2 Mbiri 24 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 24:1-27

Yowasi Akonzanso Nyumba ya Mulungu

1Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba. 2Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada. 3Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.

4Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova. 5Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.

6Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”

7Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.

8Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova. 9Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu. 10Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza. 11Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri. 12Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.

13Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa. 14Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.

15Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130. 16Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.

Kuyipa kwa Yowasi

17Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera. 18Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu. 19Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.

20Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’ ”

21Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu. 22Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”

23Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko. 24Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi. 25Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.

26Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu. 27Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

New Russian Translation

2 Паралипоменон 24:1-27

Иоаш – царь Иудеи

(4 Цар. 11:21–12:3)

1Иоашу было семь лет, когда он начал царствовать, и правил он в Иерусалиме сорок лет. Его мать звали Цивия; она была родом из Вирсавии. 2Иоаш делал то, что было правильным в глазах Господа, все время, пока был жив священник Иодай. 3Иодай выбрал для него двух жен, и у него родились сыновья и дочери.

Иоаш восстанавливает поврежденный храм

(4 Цар. 12:4-16)

4Спустя некоторое время Иоаш решил восстановить дом Господа. 5Он собрал священников и левитов и сказал им:

– Ходите по городам Иудеи и собирайте со всех израильтян деньги, которые должны ежегодно поступать на поддержание дома вашего Бога. Смотрите, не мешкайте.

Но левиты не стали спешить. 6Тогда царь призвал первосвященника Иодая и сказал ему:

– Почему ты не требуешь от левитов, чтобы они приносили от Иудеи и Иерусалима налог, установленный слугой Господа Моисеем, и обществом Израиля для скинии свидетельства?24:6 См. Исх. 30:11-16.

7(Сыновья нечестивой Аталии повредили Божий дом и даже использовали его священную утварь в служении Баалам.)

8По повелению царя был изготовлен ящик, который поставили снаружи, у ворот Господнего дома. 9Затем по Иудее и Иерусалиму было объявлено, чтобы они приносили Господу дань, которую установил для израильтян в пустыне Божий слуга Моисей. 10Все приближенные и весь народ с радостью приносили деньги и бросали их в ящик, пока он не наполнился. 11Всякий раз, когда левиты приносили ящик к царским чиновникам и те видели, что в нем много денег, царский писарь и поверенный первосвященника приходили и опустошали ящик, и его снова относили на место. Они делали это постоянно и собрали много денег. 12Царь и Иодай отдали их людям, которые исполняли работу по дому Господа. Они наняли каменщиков и плотников, чтобы обновить дом Господа, и мастеров по работе с железом и бронзой, чтобы восстановить дом.

13Рабочие трудились усердно, и работа спорилась у них в руках. Они восстановили Божий дом по его первоначальному замыслу и укрепили его. 14Завершив работу, они принесли оставшиеся деньги царю и Иодаю, и на них была изготовлена утварь для дома Господа: утварь для службы и для всесожжений, а еще блюда и другие вещи из золота и серебра. Пока Иодай был жив, в доме Господа постоянно совершались всесожжения.

15Иодай состарился и насытился жизнью. Он умер в возрасте ста тридцати лет. 16Его похоронили с царями в Городе Давида, ради добра, которое он сделал в Израиле для Бога и для Его дома.

Иоаш отворачивается от Господа

(4 Цар. 12:17-21)

17После смерти Иодая вожди Иудеи явились на поклон к царю, и он стал прислушиваться к их советам. 18Они оставили дом Господа, Бога своих предков, и стали служить столбам Ашеры и идолам. За их вину на Иудею и Иерусалим обрушился Божий гнев. 19Хотя Господь посылал к народу пророков, чтобы обратить их к Себе, и хотя пророки свидетельствовали против них, те их не слушали.

20Тогда Дух Божий сошел на24:20 Букв.: «облекся». Захарию, сына священника Иодая. Он встал перед народом и сказал:

– Так говорит Бог: «Почему вы нарушаете повеления Господа? Не будет вам успеха. Раз вы оставили Господа, то и Он оставит вас».

21Но они составили против него заговор и, по приказу царя, его забили камнями до смерти во дворе Господнего дома. 22Царь Иоаш не вспомнил о милости, оказанной ему отцом Захарии Иодаем, и убил его сына, который сказал умирая:

– Пусть Господь увидит и взыщет.

23В конце года на Иоаша двинулось войско Арама. Оно вторглось в Иудею и в Иерусалим и перебило всех правителей народа. Арамеи отослали всю добычу своему царю в Дамаск. 24Хотя войско Арама было немногочисленным, Господь отдал в их руки гораздо более сильное войско. Так как они оставили Господа, Бога своих отцов, над Иоашем свершился приговор. 25Уходя, арамеи оставили Иоаша сильно израненным. Его приближенные составили против него заговор за убийство сына священника Иодая и убили его в постели. Он умер и был похоронен в Городе Давида, но не в царских гробницах.

26В заговоре против него состояли Завад24:26 Завад – вариант имени Иозавад (см. 4 Цар. 12:21)., сын аммонитянки Шимеаты, и Иегозавад, сын моавитянки Шимриты24:26 Шимрита – вариант имени Шомера (4 Цар. 12:21).. 27Рассказ о его сыновьях, многочисленные пророчества против него и рассказ о восстановлении24:27 Букв.: «об основании». дома записаны в «Толкованиях к Книге царей». Амасия, его сын, стал царем вместо него.