2 Mbiri 26 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 26:1-23

Uziya Mfumu ya Yuda

1Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake. 2Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.

3Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu. 4Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake. 5Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.

6Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti. 7Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni. 8Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.

9Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo. 10Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.

11Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu. 12Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600. 13Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake. 14Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera. 15Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.

16Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira. 17Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira. 18Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”

19Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake. 20Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.

21Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.

22Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi. 23Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

New International Reader’s Version

2 Chronicles 26:1-23

Uzziah King of Judah

1All the people of Judah made Uzziah king. He was 16 years old. They made him king in place of his father Amaziah. 2Uzziah rebuilt Elath. He brought it under Judah’s control again. He did it after Amaziah joined the members of his family who had already died.

3Uzziah was 16 years old when he became king. He ruled in Jerusalem for 52 years. His mother’s name was Jekoliah. She was from Jerusalem. 4Uzziah did what was right in the eyes of the Lord, just as his father Amaziah had done. 5He tried to obey God during the days of Zechariah. Zechariah taught him to have respect for God. As long as Uzziah obeyed the Lord, God gave him success.

6Uzziah went to war against the Philistines. He broke down the walls of Gath, Jabneh and Ashdod. Then he rebuilt some towns that were near Ashdod. He also rebuilt some other towns where Philistines lived. 7God helped him fight against the Philistines. He also helped him fight against the Meunites and against the Arabs who lived in Gur Baal. 8The Ammonites brought to Uzziah the gifts he required of them. He became famous all the way to the border of Egypt. That’s because he had become very powerful.

9Uzziah built towers in Jerusalem. They were at the Corner Gate, the Valley Gate and the angle of the wall. He made the towers very strong. 10He also built towers in the desert. He dug many wells, because he had a lot of livestock. The livestock were in the western hills and on the plains. Uzziah had people working in his fields and vineyards in the hills and in the rich lands. That’s because he loved the soil.

11Uzziah’s army was well trained. It was ready to march out by military groups according to their numbers. Jeiel and Maaseiah brought them together. Jeiel was the secretary. Maaseiah was the officer. They were under the direction of Hananiah. He was one of the royal officials. 12The total number of family leaders who were over the fighting men was 2,600. 13An army of 307,500 men was under their command. The men were trained for war. They were a powerful force. They helped the king against his enemies. 14Uzziah provided the entire army with shields, spears, helmets, coats of armor, bows, and stones for their slings. 15In Jerusalem he invented machines to be used on the towers and on the corners of city walls. These machines were used by men who shot arrows from the walls. The machines were also used by men to throw large stones from the walls. Uzziah became famous everywhere. God greatly helped him until he became powerful.

16But after Uzziah became powerful, his pride brought him down. He wasn’t faithful to the Lord his God. He entered the Lord’s temple to burn incense on the altar for burning incense. 17Azariah the priest followed him in. So did 80 other brave priests of the Lord. 18They stood up to Uzziah. They said, “Uzziah, it isn’t right for you to burn incense to the Lord. Only the priests are supposed to do that. They are members of the family line of Aaron. They have been set apart to burn incense. So get out of here. Leave the temple. You haven’t been faithful. The Lord God won’t honor you.”

19Uzziah was holding a shallow cup. He was ready to burn incense in it. He became angry. He shouted at the priests in the Lord’s temple. He did it near the altar for burning incense. While he was shouting, a skin disease suddenly broke out on his forehead. 20Azariah the chief priest and all the other priests looked at him. They saw that Uzziah had a skin disease on his forehead. So they hurried him out of the temple. Actually, he himself really wanted to leave. He knew that the Lord was making him suffer.

21King Uzziah had the skin disease until the day he died. He lived in a separate house because he had the disease. And he wasn’t allowed to enter the Lord’s temple. Uzziah’s son Jotham was in charge of the palace. Jotham ruled over the people of the land.

22The other events of Uzziah’s rule from beginning to end were written down by Isaiah the prophet. Isaiah was the son of Amoz. 23Uzziah joined the members of his family who had already died. He was buried near them in a royal burial ground. People said, “He had a skin disease.” Uzziah’s son Jotham became the next king after him.