2 Mbiri 5 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 5:1-14

1Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.

Bokosi la Chipangano Libweretsedwa mʼNyumba ya Mulungu

2Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide. 3Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.

4Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano, 5ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula, 6ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.

7Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi. 8Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira. 9Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino. 10Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.

11Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera. 12Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi. 13Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti,

“Yehova ndi wabwino;

chikondi chake chikhala mpaka muyaya.”

Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo, 14choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

歷代志下 5:1-14

1這樣,所羅門完成了耶和華殿的一切工作。所羅門把他父親大衛獻給上帝的金銀和一切器具都搬進上帝殿的庫房。

運約櫃入聖殿

2所羅門以色列的長老、各支派的首領和族長召集到耶路撒冷,準備把耶和華的約櫃從大衛錫安運上來。 3在七月住棚節的時候,以色列人都聚集到所羅門王那裡。 4以色列的長老到齊後,祭司便抬起約櫃, 5祭司和利未人將約櫃、會幕和會幕裡的一切聖器運上來。 6所羅門王和聚集到他那裡的以色列全體會眾在約櫃前獻祭,獻上的牛羊多得不可勝數。 7祭司把耶和華的約櫃抬進內殿,即至聖所,放在兩個基路伯天使的翅膀下面。 8基路伯天使展開翅膀,遮蓋約櫃和抬約櫃的橫杠。 9橫杠非常長,在至聖所前面的聖所中也看得見橫杠的末端,但在聖所外面看不見。橫杠至今仍在那裡。 10約櫃裡除了兩塊石版,沒有別的東西。石版是以色列人離開埃及後,耶和華在何烈山跟他們立約時,摩西放進去的。

耶和華的榮耀

11隨後,祭司退出聖所,所有在場的祭司不分班次都已潔淨自己。 12所有負責歌樂的利未亞薩希幔耶杜頓,以及他們的兒子和親族都穿著細麻布衣服,站在祭壇的東邊,敲鈸、鼓瑟、彈琴,同時還有一百二十位祭司吹號。 13吹號的和歌樂手一起同聲讚美和稱謝耶和華,伴隨著號、鈸及各種樂器的聲音,高聲讚美耶和華:

「祂是美善的,

祂的慈愛永遠長存!」

那時,有雲彩充滿了耶和華的殿, 14以致祭司不能在殿裡供職,因為殿裡充滿了耶和華上帝的榮光。