2 Mbiri 4 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 4:1-22

Zipangizo za mʼNyumba ya Mulungu

1Solomoni anapanga guwa lamkuwa limene mulitali mwake linali mamita asanu ndi anayi, mulifupi mwakenso mamita asanu ndi anayi ndipo msinkhu wake unali mamita anayi ndi theka. 2Kenaka iye anapanga mbiya yayikulu yachitsulo. Inali yozungulira ndipo pakamwa pake panali pa mamita anayi ndi theka, poyeza modutsa pakati pake. Msinkhu wake unali wopitirirapo mamita awiri. Thunthu lake linali mamita 13. 3Mʼmunsi mwa mkombero wa mbiyayo anajambulamo zithunzi zangʼombe zazimuna mozungulira, zithunzi khumi pa theka la mita. Ngʼombezo zimajambulidwa mʼmizere iwiri ndipo anazipangira kumodzi ndi mbiyayo.

4Mbiyayo anayisanjika pa ngʼombe zamkuwa khumi ndi ziwiri, zitatu zoyangʼana kumpoto, zitatu zoyangʼana kumadzulo, zitatu zoyangʼana kummwera ndipo zitatu zoyangʼana kummawa. Mbiyayo inakhazikika pamwamba pa ngʼombezo, ndipo miyendo yake yonse yakumbuyo ya ngʼombezo inkaloza mʼkati. 5Mbiyayo inali yochindikala ngati chikhatho ndipo mkombero wake unali ngati mkombero wa chikho, ngati duwa lokongola kwambiri. Mʼmbiyamo munkalowa madzi okwana malita 60,000.

6Kenaka anapanga mabeseni khumi otsukira zinthu ndipo asanu amawayika mbali ya kummwera, asanu mbali ya kumpoto. Mʼmenemo amatsukiramo zinthu zimene zimagwiritsidwa ntchito pa nsembe zopsereza koma mbiyamo ndi mʼmene ankasambiramo ansembe.

7Solomoni anapanga zoyikapo nyale khumi zagolide monga momwe kunalembedwera ndipo anaziyika mʼNyumba ya Mulungu, zisanu mbali ya kummwera, ndi zisanu mbali ya kumpoto.

8Iye anapanga matebulo khumi ndipo anawayika mʼNyumba ya Mulungu, asanu mbali ya kummwera ndi asanu mbali ya kumpoto. Iye anapanganso mabeseni agolide okwanira 100.

9Iye anapanga bwalo la ansembe, bwalo lalikulu ndi zitseko za bwalolo ndipo anakuta zitsekozo ndi mkuwa. 10Anayika mbiya ija mbali yakummwera pamene mbali ya kummawa ndi kummwera zimakumana.

11Iye anapanganso miphika ndi mafosholo ndi mabeseni owazira magazi.

Kotero Hiramu anatsiriza ntchito yonse ya ku Nyumba ya Mulungu imene ankagwirira Mfumu Solomoni:

12Nsanamira ziwiri;

mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

maukonde awiri okongoletsera mbale ziwiri za mitu yapamwamba pa nsanamirazo;

13makangadza 400 a maukonde awiri okongoletserawo (mizere iwiri ya makangadza pa ukonde uliwonse, kukongoletsa mbale za mitu yapamwamba pa nsanamira);

14miyendo pamodzi ndi mabeseni ake;

15mbiya pamodzi ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri zazimuna zosanjikapo mbiyayo.

16Miphika, mafosholo, mafoloko otengera nyama ndi ziwiya zina zonse.

Zipangizo zonse zimene Hiramu Abi anapangira Mfumu Solomoni za mʼNyumba ya Yehova zinali zamkuwa wonyezimira. 17Mfumu inapangitsa zimenezi mʼchigwa cha Yorodani, ku malo amtapo amene anali pakati pa Sukoti ndi Zaretani. 18Zinthu zonse zimene Solomoni anapanga zinali zochuluka kwambiri kotero kuti kulemera kwa mkuwa sikunadziwike.

19Solomoni anapanganso ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Mulungu:

guwa lansembe lagolide;

matebulo pamene ankayikapo buledi woperekedwa kwa Mulungu;

20zoyikapo nyale zagolide ndi nyale zake zagolide weniweni, kuti ziziyaka mʼkati mwenimweni mwa malo opatulika monga analembera,

21maluwa agolide, nyale ndi mbaniro. (Zinali zagolide mmodzi);

22zozimitsira nyale zagolide weniweni, mbale zowazira magazi, mbale ndi zofukizira; ndiponso zitseko zagolide za Nyumba ya Mulungu, chitseko cha ku Malo Opatulika Kwambiri ndi zitseko za ku chipinda chachikulu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

2 Летопись 4:1-22

Храмовые принадлежности

(3 Цар. 7:23-40)

1Сулаймон сделал бронзовый жертвенник десяти метров в длину, десяти в ширину и пяти метров4:1 Букв.: «двадцати… двадцати… десяти локтей». в высоту. 2Он вылил из бронзы большой круглый бассейн, названный «морем», который был пяти метров в диаметре, двух с половиной метров высотой и пятнадцати метров4:2 Букв.: «десять… пять… тридцать локтей». в окружности. 3Снизу его окружали два ряда подобия быков – по десять на каждые полметра. Быки были отлиты с бассейном одним литьём.

4Бассейн стоял на двенадцати быках, три из которых смотрели на север, три на запад, три на юг и три на восток. Бассейн покоился на них, а их зады были обращены внутрь, к центру. 5Его стенки были восемь сантиметров толщиной, а его край был как край чаши, как цветок лилии. Бассейн вмещал в себя шестьдесят шесть тысяч литров4:5 Букв.: «одна ладонь… три тысячи батов». воды.

6Сулаймон сделал десять умывальниц и поставил пять из них на южной стороне и пять на северной. В них промывали части животных, предназначенные для всесожжения, а «морем» пользовались для омовений священнослужители.

7Он сделал десять светильников по установленному образцу и поставил их в храме, пять на южной стороне и пять на северной.

8Он сделал десять столов и поставил их в храме, пять на южной стороне и пять на северной. Ещё он сделал сто золотых кропильных чаш.

9Он сделал двор для священнослужителей, большой двор и двери для двора, и покрыл двери бронзой. 10Затем он поставил «море» на юго-восточном углу храма. 11Ещё Хурам-Ави сделал горшки, лопатки и кропильные чаши.

Список утвари храма

(3 Цар. 7:40-51)

На этом Хурам-Ави завершил всю работу, которую выполнял для царя Сулаймона в храме Всевышнего. Он сделал:

12две колонны,

две чашеобразные капители для колонн,

две сетки, украшавшие чашеобразные капители,

13четыреста плодов гранатового дерева для двух сеток (два ряда гранатов для каждой сетки, украшавшей чашеобразные капители),

14подставки с умывальницами,

15«море» и двенадцать быков под ним,

16горшки, лопатки, вилки для мяса и другие принадлежности.

Вся утварь, которую Хурам-Ави сделал царю Сулаймону для храма Вечного, была из полированной бронзы. 17Царь велел отлить её в глиняных формах в долине Иордана между Суккотом и Цартаном4:17 Букв.: «Цередата» – вариант названия Цартан (см. 3 Цар. 7:46).. 18Всей этой утвари, которую сделал Сулаймон, было так много, что веса бронзы, из которой она была сделана, не установили.

19Ещё Сулаймон сделал всю утварь для храма Всевышнего:

золотой жертвенник,

столы для священного хлеба,

20подсвечники из чистого золота со светильниками, чтобы они горели перед внутренним святилищем, как предписано,

21золотые цветы, светильники и щипцы (они были из чистого золота),

22ножницы для фитилей, кропильные чаши, блюда и сосуды для возжигания благовоний – всё из чистого золота,

а также золотые двери храма: внутренние двери в Святая Святых и внешние двери храма.