2 Mbiri 35 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 35:1-27

Yosiya Achita Chikondwerero cha Paska

1Yosiya anachita chikondwerero cha Paska wa Yehova mu Yerusalemu, ndipo mwana wankhosa wa Paska anaphedwa pa tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi woyamba. 2Iye anasankha ansembe pa maudindo awo ndipo anawalimbikitsa pa ntchito ya mʼnyumba ya Yehova. 3Iye anati kwa Alevi amene amalangiza Aisraeli onse omwe anadzipatula kwa Yehova: Ikani bokosi lopatulika mʼNyumba ya Mulungu amene Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli anamanga. Lisamanyamulidwe pa mapewa anu. Tsopano tumikirani Yehova Mulungu wanu ndi anthu ake Aisraeli. 4Mukhale mʼmagulu anu molingana ndi mabanja anu, molingana ndi momwe analembera Davide mfumu ya Israeli ndiponso mwana wake Solomoni.

5“Muziyima ku malo opatulika pamodzi ndi gulu la Alevi oyimira gulu lililonse lalingʼono la mabanja a abale anu amene ndi anthu wamba. 6Muzipha ana ankhosa a Paska, muzidzipatula nokha ndi kuwakonzera abale anu ana ankhosa awo, kuchita zimene Yehova analamulira mwa Mose.”

7Yosiya anapereka kwa anthu wamba onse ana ankhosa ndi ana ambuzi okwanira 30,000 ndi ngʼombe zazimuna 3,000, zopereka za Paska zonse zochokera pa chuma chake cha mfumu.

8Akuluakulu akenso anapereka mwaufulu kwa anthu ndi kwa ansembe ndi Alevi. Hilikiya, Zekariya ndi Yehieli oyangʼanira ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu anapereka kwa ansembe zopereka za Paska 2,600 ndi ngʼombe 300. 9Konaniya nayenso pamodzi ndi Semaya ndi Netaneli, abale ake ndi Hasabiya, Yeiyeli ndi Yozabadi, atsogoleri a Alevi, anapereka nsembe za Paska 5,000 ndi ngʼombe 500 kwa Alevi.

10Mwambo unakonzedwa ndipo ansembe anayima pamalo pawo pamodzi ndi Alevi mʼmagulu awo monga mfumu inalamulira. 11Ana ankhosa a Paska anaphedwa ndipo ansembe anawaza magazi amene anaperekedwa kwa iwo pamene Alevi anali kusenda nyamazo. 12Iwo anayika padera nsembe zopsereza kuti azipereke kwa magulu angʼonoangʼono a mabanja a anthu kuti apereke kwa Yehova monga zinalembedwa mʼbuku la Mose. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi ngʼombe. 13Anawotcha nyama za Paska monga momwe zinalembedwera ndi kuwiritsa zopereka zopatulika mʼmiphika, mʼmitsuko ndi mʼziwaya ndipo anazipereka mofulumira kwa anthu onse. 14Izi zitatha, anakonza zawo ndi za ansembe chifukwa ansembe, zidzukulu za Aaroni, anali otanganidwa kupereka nsembe zopsereza ndi mafuta a nyama mpaka madzulo. Choncho Alevi amakonza zawo ndi za ansembe, ana a Aaroni.

15Anthu oyimba nyimbo, zidzukulu za Asafu, anali pa malo awo potsata zomwe analemba Davide, Asafu, Hemani ndi Yedutuni mlosi wa mfumu. Alonda apazipata anali pa chipata chilichonse ndipo kunali kosafunika kuti achoke pa ntchito yawo, poti abale awo Alevi ankawakonzera zonse.

16Kotero pa nthawi imeneyi ntchito yonse ya Yehova ya chikondwerero cha Paska ndi nsembe zopsereza pa guwa la Yehova inachitika monga analamulira mfumu Yosiya. 17Aisraeli amene analipo anachita chikondwerero cha Paska pa nthawi imeneyi ndi kuchita mwambo wa chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti, kwa masiku asanu ndi awiri. 18Paska yofanana ndi iyi sinachitikepo ku Israeli kuyambira nthawi ya Samueli ndipo palibe mmodzi mwa mafumu a Israeli anachitapo chikondwerero cha Paska ngati anachitira Yosiya pamodzi ndi ansembe, Alevi ndi Ayuda onse ndi Aisraeli amene anali pamodzi ndi anthu a mu Yerusalemu. 19Chikondwerero cha Paska ichi chinachitika mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya.

Imfa ya Yosiya

20Zimenezi zitachitika, pamene Yosiya anakonzanso Nyumba ya Mulungu, Neko mfumu ya Igupto inapita kukachita nkhondo ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate, ndipo Yosiya anapita kukamenyana naye. 21Koma Neko anatumiza amithenga kwa iye kunena kuti, “Kodi pali mkangano wanji pakati pa iwe ndi ine, iwe mfumu ya Yuda? Ine sindikuthira nkhondo iwe pa nthawi ino, koma nyumba imene ndili nayo pa nkhondo. Mulungu wandiwuza kuti ndifulumize choncho leka kutsutsana ndi Mulungu amene ali ndi ine, mwina adzakuwononga.”

22Komabe Yosiya sanatembenuke kumusiya iyeyo, koma anadzizimbayitsa ndi kukalowa mʼnkhondo. Iye sanamvere zimene Neko ananena molamulidwa ndi Mulungu koma anapita kukamenyana naye ku chigwa ku Megido.

23Anthu oponya mivi analasa mfumu Yosiya, ndipo iye anawuza akuluakulu ake, “Chotseni. Ndavulazidwa kwambiri.” 24Choncho anamuchotsa iye mʼgaleta lake, ndipo anamuyika mʼgaleta lina limene anali nalo ndipo anabwera naye ku Yerusalemu kumene anamwalirira. Iye anayikidwa mʼmanda a makolo ake. Ndipo Ayuda ndi Yerusalemu yense anamulira.

25Yeremiya anapeka nyimbo za maliro chifukwa cha Yosiya, ndipo mpaka lero lino amuna ndi akazi onse oyimba amakumbukira Yosiya pa nyimbo zawo za maliro. Izi zinakhala mwambo mu Israeli ndipo zinalembedwa mʼNyimbo za Maliro.

26Zochitika zina za ulamuliro wa Yosiya ndi ntchito za kudzipereka kwake, monga zinalembedwa mʼMalamulo a Yehova, 27zochitika zonse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda.

Bibelen på hverdagsdansk

2. Krønikebog 35:1-27

Josias befaler, at der skal holdes påske igen

2.Kong. 23,21-23

1Josias bekendtgjorde nu, at der skulle fejres påske i Jerusalem på den 14. dag i årets første måned. På den dag skulle påskelammene slagtes. 2Som en del af forberedelserne indsatte han præsterne i deres tjeneste og opmuntrede dem til at tage vare på deres arbejde i templet. 3Til levitterne, som skulle undervise Israels folk og var indviet til at tjene Herren, sagde han: „Da pagtens ark nu står i det tempel, Salomon fik bygget, og da I derfor ikke længere skal bruge tid og kræfter på at bære rundt på den, skal I i stedet bruge jeres tid på at tjene Herren og hans folk, Israel. 4I skal fordele arbejdet efter de skiftehold, som kong David og hans søn Salomon i sin tid etablerede, og som bygger på, hvilke slægter I kommer fra. 5Hvert hold skal så tage opstilling på deres angivne plads og hjælpe dem, der kommer for at ofre i templet. 6I skal slagte påskelammene og sørge for at være indviet til tjeneste, så I kan hjælpe hele folket, mens I følger alle forskrifterne i Moses’ lov.”

7Kongen skænkede personligt 30.000 stykker småkvæg, enten lam eller gedekid, samt 3000 stykker hornkvæg til festen. 8Kongens embedsmænd og andre ledere gav også rundhåndet af, hvad de ejede, til præsterne, levitterne og de øvrige festdeltagere. Hilkija, Zekarja og Jehiel, som havde overopsyn med templet, forærede præsterne 2600 stykker småkvæg og 300 stykker hornkvæg. 9De levitiske ledere Konanja, hans brødre Shemaja og Netanel, Hashabja, Jeiel og Jozabad skænkede 5000 stykker småkvæg og 500 stykker hornkvæg til levitterne.

10Da alle forberedelser til påskefesten var fuldført, stillede præsterne sig på deres post i templet, og levitterne tog opstilling i hold, som kongen havde befalet. 11Levitterne slagtede påskelammene og gav det opsamlede blod til præsterne, der stænkede det på alteret, mens levitterne flåede og parterede dyrene. 12De dele, der skulle bringes som brændofre, blev givet til familieoverhovederne, som så bragte dem til præsterne til ofring ifølge forskrifterne i Moses’ lov. De andre dyr blev på tilsvarende måde slagtet, flået og parteret i løbet af ugen. 13De dele fra påskelammet, som folk måtte spise, blev stegt og givet til folk. Kødet fra de øvrige dyr blev derimod kogt i gryder, kar og pander og derefter givet til folket. 14Da folket havde fået deres påskelam, tilberedte levitterne påskelammet til sig selv og præsterne, der hele dagen havde haft travlt med at ofre fedtet og det, der ellers skulle brændes på brændofferalteret.

15Sangerne, som kom fra Asafs slægt, var på plads ifølge de regler, som kong David, Asaf, Heman og profeten Jedutun århundreder forinden havde bestemt. Portvagterne stod vagt, og de behøvede ikke at forlade deres post, for andre levitter klarede påskeofferet for dem.

16Sådan blev der holdt påske for Herren den dag efter alle forskrifterne. Lammene blev slagtet og brændofrene bragt på det store alter, som kong Josias havde befalet. 17Alle de israelitter, som boede i Jerusalem eller var rejst derhen, tog del i påskefesten, som de næste syv dage efterfulgtes af de usyrnede brøds fest. 18Ikke siden profeten Samuels tid havde man fejret påske i Israel efter alle forskrifterne. Ingen konge før Josias havde holdt en så storslået påskehøjtid sammen med præsterne, levitterne og folk fra hele Jerusalem, Juda og Israel. 19Denne begivenhed fandt sted i kong Josias’ 18. regeringsår.

Resten af Josias’ regeringstid

2.Kong. 23,28-30a

20Nogle år efter at Josias havde restaureret templet, var kong Neko af Egypten på vej mod Karkemish ved Eufratfloden med sin hær. Josias drog ud med sin hær for at standse ham, 21men Neko sendte følgende besked til Josias: „Denne krig angår ikke dig, judæerkonge! Lad mig være, så jeg kan koncentrere mig om at bekæmpe min fjende, for Gud har sagt, at jeg skal skynde mig. Lad være med at komme på tværs af Guds planer, ellers bliver du dræbt.”

22Men Josias ville ikke lytte til den advarsel, som Gud gav ham gennem Neko. Han førte sin hær til kamp på sletten ved Megiddo. Af sikkerhedshensyn tog han dog sin kongedragt af, før kampen begyndte. 23Alligevel blev han ramt af en dødbringende pil. „Hurtigt,” råbte han til sine livvagter, „tag mig væk fra fronten. Jeg er hårdt såret.”

24Mændene skyndte sig at bære ham over i en anden stridsvogn, og derefter kørte de ham hjem til Jerusalem, hvor han døde kort efter. Han blev begravet i det kongelige gravsted tæt ved sine forfædre, og hele Juda og Jerusalem sørgede over hans død.

25Profeten Jeremias digtede en sørgesang over kong Josias. Siden har mange sangere, både mænd og kvinder, sunget denne sørgesang, og den er nedskrevet i bogen med klagesange.

26-27Resten af kong Josias’ liv og virke fra begyndelsen til enden, inklusive hans iver efter at tjene Herren og følge Toraen i et og alt, er beskrevet i Israels og Judas kongers krønikebog.