2 Mbiri 28 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 28:1-27

Ahazi Mfumu ya Yuda

1Ahazi anali ndi zaka makumi awiri pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Iye sanachite zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide kholo lake. 2Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo anawumbanso mafano a chipembedzo cha Abaala. 3Iye amapsereza nsembe ku chigwa cha Hinomu, ndipo anaperekanso ana ake aamuna ngati nsembe yopsereza kutsatira njira zonyansa za mitundu imene Yehova anayithamangitsa pamaso pa Aisraeli. 4Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzerapo mafano, pamwamba pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse waukulu.

5Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu wake anamupereka mʼmanja mwa mfumu ya Aramu. Aaramu anamugonjetsa ndipo anagwira ukapolo anthu ake ambiri napita nawo ku Damasiko.

Yehova anamuperekanso mʼmanja mwa mfumu ya Israeli, imene inamuzunza ndi kumuphera anthu ake ambiri. 6Pa tsiku limodzi, Peka mwana wa Remaliya anapha asilikali 120,000 mu Yuda chifukwa Yuda anasiya Yehova, Mulungu wa makolo awo. 7Zikiri msilikali wa ku Efereimu, anapha Maaseya mwana wa mfumu, Azirikamu woyangʼanira nyumba yaufumu, ndi Elikana wachiwiri kwa mfumu. 8Aisraeli anagwira ukapolo abale awo, akazi, ana aamuna ndi ana aakazi okwanira 200,000. Iwo anafunkhanso katundu wambiri amene anapita naye ku Samariya.

9Koma kumeneko kunali mneneri wa Yehova dzina lake Odedi, ndipo anapita kukakumana ndi gulu lankhondo pamene linabwerera ku Samariya. Iye anawawuza kuti, “Chifukwa Yehova, Mulungu wa makolo anu anakwiyira Ayuda, Iye anawapereka mʼdzanja lanu. Koma inu mwawapha mwaukali, ukali wake wofika mpaka kumwamba. 10Ndipo tsopano mukufuna kuti amuna ndi akazi a ku Yuda ndi ku Yerusalemu akhale akapolo anu. 11Tsono mvereni! Abwezeni abale anu amene mwawagwira ukapolo, pakuti mkwiyo wa Yehova uli pa inu.”

12Tsono atsogoleri ena a ku Efereimu, Azariya mwana wa Yehohanani, Berekiya mwana wa Mesilemoti, Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilayi anatsutsana nawo amene ankachokera ku nkhondo kuja. 13Iwo anati, “Musabweretse akapolowo kuno, pakuti ife tidzakhala olakwa pamaso pa Yehova. Kodi mukufuna kuwonjezera pa machimo athu ndi kulakwa kwathu? Pakuti zolakwa zathu ndi zambiri kale ndipo mkwiyo wake woopsa uli pa Israeli.”

14Kotero asilikali aja anawasiya akapolowo pamodzi ndi katundu amene analanda ku nkhondo pamaso pa akuluakulu ndi gulu lonse la anthu. 15Anthu amene atchulidwa mayina aja anatenga akapolowo, ndipo kuchokera pa zolanda ku nkhondo, anawaveka onse amene anali maliseche. Anawapatsa zovala ndi nsapato, chakudya ndi chakumwa ndi mankhwala. Onse amene anali ofowoka anawakweza pa abulu. Choncho anabwera nawo kwa abale awo ku Yeriko, Mzinda wa Migwalangwa, ndipo kenaka anawabweza ku Samariya.

16Pa nthawi imeneyo mfumu Ahazi inatumiza mawu kwa mfumu ya ku Asiriya kupempha chithandizo. 17Ankhondo a ku Edomu anabweranso ndi kuthira nkhondo Yuda ndi kugwira akapolo. 18Pamenepo nʼkuti Afilisti atathira nkhondo mizinda ya mʼmbali mwa phiri ndi ku Negevi ku Yuda. Iwo analanda mizindayo nakhala ku Beti-Semesi, Ayaloni ndi Gederoti, komanso Soko, Timna ndi Gimizo pamodzi ndi midzi yawo yozungulira. 19Yehova anapeputsa Yuda chifukwa cha mfumu Ahazi ya Israeli, pakuti analimbikitsa zoyipa ku Yuda ndipo anali munthu wosakhulupirika kwambiri pamaso pa Yehova. 20Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera kwa iye, ndipo anabweretsa mavuto mʼmalo momuthandiza. 21Ahazi anatenga zinthu zochokera mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba yaufumu ndi kwa atsogoleri ndipo anazipereka kwa mfumu ya ku Asiriya, koma zimenezo sizinamuthandize.

22Pa nthawi yake yamavutoyi mfumu Ahazi inapitirira kukhalabe yosakhulupirika pamaso pa Yehova. 23Ahazi ankapereka nsembe kwa milungu ya ku Damasiko, imene inamugonjetsa. Iye ankaganiza kuti, “Popeza milungu ya mafumu a Aaramu yawathandiza, ine ndidzapereka nsembe kwa iyo kuti indithandize.” Koma iyoyo inakhala kugwa kwake ndi kugwa kwa Aisraeli onse.

24Ahazi anasonkhanitsa pamodzi zinthu zonse kuchokera mʼNyumba ya Mulungu ndipo anazitenga. Iye anatseka zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anayimika maguwa ansembe pa ngodya iliyonse ya msewu mu Yerusalemu. 25Mu mzinda uliwonse wa Yuda anamangamo malo achipembedzo, operekerapo nsembe zopsereza kwa milungu ina ndipo anaputa mkwiyo wa Yehova, Mulungu wa makolo ake.

26Zochitika zina pa ulamuliro wake ndi machitidwe ake onse, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli. 27Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mu mzinda wa Yerusalemu, koma sanamuyike mʼmanda a mafumu a Israeli. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

2 Летопись 28:1-27

Ахаз – царь Иудеи

(4 Цар. 16:1-5)

1Ахазу было двадцать лет, когда он стал царём, и правил он в Иерусалиме шестнадцать лет. В отличие от своего предка Довуда, он не делал того, что было правильным в глазах Вечного. 2Он ходил путями царей Исроила и тоже сделал литых идолов для служения Баалу. 3Он приносил огненные жертвы в долине Бен-Гинном и даже сжигал там своих сыновей по омерзительным обычаям народов, которых Вечный прогнал от исроильтян. 4Ахаз приносил жертвы и возжигал благовония в капищах на возвышенностях, на вершинах холмов и под каждым тенистым деревом.

5Поэтому Вечный, его Бог, отдал его в руки царя Сирии. Сирийцы разбили его, взяли много народа в плен и увели их в Дамаск. Ахаз был отдан также в руки царя Исроила, который нанёс ему тяжёлые потери. 6Пеках, сын Ремалии, убил у Иудеи сто двадцать тысяч доблестных воинов в один день, потому что Иудея оставила Вечного, Бога её предков. 7Зихри, могучий воин ефраимит, убил царского сына Маасею, распорядителя дворца Азрикама и Элкану, второго человека после царя. 8Исроильтяне взяли в плен у своих же братьев в Иудее двести тысяч жён, сыновей и дочерей. Они взяли у них и богатую добычу, которую отправили в Сомарию.

Возвращение иудейских пленников

9Но там был пророк Вечного, которого звали Одед. Он вышел навстречу войску, когда оно возвращалось в Сомарию, и сказал им:

– Вечный, Бог ваших предков, разгневался на Иудею и отдал её вам в руки, но вы истребляли её с яростью, которая достигла небес. 10А теперь вы хотите сделать мужчин и женщин Иудеи и Иерусалима своими рабами. Но разве сами вы не грешили против Вечного, вашего Бога? 11Слушайте же меня! Отпустите своих братьев, которых вы взяли в плен, назад, потому что гнев Вечного воспылал на вас.

12Некоторые из вождей Ефраима – Азария, сын Иоханана, Берехия, сын Мешиллемота, Иехизкия, сын Шаллума, и Амаса, сын Хадлая, – предостерегли тех, кто возвращался с войны.

13– Не ведите сюда этих пленников, – сказали они, – иначе мы станем виновны перед Вечным. Вы что, хотите прибавить к нашим грехам и преступлениям и этот? Наша вина и без того велика, и Его гнев воспылал на Исроил.

14Тогда воины отказались от пленников и добычи перед вождями и всем собранием. 15А те, чьи имена были упомянуты, взяли пленников и всех из них, кто был наг, одели из добычи. Они дали им одежду и обувь, снабдили едой и питьём и помазали целебным маслом. Всех, кто ослаб, они посадили на ослов. Они доставили их к их соплеменникам в Иерихон, город Пальм, и вернулись в Сомарию.

Ахаз просит защиты у ассирийцев

(4 Цар. 16:7-20)

16В то время царь Ахаз послал к царю Ассирии, прося о помощи, 17потому что эдомитяне опять пришли, напали на Иудею и увели пленников, 18а филистимляне опустошали города в предгорьях и на юге Иудеи. Они захватили города и поселились в Бет-Шемеше, Аялоне и Гедероте, а также в Сохо, Тимне и Гимзо и в их окрестных поселениях. 19Вечный унизил Иудею из-за Ахаза, царя Исроила28:19 То есть Иудеи; так же в ст. 23, 27. См. сноску на 12:1., потому что тот развратил Иудею и забыл про верность Вечному. 20К нему пришёл Тиглатпаласар28:20 Это Тиглатпаласар III. Он правил с 745 по 727 гг. до н. э., царь Ассирии, но стал притеснять его, вместо того чтобы помочь. 21Ахаз взял сокровища из храма Вечного, из собственного дворца и дворца вождей и выплатил дань царю Ассирии, но это ему не помогло.

22В этой беде царь Ахаз ещё сильнее нарушил верность Вечному. 23Он принёс жертвы богам Дамаска, думая, что это они разбили его, и говорил: «Раз боги царей Сирии помогли им, стану приносить им жертвы, чтобы они помогли и мне». Но они привели к падению и его, и весь Исроил.

24Ахаз собрал утварь храма Всевышнего и порубил её на куски. Он запер двери храма Вечного и устроил жертвенники на всех углах улиц Иерусалима. 25В каждом городе Иудеи он устроил капища, чтобы приносить жертвы чужим богам, и тем самым гневил Вечного, Бога его предков.

26Прочие события его царствования и все его деяния, от первых до последних, записаны в «Книге царей Иудеи и Исроила». 27Ахаз упокоился со своими предками и был похоронен в Иерусалиме, но не был положен в гробницы царей Исроила. И царём вместо него стал его сын Езекия.