2 Mbiri 29 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 29:1-36

Mfumu Hezekiya Ayeretsa Nyumba ya Mulungu

1Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya. 2Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.

3Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza. 4Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa 5ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika. 6Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira. 7Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli. 8Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino. 9Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo. 10Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere. 11Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”

12Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito:

Kuchokera ku banja la Kohati,

Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya;

kuchokera ku banja la Merari,

Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli;

kuchokera ku banja la Geresoni,

Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;

13kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani,

Simiri ndi Yeiyeli;

kuchokera kwa zidzukulu za Asafu,

Zekariya ndi Mataniya;

14kuchokera kwa zidzukulu za Hemani,

Yehieli ndi Simei;

kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni,

Semaya ndi Uzieli.

15Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova. 16Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni. 17Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.

18Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse. 19Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”

20Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova. 21Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova. 22Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe. 23Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo. 24Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.

25Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri. 26Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.

27Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli. 28Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.

29Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira. 30Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.

31Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.

32Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova. 33Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000. 34Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe. 35Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza.

Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso. 36Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.

La Bible du Semeur

2 Chroniques 29:1-36

Le roi Ezéchias purifie le Temple

(2 R 18.2-3)

1Ezéchias était âgé de vingt-cinq ans lorsqu’il commença à régner et il régna vingt-neuf ans à Jérusalem29.1 Soit de 715 à 686 av. J.-C., soit plutôt de 728 à 698 av. J.-C., avec un temps de corégence avec son père Ahaz jusqu’en 715.. Sa mère s’appelait Abiya, elle était fille de Zacharie. 2Il fit ce que l’Eternel considère comme juste, en tout point comme l’avait fait son ancêtre David.

3Au premier mois de la première année de son règne, il rouvrit les portes du temple de l’Eternel et les fit remettre en état29.3 Nécessaire après les déprédations d’Ahaz (28.24). La réparation des portes impliquait l’apposition de plaques d’or (2 R 18.16).. 4Il convoqua les prêtres et les lévites et les réunit sur la place orientale.

5Il leur dit : Ecoutez-moi, lévites ! Maintenant, rendez-vous rituellement purs, puis purifiez le temple de l’Eternel, le Dieu de vos ancêtres. Faites disparaître du sanctuaire tout ce qui le souille. 6Car nos pères ont été infidèles, ils ont fait ce que l’Eternel notre Dieu considère comme mal, ils l’ont abandonné, ils ont délaissé la demeure de l’Eternel et lui ont tourné le dos. 7Ils ont même fermé les portes du portique, ils ont éteint les lampes, ils ont cessé d’offrir au Dieu d’Israël les parfums et les holocaustes dans le sanctuaire. 8Aussi, l’Eternel s’est mis en colère contre Juda et Jérusalem et a fait de notre peuple un exemple terrifiant et un sujet de raillerie, et de notre pays une étendue désolée, comme vous le constatez vous-mêmes. 9Car nos pères sont tombés par l’épée, nos fils, nos filles et nos femmes ont été emmenés en captivité à cause de cela. 10C’est pourquoi j’ai décidé de conclure une alliance avec l’Eternel, le Dieu d’Israël, pour qu’il détourne de nous son ardente colère. 11Maintenant, mes amis, ne vous dérobez pas, car c’est vous que l’Eternel a choisis pour vous tenir devant lui, à son service, pour célébrer son culte et brûler des parfums en son honneur.

12Alors les lévites suivants se mirent à l’œuvre : Mahath, fils d’Amasaï, Joël, fils d’Azaria, de la lignée des Qehatites ; de la lignée de Merari ce furent Qish, fils d’Abdi, et Azaria, fils de Yehalléléel ; parmi les Guershonites : Yoah, fils de Zimma, et Eden, fils de Yoah ; 13de la lignée d’Elitsaphân : Shimri et Yeïel ; de la lignée d’Asaph : Zacharie et Mattania. 14De la lignée de Hémân : Yehiel et Shimeï et de celle de Yedoutoun : Shemaya et Ouzziel.

15Ils rassemblèrent les membres de leurs familles respectives et, après s’être rendus rituellement purs, ils allèrent entreprendre la purification du temple de l’Eternel, comme le roi le leur avait ordonné et conformément aux paroles de l’Eternel. 16Les prêtres entrèrent à l’intérieur du temple de l’Eternel pour le purifier, ils jetèrent dans la cour tous les objets impurs qu’ils y trouvèrent. Les lévites les ramassèrent pour les emporter dehors dans la vallée du Cédron. 17Ils commencèrent cette purification le premier jour du premier mois et, le huitième jour du mois, ils en arrivèrent au portique du Temple. Ils mirent huit jours à purifier le temple de l’Eternel. Le seizième jour du premier mois, le travail était terminé.

18Alors ils se rendirent chez le roi Ezéchias et lui dirent : Nous avons purifié tout le temple de l’Eternel, l’autel des holocaustes, tous ses accessoires, et la table des pains exposés devant Dieu avec tous ses accessoires. 19Nous avons préparé et purifié tous les objets que, dans sa rébellion contre l’Eternel, le roi Ahaz avait profanés pendant son règne : ils sont devant l’autel de l’Eternel.

La reconsécration du Temple

20Le lendemain, le roi Ezéchias se leva de grand matin. Il rassembla les dirigeants de la ville et monta au temple de l’Eternel. 21On amena sept taureaux, sept béliers, sept agneaux, ainsi que sept boucs en sacrifice pour le péché, pour le royaume, pour le sanctuaire et pour Juda. Le roi ordonna aux prêtres, de la lignée d’Aaron, de les offrir sur l’autel de l’Eternel. 22Les prêtres égorgèrent le gros bétail, recueillirent le sang des victimes et le répandirent sur l’autel. Ils égorgèrent de même les béliers et en répandirent le sang sur l’autel. Ils égorgèrent les agneaux et en répandirent le sang sur l’autel29.22 Selon l’ordre de Lv 1.3-5.. 23Ensuite on fit approcher les boucs destinés au sacrifice pour le péché devant le roi et devant l’assemblée. Ceux-ci posèrent leurs mains sur eux. 24Les prêtres les égorgèrent et en répandirent le sang sur l’autel pour l’offrir en sacrifice pour le péché, et accomplir ainsi le rite d’expiation pour tout Israël. Car le roi avait précisé que l’holocauste et le sacrifice pour le péché devaient être offerts pour tout Israël. 25Il fit placer les lévites dans la cour du temple de l’Eternel avec des cymbales, des luths et des lyres, selon la règle fixée par David, par Gad, le prophète du roi, et par le prophète Nathan, car c’était un commandement de l’Eternel transmis par l’intermédiaire de ses prophètes. 26Les lévites prirent place avec les instruments de musique de David, et les prêtres tenaient à la main les trompettes. 27Ezéchias ordonna d’offrir l’holocauste sur l’autel ; et, au moment où commença l’holocauste, retentit aussi le chant en l’honneur de l’Eternel accompagné des trompettes et des instruments de David, roi d’Israël. 28Toute l’assemblée se prosterna, le chœur chanta et les trompettes résonnèrent jusqu’à ce qu’on ait terminé d’offrir l’holocauste. 29Quand le sacrifice fut terminé, le roi et tous ceux qui étaient avec lui s’inclinèrent et se prosternèrent. 30Puis le roi et les dirigeants dirent aux lévites de louer l’Eternel avec les paroles composées par David et le prophète Asaph. Ils se répandirent en joyeuses louanges, puis ils s’inclinèrent et se prosternèrent.

31Alors Ezéchias reprit la parole et dit : Maintenant que vous avez été reconsacrés à l’Eternel, approchez-vous, amenez les victimes des sacrifices et les offrandes de reconnaissance au temple de l’Eternel.

L’assemblée amena des victimes pour offrir des sacrifices et des offrandes de louange, et tous ceux dont le cœur était généreux offrirent des holocaustes29.31 Dans l’holocauste, l’animal était presque entièrement brûlé sur l’autel : rien ne revenait à l’adorateur. D’où la mention de la générosité du donateur.. 32L’assemblée offrit ainsi en holocauste à l’Eternel soixante-dix taureaux et bœufs, cent béliers et deux cents agneaux. 33On consacra en outre six cents bovins et trois mille moutons. 34Mais les prêtres étaient trop peu nombreux pour dépecer tous ces animaux. Leurs frères les lévites les aidèrent29.34 Les holocaustes pouvaient normalement être préparés et offerts seulement par les prêtres, mais dans ce cas exceptionnel, les lévites les aidèrent. jusqu’à ce que ce travail soit terminé et jusqu’à ce que les autres prêtres se soient tous rendus rituellement purs, car il faut dire que les lévites avaient mis plus d’empressement à se purifier que les prêtres. 35En plus de nombreux holocaustes, il fallait encore brûler la graisse des sacrifices de communion et répandre les coupes de vin accompagnant les holocaustes. Ainsi fut rétabli le culte au temple de l’Eternel. 36Ezéchias et tout le peuple se réjouirent de la manière dont Dieu avait dirigé les choses, car tout cela s’était fait très rapidement.