2 Mbiri 19 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 19:1-11

1Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, 2mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu. 3Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”

Yehosafati Asankha Oweruza

4Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo. 5Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda. 6Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo. 7Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”

8Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu. 9Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova. 10Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.

11“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”

La Bible du Semeur

2 Chroniques 19:1-11

Le reproche du prophète Jéhu

1Josaphat, roi de Juda, revint sain et sauf chez lui à Jérusalem. 2Jéhu, fils du prophète Hanani19.2 Voir 16.7-9., sortit à sa rencontre et lui dit : Penses-tu qu’il soit juste de prêter ton concours à un homme malfaisant et de s’allier avec ceux qui haïssent l’Eternel ? Parce que tu as fait cela, l’Eternel est en colère contre toi. 3Cependant, il y a du bon en toi, car tu as brûlé les poteaux d’Ashéra du pays et tu t’es résolument attaché à Dieu.

L’organisation de la justice

4Après être demeuré quelque temps à Jérusalem, Josaphat fit une nouvelle tournée parmi le peuple, depuis Beer-Sheva jusqu’à la région montagneuse d’Ephraïm19.4 Au temps de Josaphat, le royaume de Juda était limité au nord par les montagnes d’Ephraïm., pour ramener les Israélites à l’Eternel, le Dieu de leurs ancêtres. 5Il établit des juges dans toutes les villes fortifiées du pays de Juda, 6et leur donna les instructions suivantes : Veillez avec soin à ce que vous faites, car ce n’est pas pour des hommes que vous prononcerez des jugements, mais pour l’Eternel, et il vous assistera lorsque vous rendrez la justice19.6 Sur le rôle des juges, voir Dt 16.18-20 ; 17.8-13 ; Ps 82.. 7Maintenant, ayez la plus grande crainte de l’Eternel et soyez bien circonspects dans tout ce que vous faites, car l’Eternel, notre Dieu, ne tolère ni l’injustice, ni la partialité, ni la corruption par des cadeaux.

8De même à Jérusalem, Josaphat établit quelques-uns des lévites, des prêtres et des chefs de groupe familial d’Israël dans la ville pour rendre la justice au nom de l’Eternel et pour régler les litiges entre les habitants de la ville. 9Voici les ordres qu’il leur donna : Vous remplirez vos fonctions dans la crainte de l’Eternel, pour agir consciencieusement et avec une entière intégrité de cœur. 10Chaque fois que vos compatriotes demeurant dans leurs villes respectives porteront un litige devant vous – qu’il s’agisse d’un meurtre ou d’une contestation au sujet de la Loi, d’un commandement, d’ordonnances ou d’articles de droit – vous les avertirez afin qu’ils ne se rendent pas coupables envers l’Eternel et que l’Eternel ne se mette pas en colère contre vous et contre vos compatriotes. Agissez de cette manière et vous serez irréprochables. 11Pour toutes les affaires religieuses, vous avez à votre tête le grand-prêtre Amaria, et pour les affaires civiles ou royales, c’est Zebadia, fils d’Ismaël, gouverneur de la tribu de Juda. Des lévites seront à votre disposition comme commissaires. Mettez-vous donc courageusement au travail et que l’Eternel assiste ceux qui agissent bien !