2 Mbiri 33 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 33:1-25

Manase Mfumu ya Yuda

1Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 55. 2Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira machitidwe a mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli. 3Iyeyo anamanganso malo opembedzerapo mafano amene Hezekiya abambo ake anawaphwasula; anamanganso maguwa ansembe a Baala ndi kupanga mafano a Asera. Iye amagwadira zolengedwa zonse zamlengalenga ndi kumazipembedza. 4Manase anamanga maguwa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Ine ndidzakhala mu Yerusalemu mpaka muyaya.” 5Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova anamangamo maguwa ansembe a zolengedwa zonse zamlengalenga. 6Iye ankakapereka ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza ku chigwa cha Hinomu, ankachita zamatsenga, kuwombeza ndi ufiti, ankakafunsira kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Iye anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova, kumukwiyitsa Iyeyo.

7Manase anatenga fano losema limene anapanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Mulungu, zimene Mulungu ananena kwa Davide ndi kwa mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba ya Mulungu muno, mu Yerusalemu muno, malo amene ndawasankha pakati pa mafuko onse a Israeli, ndidzakhalamo mpaka muyaya. 8Ine sindidzachotsanso phazi la Aisraeli kuchoka mʼdziko limene ndawapatsa makolo ako, ngatitu iwowa adzasamalira kuchita chilichonse chimene ndinawalamulira za malamulo onse, malangizo ndi miyambo imene inapatsidwa kudzera mwa Mose.” 9Koma Manase anasocheretsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu, kotero anachita zoyipa zambiri kupambana mitundu imene Yehova anayiwononga pamaso pa Aisraeli.

10Yehova anayankhula kwa Manase ndi anthu ake, koma iwo sanasamaleko. 11Kotero Yehova anawatumizira atsogoleri a ankhondo a ku Asiriya amene anagwira Manase ukapolo, anayika ngowe mʼmphuno mwake, namumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni. 12Ali pa mavuto akewo anafunafuna kuti Yehova Mulungu wake amukomere mtima ndipo anadzichepetsa kwakukulu pamaso pa Mulungu wa makolo ake. 13Ndipo atapemphera, Yehova anakhudzidwa ndi kupempha kwakeko ndipo anamvera madandawulo ake. Kotero anamubweretsanso ku Yerusalemu ndi ku ufumu wake. Ndipo Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu.

14Zitapita izi iye anamanga khoma la kunja kwa Mzinda wa Davide kumadzulo kwa kasupe wa Gihoni ku chigwa mpaka polowera ku Chipata cha Nsomba kuzungulira phiri la Ofeli. Iyeyo anakweza kwambiri khomalo. Anayikanso atsogoleri a nkhondo ku mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda.

15Iye anachotsa milungu yonse yachilendo ndi fano mʼNyumba ya Yehova komanso maguwa ansembe onse amene anamanga pa phiri la Nyumba ya Mulungu ndi mu Yerusalemu, nazitayira kunja kwa mzinda. 16Kenaka anabwezeretsa guwa lansembe la Yehova ndi kupereka zopereka zachiyanjano ndiponso zopereka zamatamando ndipo anawuza Yuda kuti atumikire Yehova Mulungu wa Israeli. 17Komabe anthu anapitiriza kupereka nsembe ku malo achipembedzo, koma kwa Yehova, Mulungu wawo yekha.

18Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Manase, kuphatikiza mapemphero ake kwa Mulungu wake ndi mawu amene alosi anayankhula kwa iye mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli, zalembedwa mʼmabuku a mafumu a Israeli. 19Pemphero lake ndi momwe Mulungu anakhudzidwira ndi kupempha kwakeko, pamodzinso ndi machimo ake onse ndi kusakhulupirika kwake, ndiponso malo onse amene anamanga, malo azipembedzo ndi mafano a Asera ndi mafano asanadzichepetse, zonse zalembedwa mʼmbiri ya alosi. 20Manase anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yake yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Amoni Mfumu ya Yuda

21Amoni anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka ziwiri. 22Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga anachitira Manase abambo ake. Amoni analambira ndi kupereka nsembe kwa mafano onse amene anapanga Manase. 23Koma kusiyana ndi abambo ake Manase, iye sanadzichepetse pamaso pa Yehova. Amoni anawonjeza kulakwa kwake.

24Akuluakulu a Amoni anamuchita chiwembu ndipo anamupha mʼnyumba yake yaufumu. 25Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anakonzera chiwembu mfumu Amoni, ndipo anayika mwana wake Yosiya kukhala mfumu mʼmalo mwake.

La Bible du Semeur

2 Chroniques 33:1-25

Manassé, roi de Juda

(2 R 21.1-10)

1Manassé était âgé de douze ans à son avènement. Il régna cinquante-cinq ans à Jérusalem33.1 Environ de 697 à 642 av. J.-C., avec une éventuelle corégence avec son père Ezéchias si celui-ci a vécu jusqu’en 686 av. J.-C. ( voir note sur 29.1).. 2Il fit ce que l’Eternel considère comme mal et s’adonna aux mêmes pratiques abominables que les peuples étrangers dépossédés par l’Eternel en faveur des Israélites. 3Il rebâtit les hauts lieux que son père Ezéchias avait démolis, il érigea des autels aux Baals, et dressa des poteaux sacrés à la déesse Ashéra. Il se prosterna devant tous les astres du ciel et leur rendit un culte. 4Il construisit des autels païens dans le temple de l’Eternel, malgré cette parole de l’Eternel : C’est là, à Jérusalem, que j’établirai pour toujours ma présence33.4 Voir 2 Ch 7.16..

5Il érigea des autels en l’honneur de tous les astres du ciel dans les deux parvis du temple de l’Eternel. 6Il alla même jusqu’à brûler ses fils pour les offrir en sacrifice dans la vallée de Ben-Hinnom33.6 Voir Lv 20.2-5 ; Dt 12.31 ; 18.10.. Il consultait les augures, les devins et les magiciens. Il installa des gens qui évoquaient les morts et qui prédisaient l’avenir33.6 Voir Dt 18.9-14.. Il multiplia les actes que l’Eternel considère comme mauvais, et l’irrita de cette manière. 7Il fit dresser dans le Temple l’idole sculptée qu’il avait fabriquée, alors que Dieu avait déclaré à David et à son fils Salomon : C’est dans ce temple et dans Jérusalem, que j’ai choisie parmi toutes les tribus d’Israël, que j’établirai pour toujours ma présence. 8Si les Israélites s’appliquent à obéir à tout ce que je leur ai commandé, à toute la Loi, les ordonnances et les articles de droit qu’ils ont reçus par l’intermédiaire de Moïse, je ne leur ferai plus quitter le pays que j’ai attribué à leurs ancêtres33.8 Voir 1 Ch 17.7-15 ; 2 Ch 6.4-11 ; 2 Ch 7.12-22 ; 1 R 2.2-4..

9Mais Manassé égara le peuple de Juda et les habitants de Jérusalem, de sorte qu’ils firent encore plus de mal que les peuples étrangers que l’Eternel avait exterminés au profit des Israélites. 10L’Eternel adressa des avertissements à Manassé et à son peuple, mais ils n’écoutèrent pas.

La réaction de Dieu

11Alors l’Eternel fit venir contre eux les généraux du roi d’Assyrie33.11 Le roi Esar-Haddôn (681 à 669 av. J.-C.), fils et successeur de Sennachérib, ou, plus probablement, son successeur Assourbanipal., qui capturèrent Manassé. Ils lui mirent des crochets au nez, l’attachèrent avec des chaînes de bronze et l’emmenèrent à Babylone. 12Lorsqu’il fut dans la détresse, il implora l’Eternel son Dieu et s’humilia profondément devant le Dieu de ses ancêtres. 13Il le pria, et l’Eternel l’exauça, il écouta sa supplication et le fit revenir à Jérusalem dans son royaume. Ainsi Manassé comprit que l’Eternel seul est Dieu.

14Après ces événements, il construisit à l’extérieur de la Cité de David un rempart qui passait à l’ouest des sources de Guihôn, longeait la vallée du Cédron jusqu’à l’entrée de la porte des Poissons et contournait l’Ophel. Manassé lui donna une très grande hauteur. Il établit aussi des chefs militaires dans toutes les villes fortifiées de Juda. 15Il fit disparaître du temple de l’Eternel les dieux étrangers et la statue, ainsi que les autels qu’il avait édifiés sur la colline du Temple et dans Jérusalem. Et on les jeta hors de la ville. 16Il rebâtit l’autel de l’Eternel. Il offrit des sacrifices de communion et de reconnaissance et il ordonna aux Judéens de rendre leur culte à l’Eternel, le Dieu d’Israël. 17A vrai dire, le peuple continuait à offrir des sacrifices sur les hauts lieux, mais seulement à l’Eternel son Dieu.

(2 R 21.17-18)

18Les autres faits et gestes de Manassé, la prière qu’il adressa à son Dieu et les messages que les prophètes lui adressèrent de la part de l’Eternel, le Dieu d’Israël, se trouvent dans les Actes des rois d’Israël33.18 Voir 1 R 14.19 ; 2 Ch 16.11.. 19Sa prière et l’exaucement que Dieu lui accorda, toutes ses fautes et son infidélité envers Dieu, la liste des endroits où il bâtit des hauts lieux et où il dressa des pieux sacrés d’Ashéra et des statues avant de s’humilier, tout cela est cité dans les Actes de Hozaï33.19 Hozaï: personnage inconnu. Un manuscrit hébreu et l’ancienne version grecque ont : des prophètes.. 20Manassé rejoignit ses ancêtres décédés, et on l’enterra dans son palais. Son fils Amôn lui succéda sur le trône.

Le bref règne d’Amôn

(2 R 21.19-24)

21Amôn avait vingt-deux ans à son avènement et il régna deux ans à Jérusalem33.21 De 642 à 640 av. J.-C.. 22Il fit ce que l’Eternel considère comme mal, comme l’avait fait son père Manassé. Il sacrifia à toutes les idoles que son père Manassé avait fait dresser et leur rendit un culte. 23Il ne s’humilia pas devant l’Eternel comme l’avait fait son père Manassé. Au contraire, il se rendit extrêmement coupable. 24Ses ministres conspirèrent contre lui et l’assassinèrent dans son palais. 25Mais la population du pays massacra tous ceux qui avaient comploté contre le roi Amôn et proclama son fils Josias roi à sa place.