2 Mbiri 29 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 29:1-36

Mfumu Hezekiya Ayeretsa Nyumba ya Mulungu

1Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya. 2Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.

3Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza. 4Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa 5ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika. 6Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira. 7Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli. 8Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino. 9Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo. 10Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere. 11Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”

12Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito:

Kuchokera ku banja la Kohati,

Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya;

kuchokera ku banja la Merari,

Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli;

kuchokera ku banja la Geresoni,

Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;

13kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani,

Simiri ndi Yeiyeli;

kuchokera kwa zidzukulu za Asafu,

Zekariya ndi Mataniya;

14kuchokera kwa zidzukulu za Hemani,

Yehieli ndi Simei;

kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni,

Semaya ndi Uzieli.

15Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova. 16Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni. 17Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.

18Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse. 19Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”

20Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova. 21Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova. 22Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe. 23Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo. 24Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.

25Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri. 26Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.

27Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli. 28Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.

29Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira. 30Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.

31Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.

32Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova. 33Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000. 34Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe. 35Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza.

Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso. 36Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.

Bibelen på hverdagsdansk

2. Krønikebog 29:1-36

Kong Hizkija af Juda genåbner templet

2.Kong. 18,2-3

1Hizkija var 25 år gammel, da han blev konge, og han regerede i Jerusalem i 29 år. Hans mor hed Abija og var datter af Zekarja.

2Hizkija gjorde, hvad der var ret i Herrens øjne, akkurat som sin forfar kong David. 3Allerede i sit første regeringsår, i årets første måned, sørgede han for, at Herrens hus blev åbnet og indgangsdørene istandsat. 4Det første, han gjorde, var at indkalde de ledende præster og levitter til at mødes med ham på den åbne plads øst for templet. 5Så sagde han til dem:

„Hør godt efter, levitter! I skal begynde med at rense jer selv og derefter rense jeres forfædres Guds bolig. Alt det urene skal fjernes fra helligdommen. 6Vores forældre var troløse over for Herren. De gjorde, hvad der var ondt i hans øjne, og svigtede ham. De vendte ryggen til ham og lod templet forfalde. 7De slukkede lamperne og barrikaderede dørene til forhallen. De holdt op med at bringe brændofre og røgelsesofre til Israels Gud i helligdommen. 8Derfor ramte Herrens vrede Judas og Jerusalems indbyggere, så de blev undertrykt, mishandlet og hånet. I har selv set det. 9Vores fædre blev dræbt i krig, og vores sønner, døtre og koner er i fangenskab.

10Men nu vil jeg genoprette vores pagt med Herren, Israels Gud, for at han ikke længere skal være vred på os. 11I levitter må ikke længere forsømme jeres pligter. Herren har jo udvalgt jer til at gå ind i helligdommen, til at tjene ham på folkets vegne og bringe ofre til ham.”

12Det forslag syntes lederne godt om. Der var følgende levitter til stede ved mødet: Fra Kehats slægt: Mahat, søn af Amasaj, og Joel, søn af Azarja; fra Meraris slægt: Kish, søn af Abdi, og Azarja, søn af Jehallelel; fra Gershons slægt: Joa, søn af Zimma, og Eden, søn af Joa; 13fra Elitzafans slægt: Shimri og Jeuel; fra Asafs slægt: Zekarja og Mattanja; 14fra Hemans slægt: Jehiel og Shimi; fra Jedutuns slægt: Shemaja og Uzziel.

15Disse ledere fik fat i de andre levitter, og de gennemgik alle de foreskrevne renselsesceremonier. Derefter gik de i gang med at rydde op i templet i overensstemmelse med kongens befaling, der byggede på Herrens ord. 16Præsterne gik ind i selve helligdommen og bar alt det, som var blevet vanhelliget, ud i forgården. Derefter fragtede levitterne det videre ud af byen til Kedrondalen. 17Udrensningsarbejdet påbegyndtes den første dag i årets første måned. Efter otte dage var de nået til forhallen, og der gik otte dage mere med at rydde selve templet. De blev færdige på den 16. dag i den første måned.

18Derpå gik de op til kongen og sagde: „Vi har nu fuldført udrensningen. Vi har fjernet alt urent fra templet og sat brændofferalteret, bordet med de hellige brød og alle de tilhørende redskaber i stand. 19Alle de ting, som den troløse kong Ahaz vanhelligede, har vi renset og istandsat. De står nu foran brændofferalteret.”

20Tidligt næste morgen samlede kong Hizkija byens ledende mænd og gik i spidsen for dem op til templet. 21Med sig havde de syv ungtyre, syv væddere og syv lam til brændofre, samt syv gedebukke til syndofre. De skulle være syndofre for alle de synder, kongerne, præsterne og hele Judas folk tidligere havde begået. Hizkija gav derpå præsterne ordre til at begynde ofringen af de dyr, der skulle være brændoffer. 22Præsterne slagtede ungtyrene og stænkede blodet på alteret, og det samme gjorde de med vædderne og lammene. 23Gedebukkene, der var beregnet til syndofre, blev ført frem for lederne og for kongen, der alle lagde hænderne på dem. 24Så slagtede præsterne dem og udgød blodet over alteret som et sonoffer for hele Israels folk. Kongen havde sagt, at brændofrene og syndofrene skulle gælde hele Israels folk.

25Kongen opstillede levitterne i templet, for at de skulle spille på deres harper, lyrer og bækkener efter Davids forskrifter, og som Herren havde befalet gennem profeterne Gad og Natan. 26Levitterne stod så med de instrumenter, David havde indført, mens præsterne blæste i trompeterne. 27Derpå befalede kongen, at man lagde brændofrene på alteret og satte ild til. Samtidig begyndte lovsangen til Herren til akkompagnement af trompeter og de øvrige instrumenter. 28Hele forsamlingen tog del i tilbedelsen, som varede indtil alle ofrene var brændt. 29Derefter lagde kongen og de tilstedeværende sig på knæ i tilbedelse. 30Kongen og hans embedsmænd havde befalet levitterne at lovsynge Herren med kong Davids og profeten Asafs salmer. Det gjorde de med glæde, og bagefter knælede de også på jorden i tilbedelse.

31„Nu har I alle indviet jer til at tjene Herren,” sagde kong Hizkija. „Så kan I komme hen til templet med jeres lovprisningsofre til slagtning.” Folk kom derefter med deres lovprisningsofre, og nogle bragte frivillige brændofre. 32I alt kom de med 70 okser, 100 væddere og 200 lam som brændofre. 33Derudover kom de med 600 okser og 3000 stykker småkvæg som gaver til præsterne og levitterne. 34Der var endnu ikke tilstrækkelig mange præster, der havde indviet sig, så de var for få til at klare alle offerdyrene. Levitterne måtte derfor træde til og hjælpe, for de havde vist sig mere villige end præsterne til at indvi sig. 35Foruden det store antal brændofre var der også mange drikofre og en stor mængde fedt fra takofrene.

På den måde blev ofringstjenesten i Herrens hus genoprettet. 36Kong Hizkija og hele folket glædede sig over alt det, Gud havde hjulpet dem med at udrette på så kort tid.