2 Mbiri 20 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 20:1-37

Yehosafati Agonjetsa Mowabu ndi Amoni

1Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.

2Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi). 3Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya. 4Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.

5Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano 6ndipo anati:

“Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu. 7Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya? 8Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati, 9‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’

10“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge. 11Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu. 12Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”

13Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.

14Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.

15Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu. 16Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli. 17Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’ ”

18Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova. 19Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.

20Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.” 21Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti:

“Yamikani Yehova

pakuti chikondi chake ndi chosatha.”

22Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa. 23Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.

24Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa. 25Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge. 26Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.

27Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo. 28Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.

29Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli. 30Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.

Kutha kwa Ufumu wa Yehosafati

31Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili. 32Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova. 33Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.

34Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.

35Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri. 36Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi, 37Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.

La Bible du Semeur

2 Chroniques 20:1-37

Une armée ennemie marche sur Juda – la prière de Josaphat

1Par la suite, les Moabites et les Ammonites20.1 Pour les Moabites et les Ammonites, voir note Gn 19.37, 38. renforcés par des Maonites20.1 D’après certains manuscrits de l’ancienne version grecque ; le texte hébreu traditionnel a : Ammonites. Habitants de Maôn, au sud d’Edom (Jos 15.55 ; 2 Ch 20.10, 22-23 ; 26.7). se mirent en route pour faire la guerre à Josaphat. 2On vint prévenir Josaphat en ces termes : Une vaste armée est en train de marcher contre toi d’au-delà de la mer Morte et d’Edom20.2 D’après un manuscrit hébreu, une ancienne version latine et le contexte géographique. La plupart des manuscrits hébreux, l’ancienne version grecque et la Vulgate ont : la Syrie. Les deux noms se ressemblent en hébreu et se confondent facilement.. Elle a déjà atteint Hatsatsôn-Tamar (c’est-à-dire Eyn-Guédi).

3Josaphat prit peur et décida de consulter l’Eternel. Il proclama un jeûne pour tout Juda, 4et les Judéens se rassemblèrent pour implorer le secours de l’Eternel. Ils vinrent de toutes les villes de Juda. 5Josaphat se tint debout avec l’assemblée des gens de Juda et de Jérusalem dans le temple de l’Eternel, en face du nouveau parvis. 6Il pria ainsi : Eternel, Dieu de nos ancêtres, n’es-tu pas Dieu, habitant dans le ciel, et n’est-ce pas toi qui domines sur tous les royaumes des peuples ? Tu disposes de force et de puissance ! Nul ne peut te résister. 7N’est-ce pas toi, notre Dieu, qui as chassé les anciens habitants de ce pays pour faire place à ton peuple Israël, et qui as donné ce pays pour toujours aux descendants d’Abraham, ton ami qui t’aimait20.7 Voir Jc 2.23. ? 8Ils s’y sont établis, ils y ont construit un sanctuaire en ton honneur. Puis ils ont dit : 9« Si un malheur s’abat sur nous : une guerre, un châtiment, une épidémie ou la famine, nous viendrons nous tenir devant ce temple, devant toi, puisque ta présence est établie dans ce sanctuaire, et du fond de notre détresse, nous implorerons ton secours ; alors tu écouteras et tu sauveras20.9 Allusion à la prière de Salomon (6.14-42 ; 7.12-22). ! » 10Eh bien, maintenant, voici que les Ammonites, les Moabites et les habitants des monts de Séir viennent nous attaquer. Quand Israël venait d’Egypte20.10 Voir Nb 20.14-21 ; Dt 2.1-9 qui précisent que ce sont les Edomites qui ont refusé de laisser passer les Israélites sur leur territoire., tu ne lui as pas permis de traverser le pays de ces gens-là et il a fait un détour ; il ne les a pas détruits. 11Et voilà comment ils nous récompensent : ils viennent nous chasser de la propriété que tu nous as attribuée. 12Notre Dieu, n’exerceras-tu pas tes jugements sur eux ? Car nous sommes impuissants pour résister à cette immense armée qui vient nous attaquer et nous ne savons que faire, mais nous tournons nos regards vers toi.

13Tout Juda, femmes et enfants y compris, se tenait debout devant l’Eternel.

La prophétie de Yahaziel

14Alors l’Esprit de l’Eternel vint sur Yahaziel, fils de Zacharie, descendant de Benaya, de Yeïel et de Mattania, un lévite de la lignée d’Asaph20.14 Une famille de musiciens du Temple (voir 1 Ch 15.17)., au milieu de l’assemblée. 15Yahaziel dit : Soyez attentifs, vous tous qui habitez Juda et Jérusalem, et toi aussi, roi Josaphat ! Voici ce que vous déclare l’Eternel : « Ne craignez rien et ne vous laissez pas effrayer devant cette immense armée, car cette guerre n’est pas votre affaire, c’est celle de Dieu. 16Demain matin, marchez contre eux. Ils vont gravir la montée de la Fleur. Vous les rencontrerez au bout du défilé à l’entrée du désert de Yerouel20.16 Partie du désert de Juda qui s’étendait entre la mer Morte et Teqoa. La montée de la Fleur était un sentier sinueux taillé dans le roc, débouchant à l’ouest de Teqoa. C’était le seul accès de Jérusalem depuis Eyn-Guédi.. 17Vous n’aurez même pas à combattre ; contentez-vous de prendre position et de vous tenir là : vous verrez l’Eternel vous accorder la délivrance. Gens de Juda et de Jérusalem, ne craignez rien et ne vous laissez pas effrayer ! Demain, marchez à leur rencontre, et l’Eternel sera avec vous20.17 Voir Dt 20.1-4. ! »

18Josaphat se prosterna le visage contre terre et tout Juda et les habitants de Jérusalem se laissèrent tomber devant l’Eternel et se prosternèrent devant lui. 19Alors les lévites qehatites et qoréites20.19 Familles de lévites consacrées au chant sacré et à la musique (1 Ch 6.16-23 ; Ps 42.1). se levèrent pour louer l’Eternel, le Dieu d’Israël, en chantant d’une voix très forte.

La délivrance

20Le lendemain matin, ils se levèrent tôt, et les hommes se mirent en route pour le désert de Teqoa20.20 Au sud de Bethléhem (voir 2 S 14.2).. Au moment du départ, Josaphat leur adressa la parole : Ecoutez-moi, hommes de Juda et habitants de Jérusalem ! Faites confiance à l’Eternel votre Dieu, et vous serez invulnérables ! Faites confiance à ses prophètes, et vous aurez la victoire !

21Il s’était concerté avec le peuple et avait placé en tête de l’armée des musiciens pour louer l’Eternel et la majesté de sa sainte personne. Ils se mirent en route devant les soldats en armes en chantant :

Louez l’Eternel,

car son amour ╵dure à toujours.

22Au moment où ils entonnèrent leurs cantiques de louange, l’Eternel plaça une embuscade contre les Ammonites, les Moabites et les habitants des monts de Séir qui venaient attaquer Juda, de sorte qu’ils furent battus. 23Les Ammonites et les Moabites se dressèrent contre les habitants des monts de Séir et les exterminèrent. Quand ils en eurent terminé avec eux, ils se jetèrent les uns sur les autres, jusqu’à s’anéantir.

24Lorsque les Judéens parvinrent au promontoire d’où l’on apercevait le désert, ils regardèrent du côté de leurs ennemis et ils ne virent que des cadavres jonchant le sol : il n’y avait aucun rescapé.

25Josaphat et son armée allèrent s’emparer du butin ; ils trouvèrent en abondance toutes sortes de biens, des vêtements20.25 D’après certains manuscrits hébreux et la Vulgate. Les autres manuscrits hébreux ont : des cadavres. et des objets précieux. Ils en ramassèrent une telle quantité qu’ils ne purent tout emporter. Ils restèrent trois jours à piller le butin tant il était abondant. 26Le quatrième jour, ils s’assemblèrent dans la vallée de la Bénédiction où ils bénirent l’Eternel ; c’est pourquoi on a appelé cet endroit vallée de la Bénédiction, nom qu’il porte encore aujourd’hui.

27Tous les hommes de Juda et de Jérusalem reprirent joyeusement le chemin de la ville, Josaphat en tête, car l’Eternel les avait remplis de joie en les délivrant de leurs ennemis. 28Ils arrivèrent à Jérusalem au son des luths, des lyres et des trompettes et se rendirent au temple de l’Eternel. 29Tous les autres peuples furent frappés de terreur à cause de l’Eternel lorsqu’ils apprirent comment il avait combattu les ennemis d’Israël. 30Dès lors, le royaume de Josaphat jouit de la tranquillité et son Dieu lui assura la paix sur toutes ses frontières.

La fin du règne de Josaphat – alliance coupable et échec

(1 R 22.41-51)

31Ainsi régna Josaphat sur Juda. Il était âgé de trente-cinq ans à son avènement, et il régna vingt-cinq ans à Jérusalem. Sa mère s’appelait Azouba, elle était fille de Shilhi. 32Il suivit l’exemple de son père Asa sans en dévier, en faisant ce que l’Eternel considère comme juste. 33Cependant, les hauts lieux ne disparurent pas : le peuple n’avait toujours pas attaché fermement son cœur au Dieu de ses ancêtres.

34Les autres faits et gestes de Josaphat, des premiers aux derniers, sont cités dans les Actes de Jéhu, fils de Hanani, qui ont été insérés dans le livre des rois d’Israël.

35Après cela, Josaphat, roi de Juda, s’allia avec Ahazia, roi d’Israël, dont la conduite n’était pas conforme à la volonté de Dieu. 36Ils se mirent ensemble pour construire des navires au long cours. Ils fabriquèrent ces navires dans le port d’Etsyôn-Guéber. 37Alors Eliézer, fils de Dodavahou, de Marésha, adressa à Josaphat la prophétie suivante : Parce que tu t’es allié à Ahazia, l’Eternel va détruire tes réalisations.

Effectivement, les navires furent brisés avant d’avoir pu atteindre Tarsis20.37 Tarsis: généralement compris comme un port d’Espagne. Mais il est peu probable que des navires partant d’Etsyôn-Guéber, port du golfe d’Aqaba menant à la mer Rouge, aient pu prendre la direction de l’Espagne. L’expression « aller à Tarsis » était-elle devenue une formule idiomatique pour dire « aller au bout du monde » ?.