2 Mbiri 7 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 7:1-22

Mwambo Wopereka Nyumba kwa Yehova

1Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo. 2Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova. 3Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti,

“Iye ndi wabwino;

chikondi chake chikhala chikhalire”

4Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova. 5Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu. 6Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.

7Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.

8Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto. 9Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero. 10Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.

Yehova Aonekera Solomoni

11Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu, 12Yehova anamuonekera usiku ndipo anati:

“Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.

13“Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu, 14ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo. 15Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano. 16Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.

17“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga, 18Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’

19“Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, 20pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse. 21Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’ 22Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’ ”

Bibelen på hverdagsdansk

2. Krønikebog 7:1-22

Templet indvies

1.Kong. 8,62-66

1-2Da Salomon var færdig med at bede, faldt der ild ned fra himlen og fortærede offerdyrene på alteret, og Herrens herlighed fyldte templet, så præsterne ikke kunne gå derind. 3Da Israels folk så ilden og Herrens herlighed, knælede de med ansigtet mod jorden og tilbad og takkede Herren med ordene:

„Herren er god.

Hans trofasthed varer til evig tid!”

4Kongen og folket bragte en utrolig mængde ofre til Herren. 5Kong Salomons offer alene bestod af 22.000 stykker hornkvæg og 120.000 stykker småkvæg. På den måde indviede de Guds tempel. 6Under offerhandlingen stod præsterne på deres poster, og levitterne spillede og sang: „Herrens trofasthed varer til evig tid”. De spillede på de instrumenter, som kong David havde ladet fremstille til brug ved lovprisning af Herren. Over for levitterne stod præsterne og blæste i deres trompeter, mens hele folket stod op.

7Salomon indviede den midterste del af forgården, så der også kunne brændes ofre der. Bronzealteret, som han have fået lavet, var slet ikke stort nok til at klare alle brændofrene, afgrødeofrene og fedtet fra takofrene, som skulle brændes.

8Salomon og hele Israels folk fejrede indvielsen af templet i syv dage. En vældig menneskemængde fra hele Israel tog del i festen. De var kommet helt fra landets yderste grænser, Lebo-Hamat i nord og Egyptens Bæk i syd. 9Efter indvielsesfesten fejrede de Løvhyttefesten i endnu syv dage, og dagen efter afsluttedes det hele med en særlig højtidelighed. 10Den 23. dag i den syvende måned brød folket op og vendte hjem, glade og lykkelige over al den godhed, Herren havde vist David, Salomon og sit folk, Israel.

Guds advarsel til Salomon

1.Kong. 9,1-9

11Salomon var nu færdig med at bygge Herrens hus og sit eget palads. Det var lykkedes ham at fuldføre alle sine planer for templet og paladset. 12Da viste Herren sig for ham om natten og sagde: „Jeg har hørt din bøn og udvalgt dette tempel som et sted, hvor I kan bringe ofre til mig. 13Hvis jeg fremover lukker himlens sluser, så regnen udebliver, eller hvis jeg befaler græshopper at ødelægge jeres afgrøder, eller jeg sender sygdomsepidemier iblandt jer, 14og hvis mit folk da ydmyger sig i bøn, søger mig og vender sig fra deres onde handlinger, da vil jeg høre deres bøn i Himlen, tilgive deres synder og genoprette deres land. 15Jeg vil lytte til hver en bøn, som bedes på dette sted, 16for jeg har udvalgt og indviet dette hus som min bolig for evigt. Mine øjne hviler på dette sted, og jeg vil altid have det i tanke.

17Og hvad dig angår, hvis du vil adlyde mig, som din far gjorde, hvis du vil gøre alt, hvad jeg beder dig om, og overholde mine love og påbud, 18så vil jeg lade din slægt beholde tronen til evig tid, sådan som jeg lovede din far, da jeg sagde: ‚Der vil i al fremtid være en af dine efterkommere på Israels trone!’

19Men hvis I vender jer bort fra mig, og hvis I ikke adlyder de befalinger, jeg har givet jer, men begynder at tilbede andre guder, 20så vil jeg jage mit folk ud af det land, jeg har givet dem, og jeg vil vende ryggen til mit hus her, som jeg ellers nu har gjort helligt. Da vil jeg gøre mit folk til genstand for hån og latterliggørelse blandt alle folkeslag. 21Mit hus skal lægges i ruiner, og enhver, der går forbi, vil blive slået af forundring og spørge: ‚Hvorfor har Herren været så hård mod dette land og dette hus?’ 22Og svaret skal lyde: ‚Fordi de svigtede Herren, deres Gud, som førte deres forfædre ud af Egypten. De vendte sig til andre guder, som de tilbad og tjente i stedet. Denne ulykke er Herrens straf over dem.’ ”