2 Mbiri 23 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 23:1-21

1Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri. 2Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu, 3msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu.

Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide. 4Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo, 5ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova. 6Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula. 7Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”

8Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite. 9Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu. 10Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.

11Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”

12Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko. 13Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”

14Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,” 15choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.

16Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova. 17Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.

18Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira. 19Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.

20Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka, 21ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.

La Bible du Semeur

2 Chroniques 23:1-21

Joas devient roi

1La septième année23.1 En 835 av. J.-C., le prêtre Yehoyada s’arma de courage et fit venir les chefs des « centaines23.1 Une unité militaire comprenant peut-être quelques dizaines de soldats. » : Azaria, fils de Yeroham, Ismaël, fils de Yohanân, Azaria, fils d’Obed, Maaséya, fils d’Adaya, et Elishaphath, fils de Zikri, et il fit un pacte avec eux. 2Les officiers parcoururent le royaume de Juda et rassemblèrent les lévites de toutes les villes de Juda et les chefs des groupes familiaux d’Israël, puis ils revinrent avec eux à Jérusalem, 3et toute cette assemblée conclut une alliance avec le jeune roi dans le Temple. Yehoyada leur dit : Voici le fils du roi, il régnera conformément à la promesse que l’Eternel a faite au sujet des descendants de David23.3 Voir 1 Ch 17.10-14 ; 2 Ch 6.16 ; 7.18 ; 2 S 7.16.. 4Voici ce que vous allez faire : ce prochain sabbat, l’une de vos compagnies sera de service ; en qualité de prêtres et de lévites, un tiers d’entre eux gardera les entrées, 5un autre tiers surveillera le palais royal, la troisième section se tiendra en faction à la porte de Yesod. Tout le peuple occupera le parvis du temple de l’Eternel. 6Personne ne doit pénétrer dans le temple de l’Eternel, excepté les prêtres et les lévites de service qui pourront y entrer puisqu’ils sont saints. Tout le monde doit respecter le rituel prescrit par l’Eternel. 7Les lévites entoureront le roi de tous les côtés, chacun les armes à la main. Quiconque voudra forcer l’accès au Temple sera mis à mort. Vous accompagnerez le roi dans toutes ses allées et venues.

8Les lévites et tous les Judéens exécutèrent ponctuellement tous les ordres que le prêtre Yehoyada leur avait donnés. Ils prirent chacun leurs hommes, ceux qui commençaient leur service le jour du repos et ceux qui le terminaient ce jour-là, car le prêtre Yehoyada n’avait donné congé à aucune des classes de lévites. 9Le prêtre Yehoyada remit aux chefs de « centaines » les lances ainsi que les grands et les petits boucliers du roi David qui se trouvaient dans le Temple. 10Il posta tous les hommes en demi-cercle, chacun son javelot à la main, en demi-cercle devant l’édifice, depuis l’angle sud-est du Temple jusqu’à l’angle nord-est, près de l’autel, de manière à entourer le roi. 11Alors on fit sortir le fils du roi, on plaça la couronne sur sa tête et on lui remit l’acte de l’alliance. On le sacra roi : Yehoyada et ses fils l’oignirent d’huile et ils crièrent : Vive le roi !

La mort d’Athalie

12Athalie entendit le bruit du peuple qui accourait et acclamait le roi. Elle vint au milieu de la foule au temple de l’Eternel, 13regarda et vit le roi qui se tenait debout sur son estrade à l’entrée du sanctuaire. Il était entouré des capitaines de la garde et des joueurs de trompette. Toute la population exultait de joie tandis qu’on sonnait des trompettes et que les musiciens, accompagnés de leurs instruments, dirigeaient les chants de louanges. A ce spectacle, Athalie déchira ses vêtements et dit : C’est un complot ! C’est un complot !

14Alors le prêtre Yehoyada fit avancer les chefs de « centaines » qui commandaient l’armée et leur ordonna : Faites-la sortir de l’enceinte du Temple entre les rangs ! Et si quelqu’un la suit, qu’il soit mis à mort. Car, dit le prêtre, ne la mettez pas à mort dans l’enceinte du temple de l’Eternel.

15Ils s’emparèrent donc d’Athalie et la menèrent vers le palais royal par l’entrée de la porte des chevaux : c’est là qu’ils la mirent à mort.

Joas monte sur le trône

16Yehoyada conclut entre lui, tout le peuple et le roi une alliance qui les engageait à être le peuple de l’Eternel. 17Toute la population se rendit au temple de Baal et le démolit. On mit en pièces ses autels et ses statues, et l’on tua devant les autels Mattân, le prêtre de Baal. 18Yehoyada confia la surveillance du temple de l’Eternel aux prêtres-lévites que David avait répartis pour le service du temple de l’Eternel, afin d’offrir des holocaustes à l’Eternel, conformément aux prescriptions de la Loi de Moïse, dans la joie, et en chantant les cantiques composés par David. 19Il installa les portiers aux entrées du temple de l’Eternel pour en interdire l’entrée à toute personne rituellement impure, pour quelque raison que ce soit. 20Il rassembla les chefs de « centaines », les notables, les dirigeants du peuple, ainsi que toute la population du pays, et il fit descendre le roi du Temple au palais royal par la porte supérieure. On installa le roi sur le trône du royaume. 21Tout le peuple du pays était dans la joie, et le calme régnait dans la ville maintenant qu’on avait fait mourir Athalie.