны тоже привозили Соломону золото и серебро.

15Царь Соломон сделал двести больших щитов из кованого золота, на каждый из которых пошло по шестьсот бек9:15 Около 3,5 кг. золота. 16Еще он сделал триста маленьких щитов из кованого золота, на каждый щит по триста бек9:16 Около 1,7 кг. золота. Царь поместил их во дворце Ливанского леса.

17Еще царь сделал огромный трон, выложенный слоновой костью и покрытый чистым золотом. 18У трона было шесть ступенек, и к нему было прикреплено золотое подножие. По обеим сторонам сиденья были подлокотники, и у каждого из них стояло по льву. 19Двенадцать львов стояло на шести ступеньках – по одному с каждой стороны каждой ступеньки. Никогда ничего подобного не делалось ни в каком другом царстве.

20Все чаши царя Соломона были золотыми, и вся домашняя утварь во дворце Ливанского леса была из чистого золота. Серебряного ничего не было, потому что серебро в дни Соломона не ценилось.

21На море у царя был флот из таршишских кораблей с командой из слуг Хирама. Раз в три года корабли возвращались, привозя золото, серебро, слоновую кость, обезьян и павлинов.

22Царь Соломон превосходил богатством и мудростью всех царей земли. 23Все они искали встречи с Соломоном, чтобы послушать мудрости, которую вложил в его сердце Бог. 24Всякий приходящий приносил дары – изделия из серебра и золота, одежды, оружие и пряности, лошадей и мулов, и так – из года в год.

25У Соломона было четыре тысячи стойл для коней и колесниц и двенадцать тысяч коней9:25 Или: «колесничих»; или: «всадников»., которых он держал в колесничных городах и у себя в Иерусалиме. 26Он правил всеми царями от Реки9:26 То есть Евфрата. до земли филистимлян, до самой границы Египта. 27В его правление серебро в Иерусалиме ценилось не выше простых камней, а кедра было так же много, как тутовых деревьев в предгорьях Иудеи. 28Кони Соломона поставлялись из Египта9:28 Или, возможно: «из Муцура» – области в Киликии. См. сноску на 1:16. и из других стран.

Смерть Соломона

(3 Цар. 11:41-43)

29Что же до прочих событий правления Соломона, от первых до последних, то разве не описаны они в записях пророка Нафана, в пророчестве Ахии из Шило и в видениях провидца Иддо о Иеровоаме, сыне Навата? 30Соломон правил в Иерусалиме всем Израилем сорок лет. 31Потом он упокоился со своими предками и был похоронен в Городе Давида, своего отца. А Ровоам, его сын, стал царем вместо него.