2 Mbiri 35 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 35:1-27

Yosiya Achita Chikondwerero cha Paska

1Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba. 2Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova. 3Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli. 4Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.

5“Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba. 6Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”

7Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.

8Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300. 9Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.

10Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira. 11Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo. 12Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe. 13Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse. 14Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.

15Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.

16Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya. 17Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri. 18Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu. 19Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.

Imfa ya Yosiya

20Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye. 21Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”

22Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.

23Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.” 24Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.

25Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.

26Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova, 27zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

2 Летопись 35:1-27

Возобновление праздника Освобождения

(4 Цар. 23:21-23)

1Иосия устроил в Иерусалиме праздник Освобождения35:1 См. сноску на 30:1. в честь Вечного, и в четырнадцатый день первого месяца (ранней весной) закололи жертвенного ягнёнка. 2Иосия определил священнослужителям их обязанности и ободрил их, чтобы им совершать служение в храме Вечного. 3Он сказал левитам, наставникам всего Исраила, которые были посвящены Вечному:

– Поставьте священный сундук в храме, который построил Сулейман, сын Давуда, царя Исраила. Вам больше не нужно переносить его на своих плечах. Служите отныне Вечному и Его народу Исраилу. 4Приготовьтесь к службе в храме по вашим кланам, в соответствии с указаниями, данными царём Исраила Давудом и его сыном Сулейманом. 5Стойте в святилище с группами левитов. Сделайте это для каждого клана, чтобы вы могли помочь людям. 6Заколите жертвенных ягнят, освятитесь и приготовьте ягнят для ваших соплеменников, исполняя всё, что повелел через Мусу Вечный.

7Иосия дал всем исраильтянам, которые были там, общим счётом тридцать тысяч голов мелкого скота – ягнят и козлят для жертвенных приношений, и три тысячи голов крупного скота. Всё это из имущества царя. 8Его приближённые тоже добровольно жертвовали народу, священнослужителям и левитам. Хилкия, Закария и Иехиил, ответственные за храм Аллаха, дали священнослужителям к празднику, в жертву Аллаху, две тысячи шестьсот голов мелкого скота и триста крупного. 9Хонания со своими братьями Шемаей и Нетанилом и вождями левитов Хашавией, Иеилом и Иозавадом дали левитам к празднику пять тысяч голов мелкого скота и пятьсот голов крупного.

10Когда всё было приготовлено к службе, священнослужители встали на свои места, а левиты – по своим группам, как повелел царь. 11Жертвенные ягнята были заколоты, и священнослужители кропили переданной им кровью, пока левиты свежевали животных. 12Они отложили предназначенное для всесожжения, чтобы потом раздать народу по семействам для приношения Вечному, как написано в Таурате, в книге Мусы. То же они сделали и с крупным скотом. 13Они совершили огненную жертву к празднику Освобождения, по обычаю сварили священные жертвы в горшках, котлах и кастрюлях и поспешно раздали всему народу, 14а после, приготовили для себя и для священнослужителей, потому что священнослужители, потомки Харуна, были заняты, принося всесожжения и жир животных до самой ночи. Поэтому левиты приготовили и для себя, и для священнослужителей, потомков Харуна. 15Музыканты, потомки Асафа, находились на местах, определённых им Давудом, Асафом, Еманом и царским провидцем Иедутуном. Привратникам не нужно было оставлять своих постов, потому что их собратья-левиты всё приготовили для них.

16Так вся служба Вечного была исполнена в тот день, чтобы отметить праздник Освобождения и принести всесожжения на жертвеннике Вечного, как повелел царь Иосия. 17Исраильтяне, которые были там, отмечали в то время праздник Освобождения и семь дней отмечали праздник Пресных хлебов. 18Такого праздника, как этот, не отмечали в Исраиле со дней пророка Шемуила. И никто из царей Исраила не отмечал такого праздника Освобождения, как отмечал Иосия со священнослужителями, левитами и всем народом Иудеи и Исраила, который был там с жителями Иерусалима. 19Этот праздник Освобождения отмечался на восемнадцатом году правления Иосии.

Смерть Иосии

(4 Цар. 23:28-30)

20После всего этого, когда Иосия привёл храм в порядок, Нехо35:20 Нехо II, правивший Египтом с 610 по 595 гг. до н. э., пошёл на помощь Ашшурубаллиту II, последнему царю Ассирии, воевавшему с Вавилоном., царь Египта, пошёл войной на город Каркемиш на реке Евфрат, и Иосия выступил, чтобы встретиться с ним в бою. 21Но Нехо послал к нему вестников, говоря:

– Что за распря у нас с тобой, царь Иудеи? Я сегодня иду не на тебя, но на царство, с которым враждую. Аллах велел мне торопиться, так что не противься Аллаху, Который со мною, иначе Он погубит тебя.

22Но Иосия не ушёл, а переоделся, чтобы в бою быть неузнанным. Он не послушал того, что Нехо сказал по повелению Аллаха, но пошёл сразиться с ним на равнине Мегиддо. 23Лучники попали в Иосию, и тогда он сказал своим слугам:

– Уведите меня, я тяжело ранен.

24Они взяли его из его колесницы, положили в другую колесницу, которая у него была, привезли в Иерусалим, и там он умер. Его похоронили в гробницах его предков, и вся Иудея и Иерусалим оплакивали его.

25Иеремия сложил плач по Иосии, и до сегодняшнего дня певцы и певицы вспоминают об Иосии в плачах. Они вошли в Исраиле в обиход и записаны в «Книге плачей».

26Прочие события царствования Иосии и его добрые дела, совершённые по написанному в Законе Вечного, – 27все события, от первых до последних, записаны в «Книге царей Исраила и Иудеи».